Categories
AEFESO

AEFESO 4

Umodzi wa iwo a chikhulupiriro

1 Ndikudandaulirani inu tsono, ine wandende mwa Ambuye, muyende koyenera maitanidwe amene munaitanidwa nao,

2 ndi kuonetsera kudzichepetsa konse, ndi chifatso, ndi kuonetsera chipiriro, ndi kulolerana wina ndi mnzake, mwa chikondi;

3 ndi kusamalitsa kusunga umodzi wa Mzimu mwa chimangiriro cha mtendere.

4 Thupi limodzi ndi Mzimu mmodzi, monganso anakuitanani m’chiyembekezo chimodzi cha maitanidwe anu;

5 Ambuye mmodzi, chikhulupiriro chimodzi, ubatizo umodzi,

6 Mulungu mmodzi ndi Atate wa onse amene ali pamwamba pa onse, ndi mwa onse, ndi m’kati mwa zonse.

7 Ndipo kwa yense wa ife chapatsika chisomo, monga mwa muyeso wa mphatso yaKhristu.

8 Chifukwa chake anena,

M’mene anakwera kumwamba, anamanga ndende undende,

naninkha zaufulu kwa anthu.

9 Koma ichi, chakuti, Anakwera, nchiyani nanga koma kuti anatsikiranso ku madera a kunsi kwa dziko?

10 Iye wotsikayo ndiye yemweyonso anakwera, popitiriratu miyamba yonse, kuti akadzaze zinthu zonse.

11 Ndipo Iye anapatsa ena akhaleatumwi; ndi ena aneneri; ndi ena alaliki; ndi ena abusa, ndi ena aphunzitsi;

12 kuti akonzere oyera mtima kuntchito ya utumiki, kumangirira thupi la Khristu;

13 kufikira ife tonse tikafikira ku umodzi wa chikhulupiriro, ndi wa chizindikiritso cha Mwana wa Mulungu, kwa munthu wangwiro, ku muyeso wa msinkhu wa chidzalo cha Khristu.

14 Kuti tisakhalenso makanda, ogwedezekagwedezeka, natengekatengeka ndi mphepo yonse ya chiphunzitso, ndi tsenga la anthu, ndi kuchenjerera kukatsata chinyengo cha kusocheretsa;

15 koma ndi kuchita zoona mwa chikondi tikakule m’zinthu zonse, kufikira Iye amene ali mutu ndiye Khristu;

16 kuchokera mwa Iye thupi lonse, lolukidwa ndi lolumikizidwa pamodzi, pothandizanapo mfundo yonse, monga mwa kuchititsa kwa chiwalo chonse pa muyeso wake, lichita makulidwe a thupi, kufikira chimango chake mwa chikondi.

Kusiyana kwa kuyera mtima kwa Chikhristu ndi mayendedwe oipa a akunja

17 Pamenepo ndinena ichi, ndipo ndichita umboni mwa Ambuye, kuti simuyendanso inu mongansoamitunduangoyenda, m’chitsiru cha mtima wao,

18 odetsedwa m’nzeru zao, oyesedwa alendo pa moyo wa Mulungu, chifukwa cha chipulukiro chili mwa iwo, chifukwa cha kuumitsa kwa mitima yao;

19 amenewo popeza sazindikiranso kanthu konse, anadzipereka okha kuti akhumbe zonyansa, kuti achite chidetso chonse mu umbombo.

20 Koma inu simunaphunzire Khristu chotero,

21 ngatitu mudamva Iye, ndipo munaphunzitsidwa mwa Iye, monga choonadi chili mwa Yesu;

22 kuti muvule, kunena za makhalidwe anu oyamba, munthu wakale, wovunda potsata zilakolako za chinyengo;

23 koma kuti mukonzeke, mukhale atsopano mu mzimu wa mtima wanu,

24 nimuvale munthu watsopano, amene analengedwa monga mwa Mulungu, m’chilungamo, ndi m’chiyero cha choonadi.

25 Mwa ichi, mutataya zonama, lankhulani zoona yense ndi mnzake; pakuti tili ziwalo wina ndi mnzake.

26 Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,

27 ndiponso musampatse malo mdierekezi.

28 Wakubayo asabenso; koma makamaka agwiritse ntchito, nagwire ntchito yokoma ndi manja ake, kuti akhale nacho chakuchereza wosowa.

29 Nkhani yonse yovunda isatuluke m’kamwa mwanu, koma ngati pali ina yabwino kukumangirira monga mofunika ndiyo, kuti ipatse chisomo kwa iwo akumva.

30 Ndipo musamvetse chisoni Mzimu Woyera wa Mulungu, amene munasindikizidwa chizindikiro mwa Iye, kufikira tsiku la maomboledwe.

31 Chiwawo chonse, ndi kupsa mtima, ndi mkwiyo, ndi chiwawa, ndi mwano zichotsedwe kwa inu, ndiponso choipa chonse.

32 Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzake, a mtima wachifundo, akukhululukirana nokha, monganso Mulungu mwa Khristu anakhululukira inu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EPH/4-257090310aea5a1baec5e980b2138c2f.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *