Munthu wamanjenje wa ku Kapernao
1 Ndipo Iye analowa m’ngalawa, naoloka, nadza kumzinda kwao.
2 Ndipo onani, anabwera naye kwa Iye munthu wamanjenje, wakugona pamphasa: ndipo Yesu pakuona chikhulupiriro chao, anati kwa wodwalayo, Limba mtima, mwana, machimo ako akhululukidwa.
3 Ndipo onani, ena a alembi ananena mumtima mwao, Uyu achitira Mulungu mwano.
4 Ndipo Yesu, pozindikira maganizo ao, anati, Chifukwa chanji mulinkuganizira zoipa m’mitima yanu?
5 Pakuti chapafupi nchiti, kunena, Machimo ako akhululukidwa; kapena kunena, Tanyamuka. Nuyende?
6 Koma kuti mudziwe kuti ali nazo mphamvuMwana wa Munthupansi pano za kukhululukira machimo (pomwepo ananena kwa wodwalayo), Tanyamuka, nutenge mphasa yako, numuke kunyumba kwako.
7 Ndipo ananyamuka, napita kunyumba kwake.
8 Ndipo m’mene anthu a makamu anachiona, anaopa, nalemekeza Mulungu, wakupatsa anthu mphamvu yotere.
Yesu aitana Mateyu
9 Ndipo Yesu popita, kuchokera kumeneko, anaona munthu, dzina lake Mateyu, alinkukhala polandirira msonkho, nanena kwa iye, Nditsate Ine. Ndipo iye anauka, namtsata.
10 Ndipo panali pamene Iye analinkukhala pachakudya m’nyumba, onani,amisonkhondi ochimwa ambiri anadza nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndiophunziraake.
11 NdipoAfarisi, pakuona ichi, ananena kwa ophunzira ake, Chifukwa ninji Mphunzitsi wanu alinkudya pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?
12 Ndipo m’mene Yesu anamva anati, Olimba safuna sing’anga ai, koma odwala.
13 Koma mukani muphunzire nchiyani ichi, Ndifuna chifundo, si nsembe ai; pakuti sindinadze kudzaitana olungama, koma ochimwa.
Za kusala kudya
14 Pomwepo anadza kwa Iye ophunzira ake a Yohane, nati, Chifukwa ninji ife ndi Afarisi tisala kudya kawirikawiri, koma ophunzira anu sasala?
15 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Nanga anyamata a nyumba ya ukwati angathe kulira kodi nthawi imene mkwati akhala nao? Koma adzafika masiku, pamene mkwati adzachotsedwa kwa iwo, ndipo pomwepo adzasala kudya.
16 Ndipo kulibe munthu aphathika chigamba cha nsalu yaiwisi pa chofunda chakale; pakuti chigamba chake chizomoka kuchofundacho, ndipo chichita chiboo chachikulu.
17 Kapena samathira vinyo watsopano m’matumba akale; akatero, matumba aphulika, ndi vinyo atayika, ndi matumba aonongeka; koma athira vinyo watsopano m’matumba atsopano, ndi zonse ziwiri zisungika.
Mwana wamkazi wa Yairo. Mkazi wokhudza chofunda cha Yesu
18 M’mene Iye analikulankhula nao zinthu zimenezo, onani, anadza munthu mkulu, namgwadira Iye, nanena, Wamwalira tsopanoli mwana wanga wamkazi, komatu mudze muike dzanja lanu pa iye, ndipo adzakhala ndi moyo.
19 Ndipo Yesu ananyamuka namtsata iye, ndi ophunzira ake omwe.
20 Ndipo onani, mkazi, anali ndi nthenda yachidwalire zaka khumi ndi ziwiri, anadza pambuyo pake, nakhudza mphonje ya chofunda chake;
21 pakuti analikunena mwa iye yekha, Ngati ndingakhudze chofunda chake chokha ndidzachira.
22 Koma Yesu potembenuka ndi kuona iye anati, Limba mtima, mwana wamkaziwe, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Ndipo mkaziyo anachira kuyambira nthawi yomweyo.
23 Ndipo Yesu polowa m’nyumba yake ya mkuluyo, ndi poona oimba zitoliro ndi khamu la anthu obuma,
24 ananena, Tulukani, pakuti kabuthuko sikanafe koma kali m’tulo. Ndipo anamseka Iye pwepwete.
25 Koma pamene khamulo linatulutsidwa, Iye analowamo, nagwira dzanja lake; ndipo kabuthuko kadauka.
26 Ndipo mbiri yake imene inabuka m’dziko lonse limenelo.
Yesu achiritsa akhungu awiri ndi wosalankhula
27 Ndipo popita Yesu kuchokera kumeneko, anamtsata Iye anthu awiri akhungu, ofuula ndi kuti, Mutichitire ife chifundo, mwana wa Davide.
28 Ndipo m’mene Iye analowa m’nyumbamo, akhunguwo anadza kwa Iye; ndipo Yesu anati kwa iwo, Mukhulupirira kodi kuti ndikhoza kuchita ichi? Anena kwa Iye, Inde, Ambuye.
29 Pomwepo anakhudza maso ao, nati, Chichitidwe kwa inu monga chikhulupiriro chanu.
30 Ndipo maso ao anaphenyuka. Ndipo Yesu anawauzitsa iwo, nanena, Yang’anirani, asadziwe munthu aliyense.
31 Koma iwo anatulukamo, nabukitsa mbiri yake m’dziko lonselo.
32 Ndipo pamene iwo analikutuluka, onani, anabwera naye kwa Iye munthu wosalankhula, wogwidwa ndi chiwanda.
33 Ndipo m’mene chinatulutsidwa chiwandacho, wosalankhulayo analankhula, ndipo makamu a anthu anazizwa, nanena, Kale lonse sichinaoneke chomwecho mwa Israele.
34 Koma Afarisi analinkunena, Atulutsa ziwanda ndi mphamvu zake za mfumu ya ziwanda.
Zotuta ndi antchito
35 Ndipo Yesu anayendayenda m’mizinda yonse ndi m’midzi, namaphunzitsa m’masunagogemwao, nalalikira Uthenga Wabwino wa Ufumuwo, nachiritsa nthenda iliyonse ndi zofooka zonse.
36 Koma Iye, poona makamuwo, anagwidwa m’mtima ndi chisoni chifukwa cha iwo, popeza anali okambululudwa ndi omwazikana, akunga nkhosa zopanda mbusa.
37 Pomwepo ananena kwa ophunzira ake, Zotuta zichulukadi koma antchito ali owerengeka.
38 Chifukwa chake pempherani Mwini zotuta kuti akokose antchito kukututa kwake.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/9-eded64c7d01e63afbd32280de03dbc39.mp3?version_id=1068—