Categories
CHIVUMBULUTSO

CHIVUMBULUTSO 10

Yohane adya buku lochokera Kumwamba

1 Ndipo ndinaonamngelowina wolimba alikutsika Kumwamba, wovala mtambo; ndi utawaleza pamutu pake, ndi nkhope yake ngati dzuwa, ndi mapazi ake ngati mizati yamoto;

2 ndipo anali nako m’dzanja lake kabuku kofunyulula: ndipo anaponda nalo phazi lake lamanja panyanja, ndi lamanzerelo pamtunda,

3 nafuula ndi mau aakulu, monga ngati mkango ubangula; ndipo pamene anafuula mabingu asanu ndi awiri analankhula mau ao.

4 Ndipo pamene adalankhula mabingu asanu ndi awiriwo, ndinati ndilembe; ndipo ndinamva mau ochokera Kumwamba nanena, Sindikiza nacho chizindikiro zimene adalankhula mabingu asanu ndi awiri, ndipo usazilembe.

5 Ndipo mngelo amene ndinamuona alikuimirira panyanja ndi pa mtunda, anakweza dzanja lake lamanja kuloza kumwamba,

6 nalumbira kutchula Iye amene ali ndi moyo kunthawi za nthawi, amene analenga m’mwamba ndi zinthu zili momwemo, ndi dziko lapansi ndi zinthu zili momwemo, ndi nyanja ndi zinthu zili momwemo kuti sipadzakhalanso nthawi:

7 komatu m’masiku a mau a mngelo wachisanu ndi chiwiri m’mene iye adzayamba kuomba lipenga, pamenepo padzatsirizika chinsinsi cha Mulungu, monga analalikira kwa akapolo ake aneneri.

8 Ndipo mau ndinawamva ochokera Kumwamba, analankhulanso nane, nanena, Muka, tenga buku lofunyululalo m’dzanja lamngelowakuimirira panyanja ndi padziko.

9 Ndipo ndinamuka kwa mngelo, ndi kunena naye, Ndipatse kabukuko. Ndipo ananena ndi ine, Dzatenge, nudye; ndipo kadzawawitsa m’mimba mwako, komatu m’kamwa mwako kadzazuna ngati uchi.

10 Ndipo ndinatenga kabuku m’dzanja la mngelo, ndipo ndinakadya; ndipo kanali m’kamwa mwanga kozuna ngati uchi; ndipo pamene ndinakadya m’mimba mwanga mudawawa.

11 Ndipo ananena nane, Uyenera iwe kuneneranso pa anthu ndi mitundu, ndi manenedwe, ndi mafumu ambiri.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/REV/10-255f531b57fa1bcabc3abc98e9957113.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *