Categories
MATEYU

MATEYU 24

Yesu anenera zam’tsogolo. Chiyambi cha masautso

1 Ndipo Yesu anatuluka ku Kachisi; ndipoophunziraake anadza kudzamuonetsa chimangidwe cha Kachisiyo.

2 Koma Iye anayankha nati kwa iwo, Simuona izi zonse kodi? Indetu ndinena kwa inu, Sipadzakhala pano mwala umodzi pa unzake, umene sudzagwetsedwa.

3 Ndipo pamene Iye analikukhala pansi paphiri la Azitona, ophunzira anadza kwa Iye pa yekha, nanena, Mutiuze ife zija zidzaoneka liti? Ndipo chizindikiro cha kufika kwanu nchiyani, ndi cha mathedwe a nthawi ya pansi pano?

4 Ndipo Yesu anayankha nati kwa iwo, Yang’anirani, asasokeretse inu munthu.

5 Pakuti ambiri adzafika m’dzina langa, nadzanena, Ine ndineKhristu, nadzasokeretsa anthu ambiri.

6 Koma inu mudzayamba kumva za nkhondo, ndi mbiri za nkhondo; onani, musadere nkhawa; pakuti kuyenera kuti izi zioneke; koma chitsiriziro sichinafike.

7 Pakuti mtundu umodzi wa anthu udzaukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu ndi ufumu wina; ndipo kudzakhala njala ndi zivomezi m’malo akutiakuti.

8 Koma ndizo zonsezi zowawa zoyamba.

9 Pamenepo adzakuperekani kunsautso, nadzakuphani; ndipo anthu a mitundu yonse adzadana nanu, chifukwa cha dzina langa.

10 Ndipo pomwepo ambiri adzakhumudwa, nadzaperekana wina ndi mnzake, nadzadana wina ndi mnzake.

11 Ndipo aneneri onama ambiri adzauka, nadzasokeretsa anthu ambiri.

12 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa kusaweruzika, chikondano cha anthu aunyinji chidzazilala.

13 Koma iye wakulimbika chilimbikire kufikira kuchimaliziro, yemweyo adzapulumuka.

14 Ndipo Uthenga uwu Wabwino wa Ufumu udzalalikidwa padziko lonse lapansi, ukhale mboni kwa anthu a mitundu yonse; ndipo pomwepo chidzafika chimaliziro.

Chisautso chachikulu

15 Chifukwa chake m’mene mukadzaona chonyansa cha kupululutsa, chimene chidanenedwa ndi Danielemneneri, chitaima m’malo oyera (iye amene awerenga m’kalata azindikire)

16 pomwepo iwo ali mu Yudeya athawire kumapiri:

17 iye ali pamwamba pa tsindwi, asatsikire kunyamula za m’nyumba mwake;

18 ndi iye wa m’munda asabwere kutenga chofunda chake.

19 Koma tsoka ali nalo iwo akukhala ndi pakati, ndi akuyamwitsa ana m’masiku awo!

20 Ndipo pempherani kuti kuthawa kwanu kusakhale pa nyengo yachisanu, kapena paSabata;

21 pakuti pomwepo padzakhala masauko aakulu, monga sipadakhale otero kuyambira chiyambi cha dziko, kufikira tsopano, inde ndipo sipadzakhalanso.

22 Ndipo akadaleka kufupikitsidwa masiku awo, sakadapulumuka munthu aliyense: koma chifukwa cha osankhidwawo masiku awo adzafupikitsidwa.

23 Pomwepo munthu akanena kwa inu, Onani, Khristu ali kuno, kapena uko musamvomereze;

24 chifukwa Akhristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzaonetsa zizindikiro zazikulu ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati nkotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.

25 Chifukwa chake akanena kwa inu,

26 Onani, Iye ali m’chipululu; musamukeko. Onani, ali m’zipinda; musavomereze.

27 Pakuti monga mphezi idzera kum’mawa, nionekera kufikira kumadzulo; kotero kudzakhalanso kufika kwake kwaMwana wa Munthu.

28 Kumene kulikonse kuli mtembo, miimba idzasonkhanira konko.

Kudza kwake kwa Mwana wa Munthu

29 Koma pomwepo, atapita masauko a masiku awo, dzuwa lidzadetsedwa, ndi mwezi sudzaonetsa kuwala kwake, ndi nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba, ndi mphamvu za kumwamba zidzagwedezeka:

30 ndipo pomwepo padzaoneka m’thambo chizindikiro cha Mwana wa Munthu; ndipo mitundu yonse ya padziko lapansi idzadziguguda pachifuwa, nidzapenya Mwana wa Munthu alinkudza pa mitambo ya kumwamba, ndi mphamvu ndi ulemerero waukulu.

31 Ndipo Iye adzatumizaangeloake ndi kulira kwakukulu kwa lipenga, ndipo iwo adzasonkhanitsa osankhidwa ake kumphepo zinai, kuyambira malekezero a thambo kufikira malekezero ake ena.

32 Koma phunzirani ndi mkuyufanizolake; pamene tsopano nthambi yake ili yanthete, niphuka masamba ake, muzindikira kuti dzinja liyandikira;

33 chomwechonso inu, pamene mudzaona zimenezo, zindikirani kuti Iye ali pafupi, inde pakhomo.

34 Indetu ndinena kwa inu, mbadwo uwu sudzatha kuchoka, kufikira zinthu zonsezi zidzachitidwa.

35 Thambo ndi dziko lapansi zidzachoka, koma mau anga sadzachoka ai.

Awachenjeza adikire

36 Koma za tsiku ili ndi nthawi yake saidziwa munthu aliyense, angakhale angelo a Kumwamba, kapena Mwana, koma Atate yekha.

37 Ndipo monga masiku a Nowa, kotero kudzakhala kufika kwake kwa Mwana wa Munthu.

38 Pakuti monga m’masiku aja, chisanafike chigumula, anthu analinkudya ndi kumwa, analikukwatira ndi kukwatiwa, kufikira tsiku limene Nowa analowa m’chingalawa,

39 ndipo iwo sanadziwe kanthu, kufikira kumene chigumula chinadza, chinapululutsa iwo onse, kotero kudzakhala kufika kwake kwa Mwana wa Munthu.

40 Pomwepo adzakhala awiri m’munda; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa:

41 awiri adzakhala opera pamphero; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.

42 Chifukwa chake dikirani, pakuti simudziwa tsiku lake lakufika Ambuye wanu.

43 Koma dziwani ichi, kuti mwini nyumba akadadziwa nthawi yiti mbala ikudza, iye akadadikira, ndipo sakadalola kuti nyumba yake ibooledwe.

44 Chifukwa chake khalani inunso okonzekeratu; chifukwa munthawi m’mene simuganizira, Mwana wa Munthu adzadza.

Fanizo la akapolo awiri

45 Ndani kodi ali kapolo wokhulupirika ndi wanzeru, amene mbuye wake anamkhazika woyang’anira banja lake, kuwapatsa zakudya pa nthawi yake?

46 Wodala kapolo amene mbuye wake, pakufika, adzampeza iye alikuchita chotero.

47 Indetu, ndinena kwa inu, kuti adzamkhazika iye woyang’anira zinthu zake zonse.

48 Koma kapolo woipa akanena mumtima mwake, Mbuye wanga wachedwa;

49 nadzayamba kupanda akapolo anzake, nadya ndi kumwa pamodzi ndi oledzera;

50 mbuye wa kapoloyo adzafika tsiku losamuyembekeza iye, ndi nthawi yosadziwa iye,

51 nadzamdula, nadzaika pokhala pake ndi anthu onyenga; pomwepo padzakhala kulira ndi kukukuta mano.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/24-40e421c79f64c6db17626109d9a91d53.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *