Categories
1 AKORINTO

1 AKORINTO 16

Zopereka za kwa Akhristu a ku Yerusalemu

1 Koma za chopereka cha kwa oyera mtima, monga ndinalangizaMipingoya ku Galatiya, motero chitani inunso.

2 Tsiku loyamba la sabata yense wa inu asunge yekha, monga momwe anapindula, kuti zopereka zisachitike pakudza ine.

3 Ndipo pamene ndifika, ndidzatuma iwo amene mudzawayesa oyenera, ndi makalata, apite nayo mphatso yanu kuYerusalemu.

4 Ndipo ngati kuyenera kwa ine kupitanso, adzapita nane.

Za maulendo akudza, ndi malonje a Paulo

5 Koma ndidzadza kwa inu, nditapyola Masedoniya; pakuti ndidzapyola Masedoniya;

6 ndipo kapena ndidzakhalitsa ndi inu, kapenanso kugonera nyengo yachisanu kuti mukandiperekeze ine kumene kulikonse ndipitako.

7 Pakuti sindifuna kukuonani tsopano popitirira; pakuti ndiyembekeza kukhala ndi inu nthawi, ngati alola Ambuye.

8 Koma ndidzakhala ku Efeso kufikiraPentekoste.

9 Pakuti panditsegukira pa khomo lalikulu ndi lochititsa, ndipo oletsana nafe ndi ambiri.

10 Koma akadza Timoteo, penyani kuti akhale ndi inu wopanda mantha; pakuti agwira ntchito ya Ambuye, monganso ine;

11 chifukwa chake munthu asampeputse. Koma mumperekeze mumtendere, kuti akadze kwa ine; pakuti ndimuyembekezera pamodzi ndi abale.

12 Koma za Apolo, mbaleyo, ndamuumiriza iye, adze kwa inu pamodzi ndi abale; ndipo sichinali chifuniro chake kuti adze tsopano, koma adzafika pamene aona nthawi.

13 Dikirani, chilimikani m’chikhulupiriro, dzikhalitseni amuna, limbikani.

14 Zanu zonse zichitike m’chikondi.

15 Koma ndikupemphani inu, abale, (mudziwa banja la Stefanasi, kuti ali chipatso choyamba chaAkaya, ndi kuti anadziika okha kutumikira oyera mtima),

16 kuti inunso muvomere otere, ndi yense wakuchita nao, ndi kugwiritsa ntchito.

17 Koma ndikondwera pa kudza kwao kwa Stefanasi, ndi Fortunato, ndi Akaiko; chifukwa iwo anandikwaniritsa chotsalira chanu.

18 Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu; chifukwa chake muzindikire otere.

19 Mipingo ya ku Asiya ikupatsani moni. Akupatsani moni ndithu inu mwa Ambuye, Akwila ndi Prisika, pamodzi ndi Mpingo wa m’nyumba yao.

20 Akupatsani moni abale onse. Mupatsane moni ndi kupsompsonana kopatulika.

21 Ndikupereka moni ine Paulo ndi dzanja langa.

22 Ngati wina sakonda Ambuye, akhale wotembereredwa. Akudza Ambuye.

23 Chisomo cha Ambuye YesuKhristuchikhale ndi inu.

24 Chikondi changa chikhale ndi inu nonse mwa Khristu Yesu.Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CO/16-ace8df393251fd7d667478e3f41aadd2.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *