Categories
YOWELE

YOWELE Mau Oyamba

Mau Oyamba

Yowele adalalikira makamaka pa nthawi ya ufumu wa Persiya, koma za moyo wake sitidziwa bwino. Iye akamba za mliri wa dzombe ndi chilala; zimene zaonongeratu mbeu zonse ndi mitengo yomwe. Mneneriyu aona ngati ichi ndi chizindikiro chosonyeza kuti tsiku la Yehova lidzabwera pamene Mulungu adzalanga anthu onse okana malamulo ake. Tsono Yowele akuwapempha anthuwo kuti atembenuke mtima ndi kubwerera kwa Chauta, poyembekeza kuti mwina Mulungu adzawakhulukira ndi kuwadalitsa monga adawalonjezera. Mau ena odziwika ndi akuti lidzafika tsiku pamene Yehova adzatuma mzimu wake pa anthu onse, aamuna ndi aakazi, achikulire ndi achinyamata omwe.

Za mkatimu

Mliri wa dzombe

1.1—2.17

Lonjezo la kukonzedwanso kwa zinthu

2.18-27

Tsiku la Ambuye

2.28—3.21

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *