Categories
1 AKORINTO

1 AKORINTO 3

Chifukwa cha malekano ao

1 Ndipo ine, abale, sindinathe kulankhula ndi inu monga ndi auzimu, koma monga athupi, monga makanda mwaKhristu.

2 Ndinadyetsa inu mkaka, si chakudya cholimba ai; pakuti simungachithe; ngakhale tsopano lino simungachithe; pakuti mulinso athupi;

3 pakuti, pokhala pali nkhwidzi ndi ndeu pakati pa inu simuli athupi kodi, ndi kuyendayenda monga mwa munthu?

4 Pakuti pamene wina anena, Ine ndine wa Paulo; koma mnzake, Ndine wa Apolo; simuli anthu kodi?

5 Ndipo Apolo nchiyani, ndi Paulo nchiyani? Atumiki amene munakhulupirira mwa iwo, yense monga Ambuye anampatsa.

6 Ndinaoka ine, anathirira Apolo; koma Mulungu anakulitsa.

7 Chotero sali kanthu kapena wookayo, kapena wothirirayo; koma Mulungu amene akulitsa.

8 Koma wookayo ndi wothirirayo ali amodzi; koma yense adzalandira mphotho yake ya iye yekha, monga mwa kuchititsa kwake kwa iye yekha.

Akhristu ali nyumba ya Mulungu, Yesu ali maziko a nyumbayi

9 Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; chilimo cha Mulungu, chimango cha Mulungu ndi inu.

10 Monga mwa chisomo cha Mulungu chidapatsidwa kwa ine, ngati mwini mamangidwe waluso, ndinaika maziko, koma wina amangapo. Koma yense ayang’anire umo amangira pamenepo.

11 Pakuti palibe munthu akhoza kuika maziko ena, koma amene aikidwako, ndiwo YesuKhristu.

12 Koma ngati wina amanga pa mazikowo, golide,siliva, miyala ya mtengo wake, mtengo, udzu, dziputu,

13 ntchito ya yense idzaonetsedwa; pakuti tsikulo lidzaisonyeza, chifukwa kuti yavumbululuka m’moto; ndipo moto wokha udzayesera ntchito ya yense ikhala yotani.

14 Ngati ntchito ya munthu aliyense ikhala imene anaimangako, adzalandira mphotho.

15 Ngati ntchito ya wina itenthedwa, zidzaonongeka zake; koma iye yekha adzapulumutsidwa; koma monga momwe mwa moto.

16 Kodi simudziwa kuti muli Kachisi wa Mulungu, ndi kuti Mzimu wa Mulungu agonera mwa inu?

17 Ngati wina aononga Kachisi wa Mulungu, ameneyo Mulungu adzamuononga; pakuti Kachisi wa Mulungu ali wopatulika, ameneyo ndi inu.

18 Munthu asadzinyenge yekha; ngati wina ayesa kuti ali wanzeru mwa inu m’nthawi ino ya pansi pano, akhale wopusa, kuti akakhale wanzeru.

19 Pakuti nzeru ya dziko lino lapansi ili yopusa kwa Mulungu. Pakuti kwalembedwa, Iye agwira anzeru m’chenjerero lao;

20 ndiponso Ambuye azindikira zolingirira za anzeru, kuti zili zopanda pake.

21 Chifukwa chake palibe mmodzi adzitamande mwa anthu. Pakuti zinthu zonse nzanu;

22 ngati Paulo, kapena Apolo, kapena Kefa, kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena za makono ano, kapena zilinkudza; zonse ndi zanu;

23 koma inu ndinu a Khristu; ndi Khristu ndiye wa Mulungu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CO/3-d6ab084e105bccde0d74c47193e7fa22.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *