Categories
HOSEYA

HOSEYA 7

Kuchimwa ndi kupandukira kwa Israele

1 M’mene ndichiritsa Israele, mphulupulu ya Efuremu ivumbuluka, ndi zoipa za Samariya; pakuti achita bodza, ndipo mkhungu alowa m’nyumba, ndi gulu la mbala lilanda kubwalo.

2 Ndipo sanena m’mtima mwao kuti Ine ndikumbukira zoipa zao zonse; tsopano machitidwe ao awazinga; ali pamaso panga.

3 Akondweretsa mfumu ndi zoipa zao, ndi akalonga ndi mabodza ao.

4 Achigololo onsewo; akunga ng’anjo anaitenthetsa wootcha mkate; aleka kusonkha moto, poyambira kukanda mtanda kufikira watupa mtandawo.

5 Tsiku la mfumu yathu akalonga adzidwalitsa ndi kutentha kwa vinyo; iye anatambasula dzanja lake pamodzi ndi oseka.

6 Pakuti asendera nao mtima wao wakunga ng’anjo ya mkate, pokhala alikulalira; wootcha mkate wao agona usiku wonse, m’mawa iyaka ngati moto wa malawi.

7 Onsewo atentha ngati ng’anjo, natha oweruza ao, agwa mafumu ao onse; palibe mmodzi mwa iwo wakuitana Ine.

8 Efuremu asokonezana nayo mitundu ya anthu; Efuremu ndiye kamtanda ka mkate kosatembenuzidwa.

9 Alendo anatha mphamvu yake osachidziwa iye; imvi zomwe zampakiza osachidziwa iye.

10 Ndipo kudzikuza kwa Israele kumchitira umboni pamaso pake; koma sanabwerere kunka kwa Yehova Mulungu wao, kapena kumfunafuna mwa ichi chonse.

11 Ndipo Efuremu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru; aitanira kwa Ejipito, amuka kwa Asiriya.

12 Pamene amuka ndidzawayalira ukonde wanga, ndidzawagwetsa ngati mbalame za m’mlengalenga, ndidzawalanga monga udamva msonkhano wao.

13 Tsoka kwa iwowa! Pakuti anandizembera; chionongeko kwa iwowa! Pakuti anandilakwira; ndikadawalanditsa Ine, koma anandinenera zabodza.

14 Ndipo sanafuulire kwa Ine ndi mtima wao, koma alira pakama pao, asonkhanira tirigu ndi vinyo, apikisana ndi Ine.

15 Chinkana ndawalangiza ndi lulimbitsa manja ao, andilingiririra choipa.

16 Abwerera, koma si kwa Wam’mwambayo; akunga uta wosakhulupirika; akalonga ao adzagwa ndi lupanga mwa chipongwe cha lilime lao; ichi ndicho adzawasekera m’dziko la Ejipito.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/7-edaf085e77dfdb97f19afedb5273129d.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *