Chipulumutso chichokera kuchisomo
1 Ndipo inu, anakupatsani moyo, pokhala munali akufa ndi zolakwa, ndi zochimwa zanu,
2 zimene munayendamo kale, monga mwa mayendedwe a dziko lapansi lino, monga mwa mkulu wa ulamuliro wa mlengalenga, wa mzimu wakuchita tsopano mwa ana a kusamvera;
3 amene ife tonsenso tinagonera pakati pao kale, m’zilakolako za thupi lathu, ndi kuchita zifuniro za thupi, ndi za maganizo, ndipo tinali ana a mkwiyo chibadwire, monganso otsalawo;
4 koma Mulungu, wolemera chifundo, chifukwa cha chikondi chake chachikulu chimene anatikonda nacho,
5 tingakhale tinali akufa m’zolakwa zathu, anatipatsa moyo pamodzi ndiKhristu(muli opulumutsidwa ndi chisomo),
6 ndipo anatiukitsa pamodzi, natikhazikitsa pamodzi m’zakumwamba mwaKhristuYesu;
7 kuti akaonetsere m’nthawi zilinkudza chuma choposa cha chisomo chake, m’kukoma mtima kwa pa ife mwa Khristu Yesu.
8 Pakuti muli opulumutsidwa ndi chisomo chakuchita mwa chikhulupiriro, ndipo ichi chosachokera kwa inu: chili mphatso ya Mulungu;
9 chosachokera kuntchito, kuti asadzitamandire munthu aliyense.
10 Pakuti ife ndife chipango chake, olengedwa mwa Khristu Yesu, kuchita ntchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m’menemo.
Ayuda ndi amitundu ayanjanitsidwa ndi Mulungu mwa mtanda wa Khristu
11 Momwemo kumbukirani, kuti kale inuamitundum’thupi, otchedwa kusadulidwa ndi iwo otchedwamdulidwem’thupi, umene udachitika ndi manja;
12 kuti nthawi ija munali opanda Khristu, alendo a padera ndi mbumba ya Israele, ndi alendo alibe kanthu ndi mapangano a malonjezano, opanda chiyembekezo, ndi opanda Mulungu m’dziko lapansi.
13 Koma tsopano mwa Khristu Yesu inu amene munali kutali kale, anakusendezani mukhale pafupi m’mwazi wa Khristu.
14 Pakuti Iye ndiye mtendere wathu, amene anachita kuti onse awiri akhale mmodzi, nagumula khoma lakudulitsa pakati,
15 atachotsa udani m’thupi lake, ndiwo mau a chilamulo cha kutchulako malangizo; kuti alenge awiriwa mwa Iye yekha, akhale munthu mmodzi watsopano, ndi kuchitapo mtendere;
16 ndi kuti akayanjanitse awiriwa ndi Mulungu, m’thupi limodzi mwa mtandawo, atapha nao udaniwo;
17 ndipo m’mene anadza, analalikira Uthenga Wabwino wa mtendere kwa inu akutali, ndi mtendere kwa iwo apafupi;
18 kuti mwa Iye ife tonse awiri tili nao malowedwe athu kwa Atate, mwa Mzimu mmodzi.
19 Pamenepo ndipo simulinso alendo ndi ogonera, komatu muli a mudzi womwewo wa oyera mtima ndi a banja la Mulungu;
20 omangika pa maziko aatumwindi aneneri, pali Khristu Yesu mwini, mwala wa pangodya;
21 mwa Iye chimango chonse cholumikizika pamodzi bwino, chikula, chikhale Kachisi wopatulika mwa Ambuye;
22 chimene inunso mumangidwamo pamodzi, mukhale chokhalamo Mulungu mwa Mzimu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EPH/2-054984f16af14989be1bea8f545f37dd.mp3?version_id=1068—