Categories
YOSWA

YOSWA Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli likukamba za m’mene Aisraele adalowera m’dziko la Kanani nkulilanda, Yoswa akuwatsogolera. Kenaka adagawana dzikolo.

Nkhani zodziwika bwino m’bukuli ndizo kuoloka Yordani, kugwa kwa Yeriko, kugonjetsedwa kwa Ai, ndi kukonzanso kwa chipangano pakati pa Mulungu ndi anthu ake.

Mau odziwika bwino ndi awa: “mudzisankhire lero amene mudzamtumikira…koma ine, ndi a m’nyumba yanga, tidzatumikira Yehova” (24.15).

Za mkatimu

Aisraele atenga dziko la Kanani

1.1—12.24

a. Aoloka mtsinje wa Yordani

1.1—5.15

b. Agonjetsa mzinda la Yeriko

6.1—7.26

c. Agonjetsa mzinda wa Ai ndi mizinda ina

8.1—12.24

Aisraele agawana dziko

13.1—22.34

a. Dziko la kum’mawa kwa Yordani

13.1-33

b. Dziko la kuzambwe kwa Yordani

14.1—19.51

c. Mizinda yopulumukirako

20.1-9

d. Mafuko awiri akum’mawa abwerera ku dziko lao

22.1-34

Mau a Yoswa otsanzikana nawo

23.1-16

Abwereza kuchita chipangano ku Sekemu

24.1-33

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *