Midzi yokhalamo Alevi
1 Pamenepo akulu a nyumba za atate a Alevi anayandikira kwa Eleazara wansembe, ndi kwa Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa akulu a nyumba za atate a mafuko a ana a Israele;
2 nanena nao ku Silo m’dziko la Kanani, ndi kuti Yehova analamulira mwa dzanja la Mose kuti atipatse mizinda yokhalamo ife, ndi mabusa a zoweta zathu.
3 Ndipo ana a Israele anapatsa Alevi, kutapa pa cholowa chao, monga mwa lamulo la Yehova, mizinda iyi ndi mabusa ao.
4 Ndipo maere anatulukira mabanja a Akohati; ndipo molota maere ana a Aroni wansembe, ndiwo Alevi, analandira motapa pa fuko la Yuda, ndi pa fuko la Simeoni, ndi pa fuko la Benjamini, mizinda khumi ndi itatu.
5 Ndipo ana otsala a Kohati analandira molota maere motapa pa mabanja a fuko la Efuremu, ndi pa fuko la Dani, ndi pa hafu la fuko la Manase, mizinda khumi.
6 Ndipo ana a Geresoni analandira molota maere motapa pa mabanja a fuko la Isakara, ndi pa fuko la Asere, ndi pa fuko la Nafutali, ndi pa hafu la fuko la Manase mu Basani, mizinda khumi ndi itatu.
7 Ana a Merari, monga mwa mabanja ao, analandira motapa pa fuko la Rubeni, ndi pa fuko la Gadi, ndi pa fuko la Zebuloni mizinda khumi ndi iwiri.
8 Motero ana a Israele anapatsa Alevi mizinda iyi ndi mabusa ao, molota maere, monga Yehova adalamulira mwa dzanja la Mose.
9 Ndipo anapatsa motapa pa fuko la ana a Yuda, ndi pa fuko la ana a Simeoni, mizinda iyi yotchulidwa maina ao;
10 kuti ikhale ya ana a Aroni a mabanja a Akohati, a ana a Levi, pakuti maere oyamba adatulukira iwowa.
11 Ndipo anawapatsa mudzi wa Araba, ndiye atate wa Anaki, womwewo ndi Hebroni, ku mapiri a Yuda, ndi mabusa ake ozungulirapo.
12 Koma minda ya mizinda ndi midzi yake anapatsa Kalebe mwana wa Yefune, ikhale yake.
13 Ndipo kwa ana a Aroni wansembe anapatsa Hebroni ndi mabusa ake, ndiwo mzinda wopulumukirako wakupha mnzake, ndi Libina ndi mabusa ake;
14 ndi Yatiri ndi mabusa ake, ndi Esitemowa ndi mabusa ake;
15 ndi Holoni ndi mabusa ake, ndi Debiri ndi mabusa ake;
16 ndi Aini ndi mabusa ake, ndi Yuta ndi mabusa ake, ndi Betesemesi ndi mabusa ake; mizinda isanu ndi inai yotapira mafuko awiri aja.
17 Ndipo motapira fuko la Benjamini, Gibiyoni ndi mabusa ake, Geba ndi mabusa ake,
18 Anatoti ndi mabusa ake, ndi Alimoni ndi mabusa ake; mizinda inai.
19 Mizinda yonse ya ana a Aroni, ansembe, ndiyo khumi ndi itatu, ndi mabusa ao.
20 Ndipo mabanja a ana a Kohati, Aleviwo, otsala a ana a Kohati, analandira mizinda ya maere ao motapira pa fuko la Efuremu.
21 Ndipo anawapatsa Sekemu ndi mabusa ake ku mapiri a Efuremu, ndiwo mzinda wopulumukirako wakupha mnzakeyo, ndi Gezere ndi mabusa ake;
22 ndi Kibizaimu ndi mabusa ake, Betehoroni ndi mabusa ake; mizinda inai.
23 Ndipo motapira fuko la Dani, Eliteke ndi mabusa ake, ndi Gibetoni ndi mabusa ake;
24 Ayaloni ndi mabusa ake, Gatirimoni ndi mabusa ake; mizinda inai.
25 Ndipo motapira pa hafu la fuko la Manase, Taanaki ndi mabusa ake, ndi Gatirimoni ndi mabusa ake; mizinda iwiri.
26 Mizinda yonse ya mabanja a ana otsala a Kohati ndiyo khumi ndi mabusa ao.
27 Ndipo anapatsa ana a Geresoni, a mabanja a Alevi, motapira pa hafu la fuko la Manase, Golani mu Basani ndi mabusa ake, ndiwo mzinda wopulumukirako wakupha mnzakeyo; ndi Beesetera ndi mabusa ake; mizinda iwiri.
28 Ndipo motapira pa fuko la Isakara, Kisiyoni ndi mabusa ake, Daberati ndi mabusa ake;
29 Yaramuti ndi mabusa ake, Enganimu ndi mabusa ake; mizinda inai.
30 Ndipo motapira pa fuko la Asere, Misala ndi mabusa ake, Abidoni ndi mabusa ake;
31 Helekati ndi mabusa ake, ndi Rehobu ndi mabusa ake; mizinda inai.
32 Ndipo motapira pa fuko la Nafutali, Kedesi mu Galileya ndi mabusa ake, ndiwo mzinda wopulumukirako wakupha mnzakeyo, ndi Hamotidori ndi mabusa ake, ndi Karitani ndi mabusa ake, mizinda itatu.
33 Mizinda yonse ya Ageresoni monga mwa mabanja ao ndiyo mizinda khumi ndi itatu ndi mabusa ao.
34 Ndipo anapatsa kwa mabanja a ana a Merari, otsala a Alevi, motapira pa fuko la Zebuloni, Yokoneamu ndi mabusa ake, ndi Karita ndi mabusa ake,
35 Dimina ndi mabusa ake, Nahalala ndi mabusa ake; mizinda inai.
36 Ndipo motapira pa fuko la Rubeni, Bezeri ndi mabusa ake, ndi Yahazi ndi mabusa ake,
37 Kedemoti ndi mabusa ake, ndi Mefaati ndi mabusa ake; mizinda inai.
38 Ndipo motapira m’fuko la Gadi, Ramoti mu Giliyadi ndi mabusa ake, ndiwo mzinda wopulumukirako wakupha mnzakeyo, ndi Mahanaimu ndi mabusa ake;
39 Hesiboni ndi mabusa ake, Yazere ndi mabusa ake: yonse pamodzi mizinda inai.
40 Yonseyi ndiyo mizinda ya ana a Merari monga mwa mabanja ao, ndiwo otsala a mabanja a Alevi; ndipo gawo lao ndilo mizinda khumi ndi iwiri.
41 Mizinda yonse ya Alevi, pakati pa cholowa cha ana a Israele ndiyo mizinda makumi anai kudza isanu ndi itatu, ndi mabusa ao.
42 Mizinda iyi yonse inali nao mabusa ao pozungulira pao: inatero mizinda iyi yonse.
43 Motero Yehova anawapatsa Israele dziko lonse adalumbiralo kuwapatsa makolo ao: ndipo analilandira laolao, nakhala m’mwemo.
44 Ndipo Yehova anawapatsa mpumulo pozungulira ponse, monga mwa zonse adalumbirira makolo ao; ndipo pamaso pao sipanaime munthu mmodzi wa adani ao onse; Yehova anapereka adani ao onse m’manja mwao.
45 Sikadasowa kanthu konse ka zinthu zokoma zonse Yehova adazinenera nyumba ya Israele; zidachitika zonse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/21-376c630b82c10ed5e9159832ac7d26a2.mp3?version_id=1068—