Fanizo la ukwati
1 Ndipo Yesu anayankha, nalankhulanso kwa iwo m’mafanizo, nati,
2 Ufumu wa Kumwamba ufanafana ndi munthu, mfumu, amene anakonzera mwana wake phwando la ukwati,
3 natumiza akapolo ake kukaitana oitanidwa kuukwati umene; ndipo iwo sanafune kudza.
4 Pomwepo anatumizanso akapolo ena, nanena, Uzani oitanidwawo, Onani, ndakonza phwando langa; ng’ombe zanga, ndi zonona ndinazipha, ndi zinthu zonse zapsa: idzani kuukwati.
5 Koma iwo ananyalanyaza, nachoka, wina kumunda wake, wina kumalonda ake:
6 ndipo otsala anagwira akapolo ake, nawachitira chipongwe, nawapha.
7 Koma mfumu inakwiya; nituma asilikali ake napululutsa ambanda aja, nitentha mzinda wao.
8 Pomwepo inanena kwa akapolo ake, Za ukwati tsopano zapsa, koma oitanidwawo sanayenere.
9 Chifukwa chake pitani inu kumphambano za njira, ndipo aliyense amene mukampeze, itanani kuukwatiku.
10 Ndipo akapolo ao anatulukira kunjira, nasonkhanitsa onse amene anawapeza, ngakhale oipa, ngakhale abwino; ndipo ukwatiwo unadzala ndi okhala pachakudya.
11 Koma mfumuyo m’mene inadza kuwaona akudyawo, anapenya momwemo munthu wosavala chovala cha ukwati;
12 nanena kwa iye, Mnzangawe, unalowa muno bwanji wosakhala nacho chovala cha ukwati? Ndipo iye analibe mau.
13 Pomwepo mfumu inati kwa atumiki, Mumange iye manja ndi miyendo, mumponye kumdima wakunja; komweko kudzali kulira ndi kukukuta mano.
14 Pakuti oitanidwa ndiwo ambiri, koma osankhidwa ndiwo owerengeka.
Za kupereka msonkho kwa Kaisara
15 PomwepoAfarisianamuka, nakhala upo wakumkola Iye m’kulankhula kwake.
16 Ndipo anatumiza kwa Iyeophunziraao, pamodzi ndi Aherode, amene ananena, Mphunzitsi, tidziwa kuti muli woona, ndipo muphunzitsa njira ya Mulungu moona ndithu, ndipo simusamala munthu aliyense; pakuti simuyang’anira pa nkhope ya anthu.
17 Chifukwa chake mutiuze ife, muganiza chiyani? Kuloledwa kodi kupatsa msonkho kwaKaisara, kapena iai?
18 Koma Yesu anadziwa kuipa kwao, nati, Mundiyeseranji Ine, onyenga inu?
19 Tandionetsani Ine ndalama yamsonkho. Ndipo iwo anadza nalo kwa Iye rupiya latheka.
20 Ndipo Iye anati kwa iwo, Ncha yani chithunzithunzi ichi, ndi kulemba kwake?
21 Nanena iwo, Cha Kaisara. Pomwepo Iye anati kwa iwo, Chifukwa chake patsani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.
22 Ndipo pamene iwo anamva, anazizwa, namsiya Iye, nachokapo.
Asaduki ndi kuuka kwa akufa
23 Tsiku lomwelo anadza kwa IyeAsaduki, amene amanena kuti palibe kuuka kwa akufa; namfunsa Iye,
24 nanena, Mphunzitsi, Mose anati, Ngati munthu akafa wopanda mwana, mphwake adzakwatira mkazi wake, nadzamuukitsira mbale wake mbeu.
25 Tsono panali ndi ife abale asanu ndi awiri; ndipo wakuyamba anakwatira, namwalira wopanda mbeu, nasiyira mphwake mkazi wake;
26 chimodzimodzi wachiwiri, ndi wachitatu, kufikira wachisanu ndi chiwiri.
27 Ndipo pomalizira anamwaliranso mkaziyo.
28 Chifukwa chake m’kuuka kwa akufa, iye adzakhala mkazi wa yani wa asanu ndi awiriwo? Pakuti onse anakhala naye.
29 Koma Yesu anayankha, nati kwa iwo, Mungolakwa osadziwa malembo, kapena mphamvu za Mulungu.
30 Pakuti m’kuuka kwa akufa sakwatira, kapena kukwatiwa, koma akhala ngatiangeloa Kumwamba.
31 Koma za kuuka kwa akufa, simunawerenge kodi chomwe chinanenedwa kwa inu ndi Mulungu, kuti,
32 Ine ndili Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isaki,
ndi Mulungu wa Yakobo?
Sali Mulungu wa akufa koma wa amoyo.
33 Ndipo pamene makamu a anthu anamva, anazizwa ndi chiphunzitso chake.
Lamulo lalikulu
34 Koma Afarisi, pakumva kuti Iye anatontholetsa Asaduki, anasonkhana.
35 Ndipo mmodzi wa iwo, mphunzitsi wa malamulo, anamfunsa ndi kumuyesa Iye, nati,
36 Mphunzitsi, lamulo lalikulu ndi liti la m’chilamulo?
37 Ndipo Yesu anati kwa iye, Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse.
38 Ili ndilo lamulo lalikulu ndi loyamba.
39 Ndipo lachiwiri lolingana nalo ndili, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.
40 Pa malamulo awa awiri mpokolowekapo chilamulo chonse ndi aneneri.
Khristu ndiye Mwana wa Davide
41 Ndipo pamene Afarisi anasonkhana, Yesu anawafunsa,
42 nati, Muganiza bwanji zaKhristu? Ali mwana wa yani? Iwo ananena kwa Iye, Wa Davide.
43 Iye anati kwa iwo, Ndipo Davide mu Mzimu amtchula Iye bwanji Ambuye, nanena,
44 Ambuye ananena kwa Ambuye wanga,
ukhale padzanja lamanja langa,
kufikira Ine ndidzaika adani ako pansi pa mapazi ako.
45 Chifukwa chake ngati Davide amtchula Iye Ambuye, ali mwana wake bwanji? Ndipo panalibe mmodzi anatha kumyankha mau.
46 Ndipo sanalimbike mtima munthu aliyense kumfunsa kanthu kuyambira tsiku lomwelo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/22-03aa0d45a9b679125d5a67f52b1fb712.mp3?version_id=1068—