Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 23

Oletsedwa ku msonkhano wa Yehova

1 Munthu wofulika kapena woduka chiwalo chaumuna, asalowe m’msonkhano wa Yehova.

2 Mwana wa m’chigololo asalowe m’msonkhano wa Yehova, ngakhale mbadwo wake wakhumi usalowe m’msonkhano wa Yehova.

3 Mwamoni kapena Mmowabu asalowe m’msonkhano wa Yehova; ngakhale mbadwo wao wakhumi usalowe m’msonkhano wa Yehova, ku nthawi zonse;

4 popeza sanakumane nanu ndi mkate ndi madzi m’njira muja munatuluka mu Ejipito; popezanso anakulembererani Balamu mwana wa Beori wa ku Petori wa Mesopotamiya, kuti akutemberereni.

5 Ndipo Yehova Mulungu wanu sanafune kumvera Balamu; koma Yehova Mulungu wanu anakusandulizirani tembererolo likhale mdalitso, popeza Yehova Mulungu wanu anakukondani.

6 Musawafunira mtendere, kapena chowakomera masiku anu onse ku nthawi zonse.

7 Musamanyansidwa naye Mwedomu, popeza ndiye mbale wanu; musamanyansidwa naye Mwejipito, popeza munali alendo m’dziko lake.

8 Ana obadwa nao a mbadwo wachitatu alowe m’msonkhano wa Yehova.

9 Nkhondo yanu ikatuluka pa adani anu, mudzisunge kusachita choipa chilichonse.

10 Pakakhala munthu pakati pa inu, ndiye wosayera chifukwa chochitika usiku, azituluka kunja kwa chigono, asalowe pakati pa chigono;

11 koma kudzali pofika madzulo, asambe m’madzi; ndipo litalowa dzuwa alowe pakati pa chigono.

12 Mukhale nao malo kunja kwa chigono kumene muzimukako kuthengo;

13 nimukhale nacho chokumbira mwa zida zanu; ndipo kudzali, pakukhala inu pansi kuthengo mukumbe nacho, ndi kutembenuka ndi kufotsera chakutulukacho;

14 popeza Yehova Mulungu wanu ayenda pakati pa chigono chanu kukupulumutsani ndi kupereka adani anu pamaso panu; chifukwa chake chigono chanu chikhale chopatulika; kuti angaone kanthu kodetsa mwa inu, ndi kukupotolokerani.

Za akapolo opulumuka, za achigololo, za okongoletsa mopindulitsa

15 Musamapereka kwa mbuye wake kapolo wopulumuka kwa mbuye wake kuthawira kwa inu;

16 akhale nanu, pakati panu, ku malo asankhako iye m’mudzi mwanu mwina momkonda; musamamsautsa.

17 Pasakhale mkazi wachigololo pakati pa ana aakazi a Israele, kapena wachigololo pakati pa ana aamuna a Israele.

18 Musamabwera nayo mphotho ya wachigololo, kapena mtengo wake wa galu kulowa nazo m’nyumba ya Yehova Mulungu wanu, chifukwa cha chowinda chilichonse; pakuti onse awiriwa Yehova Mulungu wanu anyansidwa nao.

19 Musamakongoletsa mbale wanu mopindulitsa; phindu la ndalama, phindu la chakudya, phindu la kanthu kalikonse kokongoletsa.

20 Mukongoletse mlendo mopindulitsa; koma mbale wanu musamamkongoletsa mopindulitsa, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni mwa zonse muzigwira ndi dzanja lanu, m’dziko limene mulowamo kulilandira.

21 Mukawindira Yehova Mulungu wanu chowinda, musamachedwa kuchichita; popeza Yehova Mulungu wanu adzakufunsani za ichi ndithu ndipo mukadachimwako.

22 Koma mukapanda kulonjeza chowinda, mulibe kuchimwa.

23 Chotuluka pa milomo yanu muchisamalire ndi kuchichita; monga munalonjezera Yehova Mulungu wanu, chopereka chaufulu munachilonjeza pakamwa panu.

24 Mukalowa m’munda wampesa wa mnansi wanu, mudyeko mphesa ndi kukhuta nazo monga mufuna eni; koma musaika kanthu m’chotengera chanu.

25 Mukalowa m’tirigu wosasenga wa mnansi wanu, mubudule ngala ndi dzanja lanu, koma musasengako ndi chisenga tirigu wachilili wa mnansi wanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/23-fce006c3bc394350bd23b083770edc37.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *