Achita Paska
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m’chipululu cha Sinai, mwezi woyamba wa chaka chachiwiri atatuluka m’dziko la Ejipito, ndi kuti,
2 Ana a Israele achitePaskapa nyengo yoikidwa.
3 Tsiku lakhumi ndi chinai la mweziwo, madzulo, muziuchita, pa nyengo yake yoikidwa; muuchite monga mwa malemba ake onse, ndi maweruzo ake onse.
4 Ndipo Mose ananena ndi ana a Israele, kuti achite Paska.
5 Ndipo anachita Paska mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi chinai la mweziwo, madzulo m’chipululu cha Sinai; monga mwa zonse Yehova adauza Mose, momwemo ana a Israele anachita.
6 Pamenepo panali amuna, anadetsedwa ndi mtembo wa munthu, ndipo sanakhoze kuchita Paska tsiku lomwelo; m’mwemo anafika pamaso pa Mose ndi pamaso pa Aroni tsiku lomwelo;
7 nanena naye amunawa, Tadetsedwa ife ndi mtembo wa munthu; atiletseranji, kuti tisabwere nacho chopereka cha Yehova pa nyengo yake yoikidwa, pakati pa ana a Israele?
8 Ndipo Mose ananena nao, Baimani; ndimve chouza Yehova za inu.
9 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
10 Nena ndi ana a Israele, ndi kuti, Angakhale munthu wa inu kapena wa mibadwo yanu, adetsedwa, chifukwa cha mtembo, kapena pokhala paulendo, koma azichitira Yehova Paska.
11 Mwezi wachiwiri, tsiku lake lakhumi ndi chinai, madzulo, auchite; audye ndi mkate wopanda chotupitsa ndi msuzi wowawa.
12 Asasiyeko kufikira m’mawa, kapena kuthyolapo fupa; auchite monga mwa lemba lonse la Paska.
13 Munthu akakhala woyera, wosakhala paulendo, koma akaleka kuchita Paska, amsadze munthuyo kwa anthu a mtundu wake; popeza sanabwere nacho chopereka cha Yehova pa nyengo yake yoikidwa, munthuyu asenze kuchimwa kwake.
14 Ndipo mlendo akakhala mwa inu, nakachitira Yehova Paska, azichita monga mwa lemba la Paska, ndi monga mwa chiweruzo chake; lemba likhale limodzi kwa inu, ndi kwa mlendo, ndi kwa wobadwa m’dziko.
Mtambo pamwamba pa Kachisi
15 Ndipo tsiku loutsa Kachisi mtambo unaphimba Kachisi, ndiwochihema chokomanako; ndicho chihema chaumboni, ndipo madzulo padaoneka pa Kachisi ngati moto, kufikira m’mawa.
16 Kudatero kosalekeza; mtambo umachiphimba, ndi moto umaoneka usiku.
17 Ndipo pokwera mtambo kuchokera kuchihema, utatero ana a Israele amayenda ulendo wao; ndipo pamalo pokhala mtambo, pamenepo ana a Israele amamanga mahema ao.
18 Pakuwauza Yehova ana a Israele amayenda ulendo, powauza Yehova amamanga mahema ao; masiku onse mtambo ukakhala pamwamba pa chihema amakhala m’chigono.
19 Ndipo pakukhalitsa mtambo masiku ambiri pamwamba pa chihema, pamenepo ana a Israele anasunga udikiro wa Yehova osayenda ulendo.
20 Ndipo pokhala mtambo pamwamba pa chihema masiku pang’ono; pamenepo anakhala m’chigono monga awauza Yehova, nayendanso ulendo monga anauza Yehova.
21 Koma mtambo ukakhala kuyambira madzulo kufikira m’mawa; pokwera mtambo m’mawa, ayenda ulendo.
22 Ngakhale masiku awiri, kapena mwezi, kapena masiku ambiri, pokhalitsa mtambo pamwamba pa chihema ndi kukhalapo, ana a Israele anakhala m’chigono, osayenda ulendo; koma pakukwera uwu, anayenda ulendo.
23 Powauza Yehova amanga mahema, powauza Yehova ayenda ulendo; anasunga udikiro wa Yehova powauza Yehova mwa dzanja la Mose.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/9-7401ea656470e41cd4b00b8b6ed75cc5.mp3?version_id=1068—