Awachenjeza za kuzunzidwa
1 Izi ndalankhula ndi inu kuti mungakhumudwitsidwe.
2 Adzakutulutsani m’masunagoge, koma ikudza nthawi imene yense wakupha inu adzayesa kuti atumikira Mulungu.
3 Ndipo izi adzachita, chifukwa sanadziwe Atate, kapena Ine.
4 Koma zinthu izi ndalankhula ndi inu kuti ikadza nthawi yao, mukakumbukire kuti ndinakuuzani. Koma izi sindinanene kwa inu kuyambira pachiyambi, chifukwa ndinali pamodzi ndi inu.
5 Koma tsopano ndimuka kwa Iye wondituma Ine; ndipo palibe wina mwa inu andifunsa Ine, Munka kuti?
6 Koma chifukwa ndalankhula izi ndi inu chisoni chadzala mumtima mwanu.
Chomwe Mzimu Woyera adzachitira anthu
7 Koma ndinena Ine choonadi ndi inu; kuyenera kwa inu kuti ndichoke Ine; pakuti ngati sindichoka, Nkhosweyo sadzadza kwa inu; koma ngati ndipita ndidzamtuma Iye kwa inu.
8 Ndipo atadza Iyeyo, adzatsutsa dziko lapansi za machimo, ndi za chilungamo, ndi za chiweruziro;
9 za machimo, chifukwa sakhulupirira Ine;
10 za chilungamo, chifukwa ndinka kwa Atate, ndipo simundionanso;
11 za chiweruzo, chifukwa mkulu wa dziko ili lapansi waweruzidwa.
12 Ndili nazo zambirinso zakunena kwa inu, koma simungathe kuzisenza tsopano lino.
13 Koma atadza Iyeyo, Mzimu wa choonadi, adzatsogolera inu m’choonadi chonse; pakuti sadzalankhula za Iye mwini; koma zinthu zilizonse adzazimva, adzazilankhula; ndipo zinthu zilinkudza adzakulalikirani.
14 Iyeyo adzalemekeza Ine; chifukwa adzatenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu.
15 Zinthu zilizonse Atate ali nazo ndi zanga; chifukwa chake ndinati, kuti atenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu.
Yesu anena za imfa, kuuka, ndikubwera kwake
16 Katsala kanthawi, ndipo simundionanso Ine, ndipo kanthawinso, ndipo mudzandiona Ine.
17 Mwaophunziraake tsono anati wina ndi mnzake, Ichi nchiyani chimene anena ndi ife, Kanthawi ndipo simundione; ndiponso kanthawi, ndipo mudzandiona; ndipo, chifukwa ndimuka kwa Atate?
18 Chifukwa chake ananena. Ichi nchiyani chimene anena, Kanthawi? Sitidziwa chimene alankhula.
19 Yesu anazindikira kuti analikufuna kumfunsa Iye, ndipo anati kwa iwo, Kodi mulikufunsana wina ndi mnzake za ichi, kuti ndinati, Kanthawi ndipo simundiona Ine, ndiponso kanthawi nimudzandiona Ine?
20 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, kuti mudzalira ndi kubuma maliro inu, koma dziko lapansi lidzakondwera; mudzachita chisoni inu, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe.
21 Mkazi pamene akuti abale ali nacho chisoni, chifukwa yafika nthawi yake; koma pamene wabala mwana, sakumbukiranso kusaukako, chifukwa cha chimwemwe kuti wabadwa munthu kudziko lapansi.
22 Ndipo inu tsono muli nacho chisoni tsopano lino, koma ndidzakuonaninso, ndipo mtima wanu udzakondwera, ndipo palibe wina adzachotsa kwa inu chimwemwe chanu.
23 Ndipo tsiku limenelo simudzandifunsa kanthu. Indetu, indetu, ndinena kwa inu, Ngati mudzapempha Atate kanthu, adzakupatsani inu m’dzina langa.
24 Kufikira tsopano simunapemphe kanthu m’dzina langa; pemphani, ndipo mudzalandira, kuti chimwemwe chanu chikwaniridwe.
25 Zinthu izi ndalankhula ndi inu m’mafanizo; ikudza nthawi imene sindidzalankhula ndi inu m’mafanizo, koma ndidzakulalikirani inu m’mafanizo, koma ndidzakulalikirani inu momveka za Atate.
26 Tsiku limenelo mudzapempha m’dzina langa; ndipo sindinena kwa inu kuti Ine ndidzafunsira inu kwa Atate;
27 pakuti Atate yekha akonda inu, chifukwa inu mwandikonda Ine, ndi kukhulupirira kuti Ine ndinatuluka kwa Atate.
28 Ndinatuluka mwa Atate, ndipo ndadza kudziko lapansi: ndilisiyanso dziko lapansi, ndipo ndipita kwa Atate.
29 Ophunzira ake ananena, Onani, tsopano mulankhula zomveka, ndipo mulibe kunena chiphiphiritso.
30 Tsopano tidziwa kuti mudziwa zonse, ndipo mulibe kusowa kuti wina akafunse Inu; mwa ichi tikhulupirira kuti munatuluka kwa Mulungu.
31 Yesu anayankha iwo, Kodi mukhulupirira tsopano?
32 Onani ikudza nthawi, ndipo yafika, imene mudzabalalitsidwa, yense ku zake za yekha, ndipo mudzandisiya Ine pa ndekha. Ndipo sindikhala pa ndekha, chifukwa Atate ali pamodzi ndi Ine,
33 Zinthu izi ndalankhula ndi inu, kuti mwa Ine mukakhale nao mtendere. M’dziko lapansi mudzakhala nacho chivuto, koma limbikani mtima; ndalingonjetsa dziko lapansi Ine.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/16-0d694d9b5dfb2f886a65aff789de101c.mp3?version_id=1068—