Categories
YOHANE

YOHANE 3

Yesu aphunzitsa Nikodemo za kubadwa kwatsopano

1 Koma panali munthu waAfarisi, dzina lake Nikodemo, mkulu wa Ayuda.

2 Iyeyu anadza kwa Yesu usiku, nati kwa Iye,Rabi, tidziwa kuti Inu ndinu mphunzitsi wochokera kwa Mulungu; pakuti palibe munthu akhoza kuchita zizindikiro zimene Inu muchita, ngati Mulungu sakhala naye.

3 Yesu anayankha nati kwa iye, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu sabadwa mwatsopano, sangathe kuona Ufumu wa Mulungu.

4 Nikodemo ananena kwa Iye, Munthu akhoza bwanji kubadwa atakalamba? Kodi akhoza kulowanso m’mimba ya amake ndi kubadwa?

5 Yesu anayankha, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu, sangathe kulowa ufumu wa Mulungu.

6 Chobadwa m’thupi chikhala thupi, ndipo chobadwa mwa Mzimu, chikhala mzimu.

7 Usadabwe chifukwa ndinati kwa iwe, Uyenera kubadwa mwatsopano.

8 Mphepo iomba pomwe ifuna, ndipo ukumva mau ake, koma sudziwa kumene ichokera, ndi kumene imuka; chotero aliyense wobadwa mwa Mzimu.

9 Nikodemo anayankha nati kwa Iye, Izi zingatheke bwanji?

10 Yesu anayankha nati kwa iye, Kodi uli mphunzitsi wa Israele, ndipo sudziwa izi?

11 Indetu, indetu, ndinena kwa iwe, Tilankhula chimene tichidziwa, ndipo tichita umboni za chimene tachiona; ndipo umboni wathu simuulandira.

12 Ngati ndakuuzani za pansi pano, ndipo simukhulupirira, mudzakhulupirira bwanji, ngati ndikuuzani za Kumwamba?

13 Ndipo kulibe munthu anakwera Kumwamba, koma Iye wotsikayo kuchokera Kumwamba, ndiyeMwana wa Munthu, wokhala mu Mwambayo.

14 Ndipo monga Mose anakweza njoka m’chipululu, chotero Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa;

15 kuti yense wakukhulupirira akhale nao moyo wosatha mwa Iye.

16 Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.

17 Pakuti Mulungu sanatume Mwana wake kudziko lapansi, kuti akaweruze dziko lapansi, koma kuti dziko lapansi likapulumutsidwe ndi Iye.

18 Wokhulupirira Iye saweruzidwa; wosakhulupirira waweruzidwa ngakhale tsopano, chifukwa sanakhulupirire dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu.

19 Koma chiweruziro ndi ichi, kuti kuunika kunadza kudziko lapansi, ndipo anthu anakonda mdima koposa kuunika; pakuti ntchito zao zinali zoipa.

20 Pakuti yense wakuchita zoipa adana nako kuunika, ndipo sakudza kwa kuunika, kuti zingatsutsidwe ntchito zake.

21 Koma wochita choonadi adza kukuunika, kuti ntchito zake zionekere kuti zinachitidwa mwa Mulungu.

Yohane achitanso umboni za Yesu

22 Zitapita izi anadza Yesu ndiophunziraake kudziko la Yudeya; ndipo pamenepo anatsotsa nao pamodzi, nabatiza.

23 Ndipo Yohane analinkubatiza mu Ainoni pafupi pa Salimu, chifukwa panali madzi ambiri pamenepo; ndipo analinkufikako anthu, nalinkubatizidwa.

24 Pakuti Yohane sanaikidwe m’ndende.

25 Pamenepo padauka kufunsana mwa ophunzira ake a Yohane ndi Myuda za mayeretsedwe.

26 Ndipo anadza kwa Yohane, nati kwa iye, Rabi, Iye amene anali ndi inu tsidya lija la Yordani, amene munamchitira umboni, taonani yemweyu abatiza, ndipo anthu onse alinkudza kwa Iye.

27 Yohane anayankha nati, Munthu sangathe kulandira kanthu, ngati sikapatsidwa kwa iye kuchokera Kumwamba.

28 Inu nokha mundichitira umboni, kuti ndinati, SindineKhristu, koma kuti ndili wotumidwa m’tsogolo mwake mwa Iye.

29 Iye amene ali naye mkwatibwi ali mkwati, koma mnzake wa mkwatiyo, wakuimirira ndi kumvera iye, akondwera kwakukulu chifukwa cha mau a mkwatiyo; chifukwa chake chimwemwe changa chimene chakwanira.

30 Iyeyo ayenera kukula koma ine ndichepe.

31 Iye wochokera Kumwamba ali woposa onse; iye amene ali wa dziko lapansi ali wa dziko lapansi, nalankhula za dziko lapansi: Iye wochokera Kumwamba ali woposa onse.

32 Chimene anachiona nachimva, achita umboni wa ichi chomwe; ndipo kulibe munthu alandira umboni wake.

33 Iye amene analandira umboni wake anaikapo chizindikiro chake kuti Mulungu ali woona.

34 Pakuti Iye amene Mulungu anamtuma alankhula mau a Mulungu; pakuti sapatsa Mzimu ndi muyeso.

35 Atate akonda Mwana, nampatsa zinthu zonse m’dzanja lake.

36 Iye amene akhulupirira Mwanayo ali nao moyo wosatha; koma iye amene sakhulupirira Mwanayo sadzaona moyo, koma mkwiyo wa Mulungu ukhala pa iye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/3-b44c91b4881964c95b9439658caa460d.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *