Yesu achiritsa munthu wambulu
1 Ndipo panali pamene Iye analowa m’nyumba ya mmodzi wa akulu aAfarisitsiku laSabata, kukadya, iwo analikumzonda Iye.
2 Ndipo onani, panali pamaso pake munthu wambulu.
3 Ndipo Yesu anayankha nati kwa achilamulo ndi Afarisi, nanena, Kodi nkuloledwa tsiku la Sabata kuchiritsa, kapena iai?
4 Koma iwo anakhala chete. Ndipo anamtenga namchiritsa, namuuza apite.
5 Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu bulu wake kapena ng’ombe yake itagwa m’chitsime, ndipo sadzaitulutsa pomwepo tsiku la Sabata kodi?
6 Ndipo iwo sanathe kumbwezera mau pa zinthu izi.
Fanizo la mipando ya ulemu
7 Ndipo Iye ananenafanizokwa oitanidwa, popenya kuti amadzisankhira mipando yaulemu, nanena kwa iwo,
8 Pamene paliponse waitanidwa iwe ndi munthu ku chakudya cha ukwati, usaseama pa mpando waulemu; kuti kapena wina waulemu wakuposa iwe akaitanidwe ndi iye,
9 ndipo pakufika iye amene adaitana iwe ndi uyu, adzati kwa iwe, Mpatse uyu malo; ndipo pomwepo udzayamba manyazi kukhala pa mpando wa kuthungo.
10 Koma pamene paliponse waitanidwa iwe, pita nukhale pansi pa malo a kuthungo; kotero kuti pamene akadza iye anakuitana iwe, akanena ndi iwe, Bwenzi langa, sendera, kwera kuno; pomwepo udzakhala ndi ulemerero pamaso pa onse akuseama pachakudya pamodzi ndi iwe.
11 Chifukwa munthu aliyense wakudzikuza adzachepetsedwa; ndipo wakudzichepetsa adzakulitsidwa.
12 Ndipo ananenanso kwa iye amene adamuitana, Pamene ukonza chakudya cha pausana kapena cha madzulo, usaitane abwenzi ako, kapena abale ako, kapena a fuko lako, kapena anansi ako eni chuma; kuti kapena iwonso angabwereze kuitana iwe, ndipo udzakhala nayo mphotho.
13 Koma pamene ukonza phwando uitane aumphawi, opunduka, otsimphina, akhungu;
14 ndipo udzakhala wodala; chifukwa iwo alibe chakubwezera iwe mphotho; pakuti idzabwezedwa mphotho pa kuuka kwa olungama.
Fanizo la phwando lalikulu
15 Ndipo pamene wina wa iwo akuseama pachakudya pamodzi ndi Iye anamva izi, anati kwa Iye, Wodala iye amene adzadya mkate mu Ufumu wa Mulungu.
16 Koma anati kwa iye, Munthu wina anakonza phwando lalikulu; naitana anthu ambiri;
17 ndipo anatumiza kapolo wake pa nthawi ya phwando kukanena kwa oitanidwawo, Idzani, chifukwa zonse zakonzeka tsopano.
18 Ndipo onse ndi mtima umodzi anayamba kuwiringula. Woyamba anati kwa iye, Ine ndagula munda, ndipo ndiyenera ndituluke kukauona; ndikupempha undilole ine ndisafika.
19 Ndipo anati wina, Ine ndagula ng’ombe za magoli asanu, ndipo ndinka kukaziyesa; ndikupempha undilole ine ndisafika.
20 Ndipo anati wina, Ine ndakwatira mkazi, ndipo chifukwa chake sindingathe kudza.
21 Ndipo kapoloyo pakubwera anauza mbuye wake zinthu izi. Pamenepo mwini nyumba anakwiya, nati kwa kapolo wake, Tuluka msanga, pita kumakwalala ndi kunjira za mzinda, nubwere nao muno aumphawi ndi opunduka ndi akhungu ndi otsimphina.
22 Ndipo kapoloyo anati, Ambuye, chimene munachilamulira chachitika, ndipo malo atsalapo.
23 Ndipo mbuye ananena kwa kapoloyo, Tuluka, nupite kumiseu ndi njira za kuminda, nuwaumirize anthu alowe, kuti nyumba yanga idzale.
24 Pakuti ndinena kwa inu, kuti kulibe mmodzi wa amuna oitanidwa aja adzalawa phwando langa.
Womtsata Ambuye adzayesedwa
25 Ndipo mipingo yambiri ya anthu inamuka naye; ndipo Iye anapotoloka, nati kwa iwo,
26 Munthu akadza kwa Ine, wosada atate wake ndi amake, ndi mkazi wake, ndi ana, ndi abale, ndi alongo ake, inde ndi moyo wake womwe wa iye mwini, sangathe kukhala wophunzirawanga.
27 Ndipo aliyense amene sasenza mtanda wake wa mwini yekha, ndi kudza pambuyo panga, sangathe kukhala wophunzira wanga.
28 Pakuti ndani wa inu amene akafuna kumanga nsanja yaitali, sayamba wakhala pansi, nawerengera mtengo wake, aone ngati ali nazo zakuimaliza?
29 Kuti kungachitike, pamene atakhazika pansi miyala ya kumaziko ake, osakhoza kuimaliza anthu onse akuyang’ana adzayamba kumseka iye,
30 ndi kunena kuti, Munthu uyu anayamba kumanga, koma sanathe kumaliza.
Fanizo la mfumu yanzeru
31 Kapena mfumu yanji pakupita kukomana ndi nkhondo ya mfumu inzake, sayamba wakhala pansi, nafunsana ndi akulu ngati akhoza ndi asilikali ake zikwi khumi kulimbana naye wina uja alikudza kukomana naye ndi asilikali zikwi makumi awiri?
32 Koma ngati sakhoza, atumiza akazembe, pokhala winayo ali kutalitali, nafunsa za mtendere.
33 Chifukwa chake tsono, yense wa inu amene sakaniza zonse ali nazo, sangathe kukhala wophunzira wanga.
34 Kotero mchere uli wokoma; koma ngati mchere utasukuluka adzaukoleretsa ndi chiyani?
35 Suyenera kuuthira pamunda kapena padzala, autaya kunja. Amene ali nao makutu akumva amve.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/14-dc3e05e0d7d0eea440279880ea6b7e76.mp3?version_id=1068—