Miyambo ya makolo
1 Pomwepo anadza kwa YesuAfarisindi alembi, ochokera kuYerusalemu, nati,
2 Ophunziraanu alumphiranji miyambo ya makolo? Pakuti sasamba manja pakudya.
3 Ndipo Iye anayankha, nati kwa iwo, Inunso mulumphiranji lamulo la Mulungu chifukwa cha miyambo yanu?
4 Pakuti Mulungu anati,
Lemekeza atate wako ndi amai ako; ndipo,
Wakunenera atate wake ndi amake zoipa, afe ndithu.
5 Koma inu munena, Aliyense amene anena kwa atate wake kapena kwa amake, Icho ukanathandizidwa nacho, nchoperekedwa kwa Mulungu;
6 iyeyo sadzalemekeza atate wake. Ndipo inu mupeputsa mau a Mulungu chifukwa cha miyambo yanu.
7 Onyenga inu! Yesaya ananenera bwino za inu, ndi kuti,
8 Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao;
koma mtima wao uli kutali ndi Ine.
9 Koma andilambira Ine kwachabe,
ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.
10 Ndipo Iye anaitana makamuwo nati kwa iwo, Imvani, nimudziwitse;
11 si chimene chilowa m’kamwa mwake chiipitsa munthu; koma chimene chituluka m’kamwa mwake, ndicho chiipitsa munthu.
12 Pomwepo anadza ophunzira, nanena kwa Iye, Mudziwa kodi kuti Afarisi anakhumudwa pakumva chonenacho?
13 Koma Iye anayankha nati, Mmera wonse, umene Atate wanga wa Kumwamba sanaubzale, udzazulidwa.
14 Kawalekeni iwo, ali atsogoleri akhungu. Ndipo ngati wakhungu amtsogolera wakhungu, onse awiri adzagwa m’mbuna.
15 Ndipo Petro anayankha nati kwa Iye, Mutifotokozere ife fanizoli.
16 Ndipo Iye anati, Kodi inunso mukhala chipulukirire?
17 Simudziwa kodi kuti zonse zakulowa m’kamwa zipita m’mimba, ndipo zitayidwa kuthengo?
18 Koma zakutuluka m’kamwa zichokera mumtima; ndizo ziipitsa munthu.
19 Pakuti mumtima muchokera maganizo oipa, zakupha, zachigololo, zachiwerewere, zakuba, za umboni wonama, zamwano;
20 izi ndizo ziipitsa munthu, koma kudya osasamba manja sikuipitsa munthu ai.
Mkazi wa ku Kanani
21 Ndipo Yesu anatulukapo napatukira kumbali za Tiro ndi Sidoni.
22 Ndipo onani, mkazi wa ku Kanani anatuluka m’malire, nafuula, nati, Mundichitire ine chifundo Ambuye, mwana wa Davide; mwana wanga wamkazi wagwidwa koopsa ndi chiwanda.
23 Koma Iye sanamyankhe mau amodzi. Ndipo ophunzira ake anadza, nampempha, nati, Mumuuze amuke; pakuti afuula pambuyo pathu.
24 Ndipo Iye anayankha, nati, Sindinatumidwa kwa ena koma kwa nkhosa zotayika za banja la Israele.
25 Koma iye anadza, namgwadira Iye, nanena, Ambuye, ndithangateni ine.
26 Ndipo Iye anayankha, nati, Sichabwino kutenga mkate wa ana, ndi kuuponyera tiagalu.
27 Koma iye anati, Eetu, Ambuye, pakutinso tiagalu timadya nyenyeswa zakugwa pagome pa ambuye ao.
28 Pomwepo Yesu anayankha, nati kwa iye, Mkaziwe, chikhulupiriro chako ndi chachikulu; chikhale kwa iwe monga momwe wafunira. Ndipo mwana wake anachira nthawi yomweyo.
Yesu achulukitsa mikate pachiwiri paja
29 Ndipo Yesu anachoka kumeneko, nadza kunyanja ya Galileya, nakwera m’phiri, nakhala pansi pamenepo.
30 Ndipo makamu ambiri a anthu anadza kwa Iye, ali nao opunduka miyendo, akhungu, osalankhula, opunduka ziwalo, ndi ena ambiri, nawakhazika pansi pa mapazi ake: ndipo Iye anawachiritsa;
31 kotero kuti khamulo linazizwa, pakupenya osalankhula nalankhula, opunduka ziwalo nachira, ndi opunduka miyendo nayenda, ndi akhungu napenya, ndipo iwo analemekeza Mulungu wa Israele.
32 Ndipo Yesu anaitana ophunzira ake, nati, Mtima wanga uchitira chifundo khamu la anthuwa, pakuti ali chikhalire ndi Ine masiku atatu, ndipo alibe kanthu kakudya, ndipo sindifuna kuwauza iwo amuke osadya, kuti angaziye panjira.
33 Ndipo ophunzira ananena kwa Iye, Tiione kuti mikate yotere m’chipululu yakukhutitsa unyinji wotere wa anthu?
34 Ndipo Yesu ananena kwa iwo, Muli nayo mikate ingati? Ndipo iwo anati, Isanu ndi iwiri, ndi tinsomba pang’ono.
35 Ndipo Iye analamulira anthuwo akhale pansi onse;
36 natenga mikateyo isanu ndi iwiri ndi nsombazo; nayamika Mulungu, nanyema, napatsa kwa ophunzira, ndi ophunzira kwa anthu.
37 Ndipo onsewa anadya, nakhuta: ndipo anatola makombo otsala madengu asanu ndi awiri odzala.
38 Ndipo anadyawo anali amuna zikwi zinai kuwaleka akazi ndi ana.
39 Ndipo m’mene Iye anauza makamuwo amuke, analowa m’ngalawa, nafika m’malire a Magadani.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/15-10faaa21fdd55fe869e07ce0afe69552.mp3?version_id=1068—