Categories
1 YOHANE

1 YOHANE 4

Za aphunzitsi onyenga

1 Okondedwa, musamakhulupirira mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ichokera mwa Mulungu: popeza aneneri onyenga ambiri anatuluka kulowa m’dziko lapansi.

2 M’menemo muzindikira Mzimu wa Mulungu: mzimu uliwonse umene uvomereza kuti YesuKhristuanadza m’thupi, uchokera mwa Mulungu;

3 ndipo mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu suchokera kwa Mulungu; ndipo uwu ndiwo mzimu wa wokana Khristu umene mudamva kuti ukudza; ndipo ulimo m’dziko lapansi tsopano lomwe,

4 Inu ndinu ochokera mwa Mulungu, tiana, ndipo munaipambana; pakuti Iye wakukhala mwa inu aposa iye wakukhala m’dziko lapansi. Iwo ndiwo ochokera m’dziko lapansi;

5 mwa ichi alankhula monga ochokera m’dziko lapansi, ndipo dziko lapansi liwamvera.

6 Ife ndife ochokera mwa Mulungu; iye amene azindikira Mulungu atimvera; iye wosachokera mwa Mulungu satimvera ife. Momwemo tizindikira mzimu wa choonadi, ndi mzimu wa chisokeretso.

Mulungu ndiye chikondi. Za kukonda Mulungu ndi kukondana ndi abale

7 Okondedwa, tikondane wina ndi mnzake: chifukwa kuti chikondi chichokera kwa Mulungu, ndipo yense amene akonda, abadwa kuchokera kwa Mulungu, namzindikira Mulungu.

8 Iye wosakonda sazindikira Mulungu; chifukwa Mulungu ndiye chikondi.

9 Umo chidaoneka chikondi cha Mulungu mwa ife, kuti Mulungu anamtuma Mwana wake wobadwa yekha, alowe m’dziko lapansi, kuti tikhale ndi moyo mwa Iye.

10 Umo muli chikondi, sikuti ife tinakonda Mulungu, koma kuti Iye anatikonda ife, ndipo anatuma Mwana wake akhale chiombolo chifukwa cha machimo athu.

11 Okondedwa, ngati Mulungu anatikonda ife kotero, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake.

12 Palibe munthu adamuona Mulungu nthawi iliyonse; tikakondana wina ndi mnzake, Mulungu akhala mwa ife, ndi chikondi chake chikhala changwiro mwa ife;

13 m’menemo tizindikira kuti tikhala mwa Iye, ndi Iye mwa ife, chifukwa anatipatsako Mzimu wake.

14 Ndipo ife tapenyera, ndipo tichita umboni kuti Atate anatuma Mwana akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi.

15 Iye amene adzavomereza kuti Yesu ali Mwana wa Mulungu, Mulungu akhala mwa iye, ndi iye mwa Mulungu.

16 Ndipo ife tazindikira, ndipo takhulupirira chikondicho Mulungu ali nacho pa ife. Mulungu ndiye chikondi, ndipo iye amene akhala m’chikondi akhala mwa Mulungu, ndipo Mulungu akhala mwa iye.

17 M’menemo chikondi chathu chikhala changwiro kuti tikhale nako kulimbika mtima m’tsiku la mlandu; chifukwa monga Iyeyu ali, momwemo tili ife m’dziko lino lapansi.

18 Mulibe mantha m’chikondi; koma chikondi changwiro chitaya kunja mantha, popeza mantha ali nacho chilango, ndipo wamanthayo sakhala wangwiro m’chikondi.

19 Tikonda ife, chifukwa anayamba Iye kutikonda.

20 Munthu akati, kuti, Ndikonda Mulungu, nadana naye mbale wake, ali wabodza: pakuti iye wosakonda mbale wake amene wamuona, sangathe kukonda Mulungu amene sanamuone.

21 Ndipo lamulo ili tili nalo lochokera kwa Iye, kuti iye amene akonda Mulungu akondenso mbale wake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1JN/4-6f5ecc11d939af64088c71f141d45125.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *