Yesu mbuye wa Sabata
1 Nyengo imeneyo Yesu anapita tsiku laSabatapakati pa minda ya tirigu; ndipoophunziraake anali ndi njala, nayamba kubudula ngala, nadya.
2 KomaAfarisi, pakuona, anati kwa Iye, Tapenyani, ophunzira anu achita chosaloleka tsiku la Sabata.
3 Koma Iye anati kwa iwo, Kodi simunawerenge chimene anachichita Davide, pamene anali ndi njala, ndi iwo amene anali naye?
4 Kuti analowa m’nyumba ya Mulungu, nadya mikate yoonetsa, imene yosaloleka kudya iye kapena amene anali naye, koma ansembe okhaokha.
5 Kapena simunawerenge kodi m’chilamulo, kuti tsiku la Sabata ansembe mu Kachisi amaipitsa tsiku la Sabata, nakhala opanda tchimo?
6 Koma ndinena kwa inu, kuti wakuposa Kachisiyo ali pompano.
7 Koma mukadadziwa nchiyani ichi, Ndifuna chifundo, si nsembe ai; simukadaweruza olakwa iwo osachimwa,
8 pakutiMwana wa Munthuali mwini tsiku la Sabata.
Yesu achiritsa wa dzanja lopuwala
9 Ndipo Iye anachokera pamenepo, nalowa m’sunagogemwao;
10 ndipo onani, munali munthu wa dzanja lopuwala. Ndipo anamfunsitsa Iye, ndi kuti, Nkuloleka kodi kuchiritsa tsiku la Sabata? Kuti ampalamulitse mlandu.
11 Koma Iye anati kwa iwo, Munthu ndani wa inu, amene ali nayo nkhosa imodzi, ndipo ngati idzagwa m’dzenje tsiku la Sabata, kodi sadzaigwira, ndi kuitulutsa?
12 Nanga kuposa kwake kwa munthu ndi nkhosa nkotani! Chifukwa cha ichi nkuloleka kuchita zabwino tsiku la Sabata.
13 Pomwepo ananena Iye kwa munthuyo, Tansa dzanja lako. Ndipo iye analitansa, ndipo linabwezedwa lamoyo longa linzake.
14 Ndipo Afarisi anatuluka, nakhala upo womchitira Iye mwa kumuononga.
15 Koma Yesu m’mene anadziwa, anachokera kumeneko: ndipo anamtsata Iye anthu ambiri; ndipo Iye anawachiritsa iwo onse,
16 nawalimbitsira mau kuti asamuwulule Iye;
17 kuti chikachitidwe chonenedwa ndi Yesayamneneriuja, kuti,
18 Taona mnyamata wanga, amene ndinamsankha,
wokondedwa wanga, amene moyo wanga ukondwera naye;
pa Iye ndidzaika Mzimu wanga,
ndipo Iye adzalalikira chiweruzo kwa akunja.
19 Sadzalimbana, sadzafuula;
ngakhale mmodzi sadzamva mau ake m’makwalala;
20 bango lophwanyika sadzalithyola,
ndi nyali yofuka sadzaizima,
kufikira Iye adzatumiza chiweruzo chikagonjetse.
21 Ndipo akunja adzakhulupirira dzina lake.
Za Yesu ndi Belezebulu
22 Pomwepo anabwera naye kwa Iye munthu wogwidwa ndi chiwanda, wakhungu ndi wosalankhula; ndipo Iye anamchiritsa, kotero kuti wosalankhulayo analankhula, napenya.
23 Ndipo makamu onse a anthu anazizwa, nanena, Uyu si mwana wa Davide kodi?
24 Koma Afarisi pakumva, anati, Uyu samatulutsa ziwanda koma ndi mphamvu yake yaBelezebulu, mkulu wa ziwanda.
25 Ndipo Yesu anadziwa maganizo ao, nati kwa iwo, Ufumu uliwonse wogawanika pa wokha sukhalira kupasuka, ndi mzinda uliwonse kapena banja logawanika pa lokha silidzakhala;
26 ndipo ngatiSatanaamatulutsa Satana, iye agawanika pa yekha; ndipo udzakhala bwanji ufumu wake?
27 Ndipo ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu yake ya Belezebulu, ana anu amazitulutsa ndi mphamvu ya yani? Chifukwa chake iwo adzakhala oweruza anu.
28 Koma ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu yake ya Mzimu wa Mulungu, pomwepo Ufumu wa Mulungu unafika pa inu.
29 Kapena akhoza bwanji munthu kulowa m’banja la munthu wolimba, ndi kufunkha akatundu ake, ngati iye sayamba kumanga munthu wolimbayo? Ndipo pamenepo adzafunkha za m’banja lake.
30 Iye wosakhala pamodzi ndi Ine akana Ine, ndi iye wosasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amwazamwaza.
31 Chifukwa chake ndinena kwa inu, Machimo onse, ndi zonena zonse zamwano, zidzakhululukidwa kwa anthu; koma chamwano cha pa Mzimu Woyera sichidzakhululukidwa.
32 Ndipo aliyense amene anganenere Mwana wa Munthu zoipa, adzakhululukidwa; koma aliyense amene anganenere Mzimu Woyera zoipa sadzakhululukidwa nthawi ino kapena ilinkudzayo.
Mitengo ndi zipatso zao
33 Ukakoma mtengo, chipatso chake chomwe chikoma; ukaipa mtengo, chipatso chake chomwe chiipa; pakuti ndi chipatso chake mtengo udziwika.
34 Akubadwa inu a njoka, mungathe bwanji kulankhula zabwino, inu akukhala oipa? Pakuti m’kamwa mungolankhula mwa kusefuka kwake kwa mtima.
35 Munthu wabwino atulutsa zabwino m’chuma chake chabwino, ndi munthu woipa atulutsa zoipa m’chuma chake choipa.
36 Ndipo ndinena kwa inu, kuti mau onse opanda pake, amene anthu adzalankhula, adzawawerengera mlandu wake tsiku la kuweruza.
37 Pakuti udzayesedwa wolungama ndi mau ako, ndipo ndi mau ako omwe udzatsutsidwa.
Chizindikiro cha Yona
38 Pomwepo alembi ndi Afarisi ena anayankha Iye nati, Mphunzitsi, tifuna kuona chizindikiro cha Inu.
39 Koma Iye anayankha nati kwa iwo, Akubadwa oipa achigololo afunafuna chizindikiro; ndipo sichidzapatsidwa kwa iwo chizindikiro, komatu chizindikiro cha Yona mneneri;
40 pakuti monga Yona anali m’mimba mwa chinsomba masiku atatu ndi usiku wake, chomwecho Mwana wa Munthu adzakhala mumtima mwa dziko lapansi masiku atatu ndi usiku wake.
41 Anthu a ku Ninive adzauka pamlandu pamodzi ndi obadwa amakono, nadzawatsutsa; chifukwa iwo anatembenuka mtima ndi kulalikira kwake kwa Yona; ndipo onani, wakuposa Yona ali pano.
42 Mfumu yaikazi ya kumwera adzauka pamlandu pamodzi ndi obadwa amakono, nadzawatsutsa; chifukwa iye anachokera kumathero a dziko lapansi kudzamva nzeru ya Solomoni; ndipo onani, wakuposa Solomoni ali pano.
43 Koma mzimu wonyansa, utatuluka mwa munthu, umapitirira malo opanda madzi kufunafuna mpumulo, osaupeza.
44 Pomwepo unena, Ndidzabwerera kunka kunyumba kwanga, konkuja ndinatulukako; ndipo pakufikako uipeza yopanda wokhalamo, yosesedwa ndi yokonzedwa.
45 Pomwepo upita, nutenga pamodzi ndi uwu mizimu ina inzake isanu ndi iwiri yoipa yoposa mwini yekhayo, ndipo ilowa, nikhalamo. Ndipo matsirizidwe ake a munthu uyo akhala oipa oposa mayambidwe ake. Kotero kudzakhalanso kwa obadwa oipa amakono.
Abale a Yesu
46 Pamene Iye anali chilankhulire ndi makamu, onani, amake ndi abale ake anaima panja, nafuna kulankhula naye.
47 Ndipo munthu anati kwa Iye, Onani, amai wanu ndi abale anu aima pabwalo, nafuna kulankhula nanu.
48 Koma Iye anayankha, nati kwa iye wonenayo, Amai wanga ndani, ndipo abale anga ndi ayani?
49 Ndipo anatambalitsa dzanja lake pa ophunzira ake, nati, Penyani amai wanga ndi abale anga!
50 Pakuti aliyense amene adzachita chifuniro cha Atate wanga wa Kumwamba, yemweyo ndiye mbale wanga, ndi mlongo wanga, ndi amai wanga.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/12-28dbc587e4da56abfa4d83a83c6b6694.mp3?version_id=1068—