Mau a Mulungu kwa Baruki
1 Mau amene ananena Yeremiyamnenerikwa Baruki mwana wake wa Neriya, pamene analemba mau awa m’buku ponena Yeremiya, chaka chachinai cha Yehoyakimu mwana wake wa Yosiya, mfumu ya Yuda, ndi kuti,
2 Yehova Mulungu wa Israele atero kwa inu, Baruki:
3 Munati, Kalanga ine tsopano! Pakuti Yehova waonjezera chisoni pa zowawa zanga; ndalema ndi kubuula kwanga, sindipeza kupuma.
4 Uzitero naye, Yehova atero: Taonani, chimene ndamanga ndidzapasula, ndi chimene ndaoka ndidzazula; ndidzatero m’dziko lonseli.
5 Kodi udzifunira wekha zinthu zazikulu? Usazifune; pakuti, taona, ndidzatengera zoipa pa anthu onse, ati Yehova: koma moyo wako ndidzakupatsa iwe ngati chofunkha m’malo monse m’mene mupitamo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/45-0b689bc167264163b21b6bf2565be91d.mp3?version_id=1068—