Mbiya ya woumba. Anthu osalapa
1 Mau amene anadza kwa Yeremiya kuchokera kwa Yehova, kuti,
2 Tauka, tatsikira kunyumba ya woumba, pamenepo ndidzakumvetsa mau anga.
3 Ndipo ndinatsikira kunyumba ya woumba, ndipo, taonani, anaumba ntchito yake ndi njinga.
4 Ndipo pamene mbiya alikuiumba ndi dothi inaonongeka m’dzanja la woumba, anaiumbanso mbiya ina, monga kunamkomera woumba kuiumba.
5 Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, kuti,
6 Nyumba ya Israele inu, kodi sindingathe kuchita ndi inu monga woumba uyu? Ati Yehova. Taonani, monga dothi m’dzanja la woumba, momwemo inu m’dzanja langa, nyumba ya Israele.
7 Mphindi imene ndidzanena za mtundu wa anthu, kapena za ufumu, kuti ndizule ndi kupasula ndi kuononga;
8 ngati mtundu umene, ndaunenera, udzatembenuka kuleka choipa chao, ndidzaleka choipacho ndidati ndiwachitire.
9 Ndipo mphindi imene ndikanenera mtundu, ndi ufumu, kuti ndimangitse mudzi wake ndi kuuoka;
10 koma ukachita choipa pamaso panga, osamvera mau anga, pamenepo ndidzaleka chabwinocho, ndidati ndiwachitire.
11 Tsopano nenatu kwa anthu a Yuda, ndi kwa okhala m’Yerusalemu, kuti, Atero Yehova: Taonani, Ine ndipangira inu choipa, ndilingalira inu kanthu kakuchitira inu choipa; mubwerere tsono inu nonse, yense kunjira yake yoipa, nimukonze njira zanu ndi machitidwe anu.
12 Koma iwo ati, Palibe chiyembekezero; pakuti ife tidzatsata zilingaliro zathu, ndipo tidzachita yense monga mwa kuuma kwa mtima wake woipa.
13 Chifukwa chake atero Yehova; Funsanitu m’mitundu, ndani wamva zotero; namwali wa Israele wachita chinthu choopsetsa kwambiri.
14 Kodi matalala a Lebanoni adzalephera pamwala wa m’munda? Kodi adzaphwa madzi ozizira otsika kutali?
15 Pakuti anthu anga andiiwala Ine, afukizira zopanda pake; aphunthwitsa iwo m’njira zao, m’njira zakale, kuti ayende m’njira za m’mbali, m’njira yosatundumuka;
16 kuti aliyense dziko lao likhale lodabwitsa, ndi kutsonya chitsonyere; yense wakupitapo adzadabwa, ndi kupukusa mutu wake.
17 Ndidzamwazamwaza iwo monga ndi mphepo ya kum’mawa pamaso pa adani; ndidzayang’anira pamsana pao, si nkhope yao, tsiku la Tsoka lao.
18 Ndipo iwo anati, Tiyeni, tilingalire Yeremiya chomchitira choipa; pakuti chilamulo sichidzathera wansembe, kapena uphungu wanzeru, kapena maumneneri. Tiyeni, timpande iye ndi lilime, tisamvere iye mau ake ali onse.
19 Mundimvere ine, Yehova, mumve mau a iwo akulimbana ndi ine.
20 Kodi choipa chibwezedwe pa chabwino? Pakuti akumbira moyo wanga dzenje. Mukumbukire kuti ndinaima pamaso panu kuwanenera zabwino, kuwachotsera iwo ukali wanu.
21 Chifukwa chake mupereke ana ao kunjala, mupereke iwo kumphamvu ya lupanga; akazi ao akhale opanda ana, ndi amasiye; amuna ao aphedwe ndi imfa, ndi anyamata ao apandidwe ndi lupanga kunkhondo.
22 Mfuu umvekedwe m’nyumba zao, pamene muwatengera khamu la nkhondo dzidzidzi; pakuti akumba dzenje lakundigwira ine, anabisira mapazi anga misampha.
23 Koma, Yehova, mudziwa uphungu wao wonse wakundinenera ine kundipha ine; musakhulukire mphulupulu yao, musafafanize tchimo lao pamaso panu; aphunthwitsidwe pamaso panu; muchite nao m’nthawi ya mkwiyo wanu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/18-d1575486fef31cc1ed71d41dbd7d22ef.mp3?version_id=1068—