Categories
YEREMIYA

YEREMIYA 45

Mau a Mulungu kwa Baruki

1 Mau amene ananena Yeremiyamnenerikwa Baruki mwana wake wa Neriya, pamene analemba mau awa m’buku ponena Yeremiya, chaka chachinai cha Yehoyakimu mwana wake wa Yosiya, mfumu ya Yuda, ndi kuti,

2 Yehova Mulungu wa Israele atero kwa inu, Baruki:

3 Munati, Kalanga ine tsopano! Pakuti Yehova waonjezera chisoni pa zowawa zanga; ndalema ndi kubuula kwanga, sindipeza kupuma.

4 Uzitero naye, Yehova atero: Taonani, chimene ndamanga ndidzapasula, ndi chimene ndaoka ndidzazula; ndidzatero m’dziko lonseli.

5 Kodi udzifunira wekha zinthu zazikulu? Usazifune; pakuti, taona, ndidzatengera zoipa pa anthu onse, ati Yehova: koma moyo wako ndidzakupatsa iwe ngati chofunkha m’malo monse m’mene mupitamo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/45-0b689bc167264163b21b6bf2565be91d.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *