Mneneri alikuima pa chipata cha Kachisi, atchula mau akulonjeza ndi akuopsa
1 Mau amene anadza kwa Yeremiya kuchokera kwa Yehova, kuti,
2 Ima m’chipata cha nyumba ya Yehova, lalikira m’menemo mau awa, ndi kuti, Tamvani mau a Yehova, inu nonse a Yuda, amene alowa m’zipata izi kuti mugwadire Yehova.
3 Yehova wa makamu atero, Mulungu wa Israele, Konzani njira zanu ndi machitidwe anu, ndipo ndidzakukhalitsani inu m’malo ano.
4 Musakhulupirire mau onama, kuti, Kachisi wa Yehova, Kachisi wa Yehova, Kachisi wa Yehova ndi awa.
5 Pakuti mukakonzatu njira zanu ndi machitidwe anu; ndi kuweruzatu milandu ya munthu ndi mnansi wake;
6 ndi kuleka kutsendereza mlendo, ndi wamasiye, ndi mkazi wamasiye, osakhetsa mwazi wosachimwa m’malo muno, osatsata milungu ina ndi kudziipitsa nayo;
7 ndipo ndidzakukhazikani inu m’malo muno, m’dziko limene ndinapatsa makolo anu, kuyambira kale lomwe kufikira muyaya.
8 Taonani, mukhulupirira mau onama, osapindulitsa.
9 Kodi mudzapha, ndi kuba, ndi kuchita chigololo, ndi kulumbira zonama, ndi kupereka nsembe kwaBaala, ndi kutsata milungu ina imene simunaidziwa,
10 ndi kudza ndi kuima pamaso panga m’nyumba ino, imene itchedwa dzina langa, ndi kuti, Talanditsidwa; kuti muchite zonyansa izi?
11 Kodi nyumba ino, imene itchedwa dzina langa, ikhala phanga la okwatula pamaso panu? Taona, Ine ndachiona, ati Yehova.
12 Koma pitani tsopano kumalo anga amene anali mu Silo, m’mene ndinaikamo dzina langa poyamba paja, ndi kuona chimene ndinachitira chifukwa cha zoipa za anthu anga Israele.
13 Ndipo tsopano, chifukwa munachita ntchito zonsezi, ati Yehova, ndipo ndinanena kwa inu, ndi kuuka mamawa ndi kunena, koma simunamve; ndipo ndinakuitanani inu, koma simunayankhe;
14 chifukwa chake ndidzaichitira nyumba iyi, imene itchedwa dzina langa, imene mukhulupirirayi, ndipo ndidzachitira malo amene ndinakupatsani inu ndi makolo anu, monga ndinachitira Silo.
15 Ndipo ndidzakuchotsani inu pamaso panga, monga ndinachotsa abale anu onse, mbeu zonse za Efuremu.
16 Chifukwa chake iwe usapempherere anthu awa, usawakwezere iwo mfuu kapena pemphero, usandipembedze; pakuti Ine sindidzakumvera iwe.
17 Kodi suona iwe chimene achichita m’mizinda ya Yuda ndi m’miseu yaYerusalemu?
18 Ana atola nkhuni, atate akoleza moto, akazi akanyanga ufa, kuti aumbe mikate ya mfumu yaikazi ya kumwamba, athirire milungu ina nsembe yothira, kuti autse mkwiyo wanga.
19 Kodi autsa mkwiyo wanga? Ati Yehova; kodi sadziutsira okha manyazi a nkhope zao?
20 Chifukwa chake, ati Ambuye Mulungu, Taonani, mkwiyo wanga ndi ukali wanga udzathiridwa pamalo ano, pa anthu, ndi pa nyama, ndi pa mitengo ya m’munda, ndi pa zipatso zapansi; ndipo udzatentha osazima.
21 Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israele; Ikani zopereka zopsereza zanu pa nsembe zophera zanu, nimudye nyama.
22 Pakuti sindinanena kwa makolo anu, tsiku lija ndinawatulutsa m’dziko la Ejipito, ngakhale kuwauza nsembe zopsereza kapena zophera;
23 koma chinthu ichi ndinawauza, kuti, Mverani mau anga, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu, ndipo inu mudzakhala anthu anga; nimuyende m’njira yonse imene ndakuuzani inu, kuti chikukomereni.
24 Koma sanamvere, sanatchere khutu, koma anayenda mu upo ndi m’kuuma kwa mtima wao woipa, nabwerera chambuyo osayenda m’tsogolo.
25 Chiyambire tsiku limene makolo anu anatuluka m’dziko la Ejipito kufikira lero lino, ndatumiza kwa inu atumiki anga onse, aneneri, tsiku ndi tsiku, kuuka mamawa ndi kuwatumiza iwo;
26 koma sanandimvere Ine sanatchere khutu lao, koma anaumitsa khosi lao; anaipa koposa makolo ao.
27 Ndipo uzinena kwa iwo mau awa onse, koma sadzakumvera iwe; ndipo udzawaitananso; koma sadzakuyankha iwe.
28 Ndipo udzati kwa iwo, Umene ndi mtundu wosamvera mau a Yehova Mulungu wao, wosalola kulangizidwa, choonadi chatha, chadulidwa pakamwa pao.
Zoopsa za Tofeti
29 Meta tsitsi lako, iwe Yerusalemu, nulitaye, nukweze maliro pa mapiri oti see; pakuti Yehova wakana ndi kusiya mbadwo umene aukwiyira.
30 Pakuti ana a Yuda anachita choipa pamaso panga, ati Yehova; naika zonyansa zao m’nyumba yotchedwa dzina langa, kuti aliipitse.
31 Namanga akachisi a ku Tofeti, kuli m’chigwa cha mwana wa Hinomu, kuti atenthe m’moto ana ao aamuna ndi aakazi; chimene sindiwanauze iwo, sichinalowe m’mtima mwanga.
32 Chifukwa chake, taonani, masiku alikudza, ati Yehova, ndipo sadzatchedwanso Tofeti, kapena Chigwa cha mwana wa Hinomu, koma Chigwa cha Kuphera; pakuti adzataya mu Tofeti, kufikira malo akuikamo adzasowa.
33 Ndipo mitembo ya anthu awa idzakhala zakudya za mbalame za mlengalenga, ndi za zilombo za dziko lapansi; palibe amene adzaziopsa.
34 Ndipo ndidzaletsa m’mizinda ya Yuda, ndi m’miseu ya Yerusalemu, mau akukondwa ndi mau akusekera, ndi mau a mkwati ndi mau a mkwatibwi; pakuti dziko lidzasanduka bwinja.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/7-f163bd0fafc7b42eaaf2c7dee0a0d9e3.mp3?version_id=1068—