Categories
YONA

YONA 2

Pemphero la Yona ali m’mimba mwa chinsomba

1 Pamenepo Yona anapemphera kwa Yehova Mulungu wake ali m’mimba mwa nsombayo.

2 Ndipo anati,

Ndinaitana Yehova m’nsautso wanga,

ndipo anandiyankha ine;

ndinafuula ndili m’mimba ya manda,

ndipo munamva mau anga.

3 Pakuti munandiponya mwakuya m’kati mwa nyanja,

ndipo madzi anandizinga;

mafunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.

4 Ndipo ndinati, Ndatayika ndichoke pamaso panu;

koma ndidzapenyanso Kachisi wanu wopatulika.

5 Madzi anandizinga mpaka moyo wanga,

madzi akuya anandizungulira,

kayandeyande wa m’nyanja anandikulunga mutu.

6 Ndinatsikira kumatsinde a mapiri,

mipingiridzo ya dziko inanditsekereza kosatha;

koma munandikwezera moyo wanga

kuuchotsa kuchionongeko, Yehova Mulungu wanga.

7 Pokomoka moyo wanga m’kati mwanga ndinakumbukira Yehova;

ndi pemphero langa linafikira Inu mu Kachisi wanu wopatulika.

8 Iwo osamalira mabodza opanda pake

ataya chifundo chaochao.

9 Koma ine ndidzakupherani Inu nsembe ndi mau akuyamika,

ndidzakwaniritsa chowinda changa.

Chipulumutso ncha Yehova.

10 Pamenepo Yehova analankhula ndi nsombayo, ndipo inamsanzira Yona kumtunda.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JON/2-58e99d0de00220c8f33c33195a6f9d77.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *