Categories
MATEYU

MATEYU 14

Herode amupha Yohane Mbatizi

1 Nthawi imeneyoHerodemfumu anamva mbiri ya Yesu,

2 nanena kwa anyamata ake, Uyo ndiye Yohane Mbatizi; anauka kwa akufa; ndipo chifukwa cha ichi zamphamvuzi zilimbalimba mwa iye.

3 Pakuti Herode adamgwira Yohane, nammanga, namuika m’nyumba yandende chifukwa cha Herodiasi, mkazi wa mbale wake Filipo.

4 Pakuti Yohane ananena kwa iye, Sikuloledwa kwa iwe kukhala naye.

5 Ndipo pofuna kumupha iye, anaopa khamu la anthu, popeza anamuyesa iyemneneri.

6 Koma pakufika tsiku la kubadwa kwake kwa Herode, mwana wamkazi wa Herodiasi anavina pakati pao, namkondweretsa Herode.

7 Pomwepo iye anamlonjeza chilumbirire, kumpatsa iye chimene chilichonse akapempha.

8 Ndipo iye, atampangira amake, anati, Ndipatseni ine kuno m’mbale mutu wa Yohane Mbatizi.

9 Ndipo mfumuyo anagwidwa ndi chisoni; koma chifukwa cha malumbiro ake, ndi cha iwo anali naye pachakudya, analamulira upatsidwe;

10 ndipo anatumiza mnyamata, namdula mutu Yohane m’nyumba yandende.

11 Ndipo anautenga mutu wake m’mbalemo, naupatsa buthulo: ndipo iye anamuka nao kwa amake.

12 Ndipoophunziraake anadza, natola mtembo, nauika; ndipo anadza nauza Yesu.

Yesu achulukitsa mikate poyamba paja

13 Ndipo Yesu pakumva, anachokera kumeneko m’ngalawa, kunka kumalo achipululu pa yekha; ndipo makamu, pamene anamva, anamtsata Iye mumtunda kuchokera m’midzi.

14 Ndipo Iye anatuluka, naona khamu lalikulu la anthu, nachitira iwo chifundo, nachiritsa akudwala ao.

15 Ndipo pamene panali madzulo, ophunzira ake anafika kwa Iye, nanena, Malo ano nga chipululu, ndipo nthawi yapita tsopano; kauzeni makamuwo amuke, apite kumidzi kukadzigulira okha kamba.

16 Koma Yesu anati kwa iwo, Iwo alibe chifukwa cha kumukira, apatseni ndinu adye.

17 Koma iwo ananena kwa Iye, Ife tilibe kanthu pano koma mikate isanu, ndi nsomba ziwiri.

18 Ndipo Iye anati, Mudze nazo kuno kwa Ine.

19 Ndipo Iye analamulira makamu a anthu akhale pansi paudzu; ndipo Iye anatenga mikate isanuyo ndi nsomba ziwirizo, ndipo m’mene anayang’ana kumwamba, anadalitsa, nanyema, napatsa mikateyo kwa ophunzira, ndi ophunzira kwa makamuwo.

20 Ndipo anadya onse, nakhuta; ndipo anatola makombo otsala, nadzala madengu khumi ndi iwiri.

21 Ndipo anadyawo anali amuna monga zikwi zisanu, kuwaleka akazi ndi ana.

Yesu ayenda panyanja

22 Ndipo pomwepo Iye anafulumiza ophunzira alowe m’ngalawa, ndi kumtsogolera Iye kutsidya lija, kufikira Iye atauza makamu amuke.

23 Ndipo pamene Iye anawauza makamuwo, anakwera m’phiri pa yekha, kukapemphera: ndipo pamene panali madzulo, Iye anakhala kumeneko yekha.

24 Koma pomwepo ngalawa idafika pakati pa nyanja, yozunzika ndi mafunde; pakuti mphepo inadza mokomana nao.

25 Ndipo pa ulonda wachinai wa usiku, Iye anadza kwa iwo, nayenda pamwamba pa nyanja.

26 Koma m’mene ophunzirawo anamuona Iye, alikuyenda pamadzi, ananthunthumira, nati, Ndi mzukwa! Ndipo anafuula ndi mantha.

27 Koma pomwepo Yesu analankhula nao, nati, Limbani mtima; ndine; musaope.

28 Ndipo Petro anamyankha Iye nati, Ambuye, ngati ndinutu, mundiuze ndidze kwa Inu pamadzi.

29 Ndipo Iye anati, Idza. Ndipo Petro anatsika m’ngalawa, nayenda pamadzi, kufika kwa Yesu.

30 Koma m’mene iye anaiona mphepo, anaopa; ndipo poyamba kumira, anafuula, nati, Ambuye, ndipulumutseni ine!

31 Ndipo pomwepo Yesu anatansa dzanja lake, namgwira iye, nanena naye, Iwe wokhulupirira pang’ono, wakayikiranji mtima?

32 Ndipo pamene iwo analowa m’ngalawamo, mphepo inaleka.

33 Ndipo iwo amene anali m’ngalawamo anamgwadira, nanena, Zoonadi, ndinu Mwana wa Mulungu.

34 Ndipo pamene iwo anaoloka, anafika kumtunda, ku Genesarete.

35 Ndipo m’mene amuna a pamenepo anamzindikira, anatumiza konse kudziko lonse lozungulira, nadza nao kwa Iye onse akukhala ndi nthenda;

36 ndipo anampempha Iye, kuti akhudze mphonje yokha ya chovala chake; ndipo onse amene anamkhudza anachiritsidwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/14-25fa18e7c226f893b2233c32ad645011.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *