Categories
NUMERI

NUMERI 27

Ana aakazi a Zelofehadi

1 Pamenepo anayandikiza ana aakazi a Zelofehadi mwana wa Hefere, ndiye mwana wa Giliyadi, ndiye mwana wa Makiri, ndiye mwana wamwamuna wa Manase, wa mabanja a Manase mwana wa Yosefe; ndipo maina a ana ake aakazi ndiwo, Mala, Nowa, Hogila ndi Milika ndi Tiriza.

2 Ndipo anaima pamaso pa Mose, ndi pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa akalonga; ndi khamu lonse, pakhomo pachihema chokomanako, ndi kuti,

3 Atate wathu adamwalira m’chipululu, ndipo sanakhale iye pakati pa msonkhano wa iwo akusonkhana kutsutsana ndi Yehova, mu msonkhano wa Kora; koma anafera zoipa zakezake; ndipo analibe ana aamuna.

4 Lichotsedwerenji dzina la atate wathu pakati pa banja lake, popeza alibe mwana wamwamuna? Tipatseni dziko lathulathu pakati pa abale a atate wathu.

5 Ndipo Mose anapita nao mlandu wao pamaso pa Yehova.

6 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

7 Ana aakazi a Zelofehadi anena zoona; uwapatse ndithu cholowa chikhale chaochao pakati pa abale a atate wao; nuwalandiritse cholowa cha atate wao.

8 Ndipo unene ndi ana a Israele, ndi kuti, Akafa munthu wamwamuna wopanda mwana wamwamuna, cholowa chake achilandire mwana wake wamkazi.

9 Ndipo akapanda kukhala naye mwana wamkazi, mupatse abale ake cholowa chake.

10 Ndipo akapanda kukhala nao abale, mupatse abale a atate wake cholowa chake.

11 Ndipo akapanda abale a atate wake, mupatse wa chibale wake woyandikizana naye wa fuko lake cholowa chake, likhale lakelake; ndipo likhale kwa ana a Israele lemba monga Yehova wamuuza Mose.

Aikidwa Yoswa m’malo mwa Mose

12 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Kwera m’phiri ili la Abarimu, nupenye dziko limene ndapatsa ana a Israele.

13 Utaliona iwenso udzaitanidwa kunka kwa anthu a mtundu wako, monga anaitanidwa Aroni mbale wako;

14 popeza munapikisana nao mau anga m’chipululu cha Zini, potsutsana nane khamulo, osandipatula Ine pamadziwo pamaso pao. Ndiwo madzi a Meriba mu Kadesi, m’chipululu cha Zini.

15 Ndipo Mose ananena ndi Yehova, nati,

16 Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, aike munthu pa khamulo,

17 wakutuluka pamaso pao, ndi kulowa pamaso pao, wakuwatulutsa ndi kuwalowetsa; kuti khamu la Yehova lisakhale ngati nkhosa zopanda mbusa.

18 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Utenge Yoswa mwana wa Nuni, ndiye munthu mwa iye muli mzimu, nuike dzanja lako pa iye;

19 numuimike pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse; numlangize pamaso pao.

20 Ndipo umuikirepo ulemerero wako, kuti khamu lonse la ana a Israele ammvere.

21 Ndipo aime pamaso pa Eleazara wansembe, amene amfunsire monga mwa chiweruzo cha Urimu pamaso pa Yehova; ponena iye azituluka, ndi ponena iye azilowa, ndi iye ndi ana onse a Israele pamodzi naye, ndiwo khamu lonse.

22 Ndipo Mose anachita monga Yehova adamuuza; natenga Yoswa namuimitsa pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse;

23 namuikira manja ake, namlangiza monga Yehova adanena ndi dzanja la Mose.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/27-075e919676b2dfbd47132f5c049260e8.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *