Categories
1 AKORINTO

1 AKORINTO 1

1 Paulo, woitanidwa akhalemtumwiwaKhristuYesu mwa chifuniro cha Mulungu, ndi Sostene mbaleyo,

2 kwaMpingowa Mulungu wakukhala mu Korinto, ndiwo oyeretsedwa mwa Khristu Yesu, oitanidwa akhale oyera mtima, pamodzi ndi onse akuitana pa dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu, m’malo monse, ndiye wao, ndi wathu:

3 Chisomo kwa inu ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Khristu.

4 Ndiyamika Mulungu wanga nthawi yonse kaamba ka inu, chifukwa cha chisomo cha Mulungu chinapatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu;

5 kuti m’zonse munalemezedwa mwa Iye, m’mau onse, ndi chidziwitso chonse;

6 monga umboni wa Khristu unakhazikika mwa inu;

7 kotero kuti sichikusowani inu chaufulu chilichonse; pakulindira inu vumbulutso la Ambuye wathu Yesu Khristu;

8 amenenso adzakukhazikitsani inu kufikira chimaliziro, kuti mukhale opanda chifukwa m’tsiku la Ambuye wathu Yesu Khristu.

9 Mulungu ali wokhulupirika amene munaitanidwa mwa Iye, ku chiyanjano cha Mwana wake Yesu Khristu, Ambuye wathu.

Malekano mu Mpingo wa ku Korinto

10 Koma ndikudandaulirani inu, abale, mwa dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti munene chimodzimodzi inu nonse, ndi kuti pasakhale malekano pakati pa inu; koma mumangike mu mtima womwewo ndi m’chiweruziro chomwecho.

11 Pakuti zinamveka kwa ine za inu, abale anga, ndi iwo a kwa Koloe, kuti pali makani pakati pa inu.

12 Koma ichi ndinena, kuti yense wa inu anena, Ine ndine wa Paulo; koma ine wa Apolo; koma ine wa Kefa; koma ine wa Khristu.

13 Kodi Khristu wagawika? Kodi Paulo anapachikidwa chifukwa cha inu? Kapena kodi munabatizidwa m’dzina la Paulo?

14 Ndiyamika Mulungu kuti sindinabatize mmodzi yense wa inu, koma Krispo ndi Gayo;

15 kuti anganene mmodzi kuti mwabatizidwa m’dzina langa.

16 Koma ndinabatizanso a pa banja la Stefanasi; za ena, sindidziwa ngati ndinabatiza wina yense.

Nzeru za Mulungu ndi nzeru za anthu

17 Pakuti Khristu sananditume ine kubatiza, koma kulalikira Uthenga Wabwino, si mu nzeru ya mau, kuti mtanda wa Khristu ungayesedwe wopanda pake.

18 Pakuti mau a mtanda ali ndithu chinthu chopusa kwa iwo akutayika, koma kwa ife amene tilikupulumutsidwa ali mphamvu ya Mulungu.

19 Pakuti kulembedwa,

Ndidzaononga nzeru za anzeru,

ndi kuchenjera kwa ochenjera ndidzakutha.

20 Ali kuti wanzeru? Mlembi ali kuti? Ali kuti wotsutsana wa nthawi ya pansi pano? Kodi Mulungu sanaipusitse nzeru ya dziko lapansi?

21 Pakuti popeza m’nzeru ya Mulungu dziko lapansi, mwa nzeru yake, silinadziwe Mulungu, chidamkonda Mulungu kupulumutsa okhulupirirawo mwa chopusa cha kulalikira.

22 Ndipo popeza Ayuda afunsa zizindikiro, ndi Agriki atsata nzeru:

23 koma ife tilalikira Khristu wopachikidwa, kwa Ayudatu chokhumudwitsa, ndi kwaamitunduchinthu chopusa;

24 koma kwa iwo oitanidwa, ndiwo Ayuda ndi Agriki, Khristu mphamvu ya Mulungu, ndi nzeru ya Mulungu.

25 Chifukwa kuti chopusa cha Mulungu chiposa anthu ndi nzeru zao; ndipo chofooka cha Mulungu chiposa anthu ndi mphamvu yao.

26 Pakuti penyani maitanidwe anu, abale, kuti saitanidwa ambiri anzeru, monga mwa thupi; ambiri amphamvu, mfulu zambiri, iai;

27 koma Mulungu anasankhula zopusa za dziko lapansi, kuti akachititse manyazi anzeru; ndipo zofooka za dziko lapansi Mulungu anazisankhula, kuti akachititse manyazi zamphamvu;

28 ndipo zopanda pake za dziko lapansi, ndi zonyozeka, anazisankhula Mulungu, ndi zinthu zoti kulibe; kuti akathere zinthu zoti ziliko;

29 kuti thupi lililonse lisadzitamande pamaso pa Mulungu.

30 Koma kwa Iye muli inu mwa Khristu Yesu, amene anayesedwa kwa ife nzeru ya kwa Mulungu, ndi chilungamo ndi chiyeretso ndi chiombolo;

31 kuti monga mwalembedwa, Iye amene adzitamanda, adzitamande mwa Ambuye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CO/1-b38ecac648833b699fe0eb34517e06a1.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *