Categories
YEREMIYA

YEREMIYA 34

Zedekiya adzatengedwa, Yerusalemu adzalandidwa

1 Mau amene anadza kwa Yeremiya kuchokera kwa Yehova, pamene Nebukadinezara mfumu ya Babiloni, ndi nkhondo yake yonse, ndi maufumu onse a dziko lapansi amene anagwira mwendo wake, ndi anthu onse, anamenyana ndiYerusalemu, ndi mizinda yake yonse, akuti,

2 Yehova Mulungu wa Israele atero, Pita, nena kwa Zedekiya mfumu ya Yuda, numuuze iye, kuti Yehova atero, Taona, ndidzapereka mzindawu m’dzanja la mfumu ya ku Babiloni, ndipo adzautentha ndi moto;

3 ndipo iwe sudzapulumuka m’dzanja lake, koma udzagwiridwadi, nudzaperekedwa m’dzanja lake; ndipo maso ako adzaonana nao a mfumu ya ku Babiloni, ndipo iye adzanena nawe pakamwa ndi pakamwa, ndipo udzanka ku Babiloni.

4 Koma tamva mau a Yehova, iwe Zedekiya mfumu ya Yuda; Yehova atero za iwe, Sudzafa ndi lupanga;

5 udzafa ndi mtendere; ndipo adzawambika iwe monga anawambika makolo ako, mafumu akale usanakhale iwe; ndipo adzakulirira iwe, kuti, Kalanga ine ambuye! Pakuti ndanena mau, ati Yehova.

6 Ndipo Yeremiyamneneriananena mau onsewa kwa Zedekiya mfumu ya Yuda mu Yerusalemu,

7 pamene nkhondo ya mfumu ya ku Babiloni inamenyana ndi Yerusalemu, ndi mizinda yonse ya Yuda imene inatsala, ndi Lakisi ndi Azeka; pakuti mizinda ya Yuda yamalinga yotsala ndi imeneyi.

Oyesa abale ao akapolo aopsedwa

8 Mau amene anadza kwa Yeremiya kuchokera kwa Yehova, mfumu Zedekiya atapangana pangano ndi anthu onse amene anali pa Yerusalemu, kuti awalalikire iwo ufulu;

9 kuti yense ammasule kapolo wake wamwamuna, ndi wamkazi, pokhala iye Muhebri wamwamuna kapena wamkazi, kuti yense asayese Myuda mnzake kapolo wake;

10 ndipo akulu onse ndi anthu onse anamvera, amene anapangana mapangano, akuti yense ammasule kapolo wake wamwamuna, kapena wamkazi osawayesanso akapolo; iwo anamvera nawamasula;

11 koma pambuyo pake anabwerera, nabweza akapolo ake aamuna ndi aakazi, amene anawamasula, nawagonjetsanso akhale akapolo aamuna ndi aakazi;

12 chifukwa chake mau a Yehova anadza kwa Yeremiya kuchokera kwa Yehova, kuti,

13 Yehova Mulungu wa Israele atero: Ndinapangana mapangano ndi makolo anu tsiku lija ndinawatulutsa m’dziko la Ejipito, kutuluka m’nyumba ya ukapolo, kuti,

14 Zitapita zaka zisanu ndi ziwiri mudzaleka amuke yense mbale wake amene ali Muhebri, amene anagulidwa ndi inu, amene anakutumikirani inu zaka zisanu ndi chimodzi, mudzammasule akuchokereni; koma makolo anu sanandimvere Ine, sananditchere Ine khutu.

15 Ndipo mwabwerera inu tsopano, ndi kuchita chimene chili cholungama pamaso panga, pakulalikira ufulu yense kwa mnzake; ndipo munapangana pangano pamaso panga m’nyumba imene itchedwa dzina langa;

16 koma mwabwerera ndi kuipitsa dzina langa, ndi kubwezera mu ukapolo yense kapolo wake wamwamuna, ndi wamkazi, amene munammasula akachite zao, ndipo munawagonjetsa, akhale akapolo anu aamuna ndi aakazi.

17 Chifukwa chake Yehova atero: Simunandimvere Ine, kuti mulalikire ufulu, munthu yense kwa mbale wake, ndi munthu yense kwa mnzake; taonani, ndilalikira kwa inu ufulu, ati Yehova, wa kulupanga, kumliri, ndi kunjala; ndipo ndidzakuperekani mukhale oopsetsa m’maufumu onse a dziko lapansi.

18 Ndipo ndidzapereka anthu akulakwira pangano langa, amene sanachite mau a pangano limene anapangana pamaso panga, muja anadula pakati mwanawang’ombe ndi kupita pakati pa mbali zake;

19 akulu a Yuda, ndi akulu a Yerusalemu, adindo, ndi ansembe, ndi anthu onse a m’dziko, amene anapita pakati pa mbali za mwanawang’ombe;

20 ndidzapereka iwo m’dzanja la adani ao, ndi m’dzanja la iwo akufuna moyo wao; ndipo mitembo yao idzakhala chakudya cha mbalame za mlengalenga, ndi cha zilombo za padziko lapansi.

21 Ndipo Zedekiya mfumu ya Yuda ndi akulu ake ndidzawapereka m’dzanja la adani ao, ndi m’dzanja la akufuna moyo wao, ndi m’dzanja la nkhondo ya mfumu ya ku Babiloni, imene yakuchokerani.

22 Taonani, ndidzauza, ati Yehova, ndidzabwezera iwo kumzinda uno; ndipo adzamenyana nao, nadzaulanda, nadzautentha ndi moto; ndipo ndidzayesa mizinda ya Yuda mabwinja, palibenso wokhalamo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/34-63113c59ba909ab6a8ae7ebe210f5290.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *