Categories
MATEYU

MATEYU 2

Anzeru a kum’mawa

1 Ndipo pa kubadwa kwake kwa Yesu mu Betelehemu wa Yudeya m’masiku aHerodemfumu, onani, Anzeru a kum’mawa anafika kuYerusalemu,

2 nati, Ali kuti amene anabadwa mfumu ya Ayuda? Chifukwa tinaona nyenyezi yake kum’mawa, ndipo tinadzera kudzamlambira Iye.

3 Ndipo Herode mfumuyo pakumva ichi anavutika, ndi Yerusalemu yense pamodzi naye.

4 Ndipo pamene anasonkhanitsa ansembe aakulu onse ndi alembi a anthu, anafunsira iwo, Adzabadwira kutiKhristuyo?

5 Ndipo anamuuza iye, Mu Betelehemu wa Yudeya; chifukwa kunalembedwa kotere ndimneneri, kuti,

6 Ndipo iwe Betelehemu, dziko la Yudeya,

sukhala konse wamng’onong’ono mwa akulu a Yudeya.

Pakuti Wotsogolera adzachokera mwa iwe,

amene adzaweta anthu anga Aisraele.

7 Pomwepo Herode anawaitana Anzeruwo m’tseri, nafunsitsa iwo nthawi yake idaoneka nyenyeziyo.

8 Nawatumiza ku Betelehemu, nati, Yendani mufunitsitse za kamwanako; ndipo pamene mudzampeza, mundibwezere mau, kuti inenso ndidzadze kudzamlambira Iye.

9 Ndipo iwo, m’mene anamva mfumu, anamuka; ndipo onani, nyenyezi ija anaiona kum’mawa, inawatsogolera iwo, kufikira inadza nkuima pamwamba pomwe panali kamwanako.

10 Ndipo iwo poona nyenyeziyo, anakondwera ndi kukondwera kwakukulu.

11 Ndipo pofika kunyumba anaona kamwanako ndi Maria amake, ndipo anagwa pansi namgwadira Iye; namasula chuma chao, nampatsa Iye mitulo, ndiyo golide ndilubanindimure.

12 Ndipo iwo, pochenjezedwa m’kulota kuti asabwerere kwa Herode, anachoka kupita ku dziko lao panjira ina.

Athawira ku Ejipito

13 Ndipo pamene iwo anachoka, onani,mngelowa Ambuye anaonekera kwa Yosefe m’kulota, nati, Tauka, nutenge kamwanako ndi amake, nuthawire ku Ejipito, nukakhale kumeneko kufikira ndidzakuuza iwe; pakuti Herode adzafuna kamwana kukaononga Iko.

14 Ndipo iye ananyamuka natenga kamwana ndi amake usiku, nachoka kupita ku Ejipito;

15 nakhalabe kumeneko kufikira atamwalira Herode; kuti chikachitidwe chonenedwa ndi Ambuye mwa mneneri kuti,

Ndinaitana Mwana wanga atuluke mu Ejipito.

Aphedwa ana mu Betelehemu

16 Pamenepo Herode, poona kuti anampusitsa Anzeruwo, anapsa mtima ndithu, natumiza ena kukaononga tiana tonse ta mu Betelehemu ndi ta m’midzi yake yonse, takufikira zaka ziwiri ndi tating’ono tonse, monga mwa nthawi imeneyo iye anafunsitsa kwa Anzeruwo.

17 Pomwepo chinachitidwa chonenedwa ndi Yeremiya mneneri, kuti,

18 Mau anamveka mu Rama,

maliro ndi kuchema kwambiri;

Rakele wolira ana ake,

wosafuna kusangalatsidwa,

chifukwa palibe iwo.

Abwera kuchokera ku Ejipito

19 Koma pakumwalira Herode, onani, mngelo wa Ambuye anaonekera m’kulota kwa Yosefe mu Ejipito,

20 nati, Tauka, nutenge kamwana ndi amake, nupite kudziko la Israele: chifukwa anafa uja wofuna moyo wake wa kamwanako.

21 Ndipo anauka iye, natenga kamwana ndi amake, nalowa m’dziko la Israele.

22 Koma pakumva iye kutiArkelaoanali mfumu ya Yudeya m’malo mwa atate wake Herode, anachita mantha kupita kumeneko; ndipo pamene anachenjezedwa ndi Mulungu m’kulota, anamuka nalowa kudziko la Galileya,

23 nadza nakhazikika m’mzinda dzina lake Nazarete kuti chikachitidwe chonenedwa ndi aneneri kuti, Adzatchedwa Mnazarayo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/2-b5132ed34898587b8f1d1f99f947b589.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *