Categories
2 SAMUELE

2 SAMUELE 22

Nyimbo yoyamikira Yehova ya Davide

1 Ndipo Davide analankhula kwa Yehova mau a nyimbo iyi tsikuli Yehova anampulumutsa m’dzanja la adani ake onse, ndi m’dzanja la Saulo.

2 Ndipo anati,

Yehova ndiye thanthwe langa,

ndi ngaka yanga, ndi Mpulumutsi wanga, wangadi.

3 Mulungu wa thanthwe langa,

Iye ndidzamkhulupirira;

chikopa changa, ndi nyanga ya chipulumutso changa,

nsanja yanga yaitali, ndi populumukirapo panga;

Mpulumutsi wanga, mundipulumutsa kuchiwawa.

4 Ndidzaitana kwa Yehova amene ayenera timtamande;

chomwecho ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.

5 Pakuti mafunde a imfa anandizinga,

mitsinje ya zopanda pake inandiopsa ine.

6 Zingwe za kumanda zinandizingira;

misampha ya imfa inandifikira ine.

7 M’kusauka kwanga ndinaitana kwa Yehova,

inde ndinakuwira kwa Mulungu wanga;

ndipo Iye anamva mau anga ali mu Kachisi wake,

ndi kulira kwanga kunafika ku makutu ake.

8 Pomwepo dziko linagwedezeka ndi kunthunthumira.

Maziko a dziko la kumwamba anasunthika.

Nagwedezeka, chifukwa Iye anakwiya.

9 M’mphuno mwake munatuluka utsi,

ndi moto wotuluka m’kamwa mwake unaononga;

makala anayaka nao.

10 Anaweramitsa miyambanso, natsika;

ndipo mdima wandiweyani unali pansi pa mapazi ake.

11 Ndipo Iye anaberekeka pakerubinauluka;

inde anaoneka pa mapiko a mphepo.

12 Ndipo anayesa mdimawo ngati mahema omzungulira Iye,

kusonkhana kwa madzi ndi mitambo yochindikira ya mlengalenga.

13 Cheza cha pamaso pake

makala a moto anayaka.

14 Yehova anagunda kumwamba;

ndipo Wam’mwambamwamba ananena mau ake.

15 Ndipo Iye anatumiza mivi, nawawaza;

mphezi, nawaopsa.

16 Pamenepo m’munsi mwa nyanja munaoneka,

maziko a dziko anaonekera poyera,

ndi mtonzo wa Yehova,

ndi mpumo wa mpweya wa m’mphuno mwake.

17 Iye anatumiza kuchokera kumwamba nanditenga;

Iye ananditulutsa m’madzi aakulu.

18 Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

kwa iwo akudana ndi ine;

pakuti anandiposa mphamvu.

19 Anandifikira ine tsiku la tsoka langa;

koma Yehova anali mchirikizo wanga.

20 Iye ananditulutsanso ku malo aakulu;

Iye anandipulumutsa,

chifukwa akondwera ndi ine.

21 Yehova anandibwezera monga mwa cholungama changa;

monga mwa kuyera kwa manja anga anandipatsa mphotho.

22 Pakuti ndinasunga njira za Yehova,

osapatukira ku zoipa kusiya Mulungu wanga.

23 Pakuti maweruzo ake onse anali pamaso panga;

ndipo za malemba ake, sindinawapatukire.

24 Ndinakhalanso wangwiro kwa Iye,

ndipo ndinadzisunga kusachita kuipa kwanga.

25 Chifukwa chake Yehova anandibwezera monga mwa cholungama changa;

monga mwa kuyera kwanga pamaso pake.

26 Ndi chifundo Inu mudzadzionetsa wachifundo,

ndi munthu wangwiro mudzadzionetsa wangwiro.

27 Ndi oyera mtima mudzadzionetsa woyera mtima;

ndi otsutsatsutsa mudzadzionetsa wopotoza.

28 Ndipo mudzapulumutsa anthu osautsidwa;

koma maso anu ali pa odzikuza kuti muwachepetse.

29 Pakuti Inu ndinu nyali yanga, Yehova;

ndipo Yehova adzaunika mumdima mwanga.

30 Pakuti ndi Inu ndithamangira gulu;

ndi Mulungu wanga ndilumphira linga.

31 Kunena za Mulungu, njira yake ili yangwiro;

mau a Yehova anayesedwa;

Iye ndiye chikopa kwa onse akukhulupirira Iye.

32 Pakuti Mulungu ndani, koma Yehova?

Ndipo thanthwe ndani, koma Mulungu wathu?

33 Mulungu ndiye linga langa lamphamvu;

ndipo Iye ayendetsa angwiro mu njira yake.

34 Iye asandutsa mapazi ake akunga mapazi a mbawala;

nandiika pa misanje yanga.

35 Iye aphunzitsa manja anga nkhondo;

kotero kuti manja anga alifula uta wamkuwa.

36 Ndiponso munandipatsa chikopa cha chipulumutso chanu;

ndi kufatsa kwanu kunandikulitsa.

37 Munakulitsa kulunza kwanga pansi panga,

ndi mapazi anga sanaterereke.

38 Ndinapirikitsa adani anga, ndi kuwaononga;

ndiponso sindinabwerere mpaka nditawatha.

39 Ndinawatha ndi kuwapyoza, kuti sangathe kuuka,

inde anagwa pansi pa mapazi anga.

40 Pakuti Inu munandimanga m’chuuno ndi mphamvu ya kunkhondo;

munandigonjetsera akundiukira.

41 Munatembenuzitsanso adani anga andipatse mbuyo,

kuti ndiwalikhe akudana ndi ine.

42 Anayang’ana iwo, koma panalibe wopulumutsa;

ngakhale kwa Yehova, koma Iye sanawayankhe.

43 Pomwepo ndinawasansantha asalale ngati fumbi la padziko,

ndinawapondereza ngati dothi la m’makwalala.

44 Inunso munandipulumutsa ine pa kulimbana kwa anthu anga;

munandisunga ndikhale mutu waamitundu;

Anthu amene sindinawadziwe adzanditumikira ine.

45 Alendo adzandigonjera ine,

pakumva za ine, adzandimvera pomwepo.

46 Alendo adzafota,

nadzabwera ndi kunthunthumira otuluka mokwiririka mwao.

47 Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;

ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la chipulumutso changa;

48 inde Mulungu wakundibwezera chilango ine,

ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.

49 Amene anditulutsa kwa adani anga;

inde mundikweza ine pamwamba pa iwo akundiukira;

mundipulumutsa kwa munthu wachiwawa.

50 Chifukwa chake ndidzakuongani Yehova, pakati pa amitundu,

ndipo ndidzaimba zolemekeza dzina lanu.

51 Iye apatsa mfumu yake chipulumutso chachikulu;

naonetsera chifundo wodzozedwa wake,

kwa Davide ndi mbeu yake ku nthawi zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2SA/22-06f0c38dcd56c1f96249c9363cdb4311.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *