Paulo ku Korinto ndi ku Efeso. Abwera ku Yerusalemu
1 Zitapita izi anachoka ku Atene, nadza ku Korinto.
2 Ndipo anapeza Myuda wina dzina lake Akwila, fuko lake la ku Ponto, atachoka chatsopano ku Italiya, pamodzi ndi mkazi wake Prisila, chifukwa Klaudio analamulira Ayuda onse achoke mu Roma; ndipo Paulo anadza kwa iwo:
3 ndipo popeza anali wa ntchito imodzimodzi, anakhala nao, ndipo iwowa anagwira ntchito; pakuti ntchito yao inali yakusoka mahema.
4 Ndipo anafotokozera m’sunagogemasabata onse, nakopa Ayuda ndi Agriki.
5 Koma pamene Silasi ndi Timoteo anadza potsika ku Masedoniya, Paulo anapsinjidwa ndi mau, nachitira umboni kwa Ayuda kuti Yesu ndiyeKhristu.
6 Koma pamene iwo, anamkana, nachita mwano, anakutumula malaya ake, nati kwa iwo, Mwazi wanu ukhale pa mitu yanu; ine ndilibe kanthu; kuyambira tsopano ndinka kwaamitundu.
7 Ndipo anachoka kumeneko, nalowa m’nyumba ya munthu, dzina lake Tito Yusto, amene anapembedza Mulungu, nyumba yake inayandikizana ndi sunagoge.
8 Ndipo Krispo, mkulu wa sunagoge, anakhulupirira Ambuye, ndi apabanja ake onse; ndipo Akorinto ambiri anamva, nakhulupirira, nabatizidwa.
9 Ndipo Ambuye anati kwa Paulo usiku m’masomphenya, Usaope, koma nena, usakhale chete;
10 chifukwa Ine ndili pamodzi ndi iwe, ndipo palibe munthu adzautsana ndi iwe kuti akuipse; chifukwa ndili nao anthu ambiri m’mzinda muno.
11 Ndipo anakhala komwe chaka chimodzi kudza miyezi isanu ndi umodzi; naphunzitsa mau a Mulungu mwa iwo.
12 Tsono pamene Galio anali chiwanga chaAkaya, Ayuda ndi mtima umodzi anamuukira Paulo, nanka naye kumpando wachiweruziro,
13 kuti, Uyu akopa anthu apembedze Mulungu pokana chilamulo.
14 Koma pamene Paulo anati atsegule pakamwa pake, Galio anati kwa Ayuda, Ukadakhala mlandu wa chosalungama, kapena dumbo loipa, Ayuda inu, mwenzi nditakumverani inu;
15 koma akakhala mafunso a mau ndi maina ndi chilamulo chanu; muyang’ane inu nokha; sindifuna kuweruza zimenezi.
16 Ndipo anawapirikitsa pa mpando wachiweruziro.
17 Ndipo anamgwira Sostene, mkulu wa sunagoge, nampanda kumpando wachiweruziro. Ndipo Galio sanasamalire zimenezi.
18 Paulo atakhala chikhalire masiku ambiri, anatsazika abale, nachoka pamenepo, napita m’ngalawa ku Siriya, pamodzi naye Prisila ndi Akwila; popeza anameta mutu wake mu Kenkrea; pakuti adawinda.
19 Ndipo iwo anafika ku Efeso, ndipo iye analekana nao pamenepo: koma iye yekha analowa m’sunagoge, natsutsana ndi Ayuda.
20 Pamene iwo anamfunsa iye kuti akhale nthawi ina yoenjezerapo, sanavomereze;
21 koma anawatsanzika, nati, Akafuna Mulungu, ndidzabwera kwa inu; ndipo anachoka ku Efeso m’ngalawa.
22 Ndipo pamene anakocheza pa Kesareya, anakwera naulonjeraMpingo, natsikira ku Antiokeya.
23 Atakhala kumeneko nthawi, anachoka, napita ku madera osiyanasiyana a dziko la Galatiya ndi la Frijiya, nakhazikitsaophunziraonse.
Apolo ku Efeso ndi Korinto
24 Ndipo anafika ku Efeso Myuda wina dzina lake Apolo, fuko lake la ku Aleksandriya, munthu wolankhula mwanzeru; ndipo anali wamphamvu m’malembo.
25 Iyeyo anaphunzitsidwa m’njira ya Ambuye; pokhala nao mzimu wachangu, ananena ndi kuphunzitsa mosamalira zinthu za Yesu, ndiye wodziwa ubatizo wa Yohane wokha;
26 ndipo iye anayamba kulankhula molimba mtima m’sunagoge, koma pamene anamumva iye Prisila ndi Akwila, anamtenga, namfotokozera njira ya Mulungu mosamalitsa.
27 Ndipo pamene iye anafuna kuoloka kunka ku Akaya, abale anamfulumiza, ndi kulembera makalata kwa ophunzira kuti amlandire: ndipo pamene anafika, iye anathangata ndithu iwo akukhulupirira mwa chisomo;
28 pakuti ndi mphamvu anatsutsa Ayuda, pamaso pa anthu, nasonyeza mwa malembo kuti Yesu ndiye Khristu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/18-c8dc85f4ca22a08cc9e1b020505eca76.mp3?version_id=1068—