Categories
GENESIS

GENESIS 37

Yosefe agulitsidwa ndi abale ake

1 Ndipo Yakobo anakhala m’dziko limene anakhalamo mlendo atate wake, m’dziko la Kanani.

2 Mibadwo ya Yakobo ndi iyi; Yosefe anali wa zaka khumi ndi zisanu ndi ziwiri analinkudyetsa zoweta pamodzi ndi abale ake; ndipo anali mnyamata pamodzi ndi ana a Biliha, ndi ana aamuna a Zilipa, akazi a atate wake; ndipo Yosefe anamfotokozera atate wake mbiri yao yoipa.

3 Koma Israele anamkonda Yosefe koposa ana ake onse, pakuti anali mwana wa ukalamba wake; ndipo anamsokera iye malaya amwinjiro.

4 Ndipo abale ake anaona kuti atate wake anamkonda iye koposa abale ake onse: ndipo anamuda iye, ndipo sanathe kulankhula ndi iye mwamtendere.

5 Yosefe ndipo analota loto, nawafotokozera abale ake; ndipo anamuda iye koposa.

6 Ndipo iye anati kwa iwo, Tamvanitu loto limene ndalota:

7 pakuti taonani, ndinalinkumanga mitolo m’munda, ndipo taonani, mtolo wanga unauka nuima chilili! Ndipo taonani, mitolo yanu inadza niuzinga kwete, niuweramira mtolo wanga.

8 Abale ake ndipo anati kwa iye, Kodi udzakhala mfumu yathu ndithu? Kapena udzatilamulira ife ndithu kodi? Ndipo anamuda iye koposa chifukwa cha maloto ake ndi mau ake.

9 Ndipo analotanso loto lina, nafotokozera abale ake, nati, Taonani, ndalotanso loto lina: ndipo taonani, dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi khumi ndi imodzi zinandiweramira ine.

10 Ndipo iye anafotokozera atate wake ndi abale ake; ndipo atate wake anamdzudzula, nati kwa iye, Loto limene walota iwe nlotani? Kodi ine ndi amai ako ndi abale ako tidzafika ndithu tokha kuweramira iwe pansi?

11 Ndipo abale ake anamchitira iye nsanje, koma atate wake anasunga mau amene m’mtima mwake.

12 Ndipo abale ake ananka kukaweta zoweta za atate wao mu Sekemu.

13 Ndipo Israele anati kwa Yosefe, Kodi abale ako sadyetsa zoweta mu Sekemu? Tiyeni, ndikutuma iwe kwa iwo. Ndipo anati, Ndine pano.

14 Ndipo anati kwa iye, Pita tsopano, nukaone ngati abale ako ali bwino, ndi ngati zoweta zili bwino; nundibwezere ine mau. Ndipo anamtuma iye kuchokera m’chigwa cha Hebroni, ndipo anadza ku Sekemu.

15 Ndipo anampeza munthu, taonani, analinkusokera m’thengo; munthuyo ndipo anamfunsa, nati, Kodi ufuna chiyani?

16 Ndipo iye anati, Ndifuna abale anga. Undiuzetu kumene adyetsa zoweta.

17 Munthuyo ndipo anati, Anachoka pano; pakuti ndinamva alinkuti, Timuke ku Dotani. Yosefe ndipo anatsata abale ake, nawapeza ali ku Dotani.

18 Ndipo iwo anamuona iye ali patali, ndipo asanayandikire pafupi ndi iwo, anampangira iye chiwembu kuti amuphe.

19 Ndipo anati wina ndi mnzake, Taonani, alinkudza mwini maloto uja.

20 Tiyeni tsopano timuphe iye timponye m’dzenje, ndipo tidzati, Wajiwa ndi chilombo; ndipo tidzaona momwe adzachita maloto ake.

21 Ndipo Rubeni anamva nampulumutsa iye m’manja mwao; nati, Tisamuphe iye.

22 Ndipo Rubeni anati kwa iwo, Musakhetse mwazi; mponyeni iye m’dzenjemo m’chipululu muno, koma musamsamulire iye manja: kuti ampulumutse iye m’manja mwao, ambwezenso kwa atate wake.

23 Ndipo panali pamene Yosefe anafika kwa abale ake, anamvula Yosefe malaya ake, malaya amwinjiro amene anavala iye;

24 ndipo anamtenga iye, namponya m’dzenjemo; m’dzenjemo munalibe kanthu, munalibe madzi m’menemo.

25 Ndipo iwo anakhala pansi kuti adye chakudya; ndipo anatukula maso ao, nayang’ana, ndipo taonani, ulendo wa Aismaele anachokera ku Giliyadi ndingamirazao, zilinkunyamula zonunkhira ndi mafuta amankhwala ndimurealinkumuka kutsikira nazo ku Ejipito.

26 Ndipo Yuda anati kwa abale ake, Nanga tidzapindulanji tikamupha mbale wathu ndi kufotsera mwazi wake?

27 Tiyeni timgulitse iye kwa Aismaele, tisasamulire iye manja; chifukwa ndiye mbale wathu, thupi lathu. Ndipo anamvera iye abale ake.

28 Ndipo anapita pamenepo Amidiyani a malonda: ndipo anamtulutsa namkweza Yosefe m’dzenjemo, namgulitsa kwa Aismaele ndi masekeli asilivamakumi awiri; ndipo ananka naye Yosefe ku Ejipito.

29 Ndipo Rubeni anabwera kudzenje, ndipo taonani, Yosefe mulibe m’dzenjemo: ndipo iye anang’amba nsalu yake.

30 Ndipo anabwera kwa abale ake, nati, Mwana palibe; ndipo ine ndipita kuti?

31 Ndipo anatenga malaya ake a Yosefe, napha tonde, naviika malaya m’mwazi wake:

32 natumiza malaya amwinjiro, nadza nao kwa atate ao: ndipo anati, Siwa tawatola; muzindikire tsono ngati ndi malaya a mwana wanu, kapena ndi ena.

33 Ndipo anazindikira nati, Ndiwo malaya a mwana wanga: wajiwa ndi chilombo: Yosefe wakadzulidwa ndithu.

34 Yakobo ndipo anang’amba malaya ake, na vala chiguduli m’chuuno mwake namlirira mwana wake masiku ambiri.

35 Ndipo ana aamuna ake onse ndi ana aakazi onse anauka kuti amtonthoze: koma anakana kutonthozedwa; ndipo anati, Pakuti ndidzatsikira kumanda kwa mwana wanga, ndilinkulirabe. Atate wake ndipo anamlirira.

36 Amidiyani ndipo anamgulitsa iye anke ku Ejipito kwa Potifara, nduna yaFarao, kazembe wa alonda.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GEN/37-3b270ffe47ca8aa108e99e21d2dcc680.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *