Yesu auka kwa akufa
1 Ndipo litapitaSabata, Maria wa Magadala, ndi Maria amake wa Yakobo, ndi Salome, anagula zonunkhira, kuti akadze kumdzoza Iye.
2 Ndipo anadza kumanda mamawa tsiku loyamba la Sabata, litatuluka dzuwa.
3 Ndipo analikunena mwa okha, Adzatikunkhunizira ndani mwalawo, pakhomo la manda?
4 Ndipo pamene anakweza maso anaona kuti mwala wakunkhunizidwa, pakuti unali waukulu ndithu.
5 Ndipo pamene analowa m’manda, anaona mnyamata alikukhala kumbali ya kudzanja lamanja, wovala mwinjiro woyera; ndipo iwo anadabwa.
6 Ndipo iye ananena nao, Musadabwe: mulikufuna Yesu Mnazarene amene anapachikidwa; anauka; sali pano; taonani, mbuto m’mene anaikamo Iye!
7 Koma mukani, uzaniophunziraake, ndi Petro, kuti akutsogolerani inu ku Galileya; kumeneko mudzamuona Iye, monga ananena ndi inu.
8 Ndipo anatuluka iwo, nathawa kumanda; pakuti kunthunthumira ndi kudabwa kwakukulu kudawagwira; ndipo sanauze kanthu kwa munthu aliyense; pakuti anachita mantha.
Yesu aonekera kwa ophunzira ake
9 Ndipo pamene Iye adauka mamawa tsiku loyamba la sabata, anayamba kuonekera kwa Maria wa Magadala, amene Iye adamtulutsira ziwanda zisanu ndi ziwiri.
10 Iyeyu anapita kuwauza iwo amene ankakhala naye, ali ndi chisoni ndi kulira misozi.
11 Ndipo iwowo, pamene anamva kuti ali moyo, ndi kuti adapenyeka kwa iye, sanamvere.
12 Ndipo zitatha izi, anaonekanso Iye m’maonekedwe ena kwa awiri a iwo alikuyenda kupita kumidzi.
13 Ndipo iwowa anachoka nawauza otsala; koma iwo omwe sanawavomereze.
14 Ndipo chitatha icho anaonekera kwa khumi ndi mmodzi iwo okha, alikuseama pachakudya; ndipo anawadzudzula chifukwa cha kusavomereza kwao ndi kuuma mtima, popeza sanavomereze iwo amene adamuona, atauka Iye.
15 Ndipo ananena nao, Mukani kudziko lonse lapansi, lalikirani Uthenga Wabwino kwa olengedwa onse.
16 Amene akhulupirira nabatizidwa, adzapulumutsidwa; koma amene sakhulupirira adzalangidwa.
17 Ndipo zizindikiro izi zidzawatsata iwo akukhulupirira: m’dzina langa adzatulutsa ziwanda; adzalankhula ndi malankhulidwe atsopano;
18 adzatola njoka, ndipo ngakhale akamwa kanthu kakufa nako, sikadzawapweteka; adzaika manja ao pa odwala, ndipo adzachira.
19 Pamenepo Ambuye Yesu, atatha kulankhula nao, analandiridwa Kumwamba, nakhala padzanja lamanja la Mulungu.
20 Ndipo iwowa anatuluka, nalalikira ponseponse, ndipo Ambuye anachita nao pamodzi, natsimikiza mau ndi zizindikiro zakutsatapo.Amen.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/16-e61ac6f0ef6fafd88a5facb0f37dbc0b.mp3?version_id=1068—