Categories
1 AKORINTO

1 AKORINTO 8

Kunena za kudya nyama yoperekedwa nsembe kwa mafano

1 Koma za zoperekedwa nsembe kwa mafano: Tidziwa kuti tili nacho chidziwitso tonse. Chidziwitso chitukumula, koma chikondi chimangirira.

2 Ngati wina ayesa kuti adziwa kanthu sanayambe kudziwa monga ayenera kudziwa.

3 Koma ngati wina akonda Mulungu, yemweyu adziwika ndi Iye.

4 Tsono kunena za kudya zoperekedwa nsembe kwa mafano, tidziwa kuti fano silili kanthu padziko lapansi, ndi kuti palibe Mulungu koma mmodzi.

5 Pakuti ngakhalenso iliko yoti yonenedwa milungu, kapena m’mwamba, kapena padziko lapansi, monga iliko milungu yambiri, ndi ambuye ambiri;

6 koma kwa ife kuli Mulungu mmodzi, Atate amene zinthu zonse zichokera kwa Iye, ndi ife kufikira kwa Iye; ndi Ambuye mmodzi YesuKhristu, amene zinthu zonse zili mwa Iye, ndi ife mwa Iye.

7 Komatu chidziwitso sichili mwa onse; koma ena, ozolowera fano kufikira tsopano, adyako monga yoperekedwa nsembe kwa fano; ndipo chikumbumtima chao, popeza nchofooka, chidetsedwa.

8 Koma chakudya sichitivomerezetsa kwa Mulungu; kapena ngati sitidya sitisowa; kapena ngati tidya tilibe kupindulako.

9 Koma yang’anirani kuti ulamuliro wanu umene ungakhale chokhumudwitsa ofookawo.

10 Pakuti wina akaona iwe amene uli nacho chidziwitso, ulikukhala pachakudya mu Kachisi wa fano, kodi chikumbumtima chake, popeza ali wofooka, sichidzalimbika kudya zoperekedwa nsembe kwa mafano?

11 Pakuti mwa chidziwitso chako wofookayo atayika, ndiye mbale amene Khristu anamfera.

12 Koma pakuchimwira abale, ndi kulasa chikumbumtima chao chofooka, muchimwira kotero Khristu.

13 Chifukwa chake, ngati chakudya chikhumudwitsa mbale wanga, sindidzadya nyama kunthawi yonse, kuti ndingakhumudwitse mbale wanga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CO/8-438bb66241a7b56ca0560c0f2ca78999.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *