Categories
DANIELE

DANIELE Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli lidalembedwa pamene Ayuda ankazunzika kwambiri chifukwa cha malamulo ankhanza a mfumu yakunja. Wolemba bukuli alongosola zimene iye adaziwona m’masomphenya; afuna kuwalimbitsa mtima Ayudawo powauza kuti lidzabwera tsiku pamene Mulungu adzaithetsa mphamvu mfumu yoipa ija, mwakuti anthu ake adzapezanso ufulu.

Za m’masomphenyazi zikuwonetsa chiyambi chake ndiponso kutha kwake kwa maufumu angapo, kuyambira ufumu wa Babiloni; ndiponso zikulosa zakuti Mulungu adzawagwetsera pansi mafumu akunja aja ndi kupambanitsa anthu ake.

Bukuli lili ndi zigawo ziwiri: Gawo loyamba ndilo nkhani zokhudza Daniele ndi anzake ena okhala ku ukapolo ku Babiloni. Zikuwonetsa m’mene iwo anapambanira adani awo chifukwa chokhulupirira ndi kumvera Mulungu. Gawo lachiwiri likunena za m’masomphenya osiyanasiyana amene Daniele anawaona.

Za mkatimu

Daniele ndi abwenzi ake

1.1—6.28

Zina ndi zina zimene Daniele adaziwona m’masomphenya

7.1—11.45

a. Nyama zinai

7.1-28

b. Tonde ndi mbuzi

8.1—9.2

7

c. Wamthenga wakumwamba

10.1—11.45

d. Za nthawi yomaliza

12.1-13

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *