Categories
2 MAFUMU

2 MAFUMU 8

Wa ku Sunemu abwera kwao itatha njalayo

1 Ndipo Elisa ananena ndi mkazi uja adamuukitsira mwana wake, kuti, Nyamuka, numuke iwe ndi banja lako, nugonere komwe ukaone malo; pakuti Yehova waitana njala, nidzagwera dziko zaka zisanu ndi ziwiri.

2 Nanyamuka mkaziyo, nachita monga mwa mau a munthu wa Mulunguyo, namuka ndi banja lake, nagonera m’dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.

3 Ndipo pakutha pake pa zaka zisanu ndi ziwirizo, mkaziyo anabwera kuchoka m’dziko la Afilisti, natuluka kukanena za nyumba yake ndi munda wake kwa mfumu.

4 Koma mfumu inalikulankhula ndi Gehazi mnyamata wa munthu wa Mulungu, ndi kuti, Ndifotokozere zazikulu zonse Elisa wazichita.

5 Ndipo kunali, alimkufotokozera mfumu m’mene adamuukitsira wakufayo, taonani, mkaziyo adamuukitsira mwana wake ananena za nyumba yake ndi munda wake kwa mfumu. Nati Gehazi, Mbuye wanga mfumu, suyu mkaziyo, suyu mwana wake Elisa anamuukitsayo?

6 Ndipo pofunsa mfumu, mkaziyo anaisimbira. Pamenepo mfumu anamuikira mdindo, ndi kuti, Bwezetsa zake zonse ndi zipatso zonse za m’munda, chichokere iye m’dziko mpaka lero lino.

Hazaele mfumu ya Aramu

7 Ndipo Elisa anafika ku Damasiko, podwala Benihadadi mfumu ya Aramu; ndipo anamuuza, kuti, Munthu wa Mulungu wadza kuno.

8 Niti mfumu kwa Hazaele, Tenga chaufulu m’dzanja lako, nukakumane naye munthu wa Mulungu, nukafunsire Yehova mwa iye, ndi kuti, Ndidzachira kodi nthenda iyi?

9 Namuka Hazaele kukakomana naye, napita nacho chaufulu, ndicho cha zokoma zonse za mu Damasiko, zosenzangamiramakumi anai, nafika naima pamaso pake, nati, Mwana wanu Benihadadi mfumu ya Aramu, wandituma ine kwa inu, ndi kuti, Kodi ndidzachira nthenda iyi?

10 Nanena naye Elisa, Kamuuze, kuti, Sudzachira konse; popeza Yehova wandionetsa kuti adzafa ndithu.

11 Ndipo anamyang’ana chidwi, mpaka anachita manyazi, nalira misozi munthu wa Mulungu.

12 Nati Hazaele, Muliriranji, mbuye wanga? Nayankha iye, Popeza ndidziwa choipa udzachitira ana a Israele; udzatentha malinga ao ndi moto, nudzapha anyamata ao ndi lupanga, nudzaphwanya makanda ao, nudzang’amba akazi ao okhala ndi pakati.

13 Nati Hazaele, Koma nanga kapolo wanu ali chiyani, ndiye galu, kuti akachite chinthu chachikulu ichi? Nayankha Elisa, Yehova wandionetsa kuti udzakhala mfumu ya pa Aramu.

14 Ndipo anachoka kwa Elisa, nadza kwa mbuye wake; ameneyo ananena naye, Anakuuza chiyani Elisa? Nati iye, Anandiuza kuti mudzachira ndithu.

15 Ndipo kunali m’mawa mwake, anatenga chimbwi, nachiviika m’madzi, nachiphimba pankhope pa mfumu, nifa; ndipo Hazaele analowa ufumu m’malo mwake.

Yehoramu mfumu ya Yuda

16 Ndipo chaka chachisanu cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israele, pokhala Yehosafati mfumu ya Yuda, Yehoramu mwana wa Yehosafati analowa ufumu.

17 Ndiye wa zaka makumi atatu ndi chiwiri polowa ufumu wake, nachita ufumu zaka zisanu ndi zitatu kuYerusalemu.

18 Nayenda m’njira ya mafumu a Israele, m’mene inachitira nyumba ya Ahabu; pakuti mkazi wake ndiye mwana wa Ahabu, nachita iye choipa pamaso pa Yehova.

19 Koma Yehova sanafune kuononga Yuda, chifukwa cha Davide mtumiki wake monga adamuuza, kuti adzampatsa nyali ya kwa ana ake kosalekeza.

20 Masiku ake Aedomu anapanduka ku ulamuliro wa Yuda, nadziikira mfumu okha.

21 Pamenepo Yoramu anaoloka kunka ku Zairi, ndi magaleta ake onse pamodzi naye; nauka iye usiku, nakantha Aedomu akumzinga ndi nduna za magaleta, nathawira anthu kwa mahema ao.

22 Motero Aedomu anapanduka ku ulamuliro wa Yuda mpaka lero lino. Ndipo Alibina anapanduka nthawi yomweyi.

23 Ndi machitidwe ena a Yoramu, ndi zonse anazichita, sizinalembedwe kodi m’buku la machitidwe a mafumu a Yuda.

24 Nagona Yoramu ndi makolo ake, naikidwa pamodzi ndi makolo ake m’mzinda wa Davide; ndipo Ahaziya mwana wake anakhala mfumu m’malo mwake.

Ahaziya mfumu ya Yuda

25 Chaka chakhumi ndi ziwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda analowa ufumu wake.

26 Ahaziya ndiye wa zaka makumi awiri mphambu ziwiri polowa ufumu wake, nakhala mfumu mu Yerusalemu chaka chimodzi. Ndi dzina la make ndiye Ataliya mdzukulu wa Omuri mfumu ya Israele.

27 Ndipo anayenda m’njira ya nyumba ya Ahabu, nachita choipa pamaso pa Yehova, m’mene inachitira nyumba ya Ahabu; pakuti ndiye wa chibale cha banja la Ahabu.

28 Ndipo anamuka Yoramu mwana wa Ahabu kukathira nkhondo pa Hazaele mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi; ndi Aaramu analasa Yoramu.

29 Ndipo mfumu Yoramu anabwera kuti ampoletse mu Yezireele mabalawo adamkantha Aaramu ku Rama, polimbana naye Hazaele mfumu ya Aramu. Natsikirako Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda kukamuona Yoramu mwana wa Ahabu mu Yezireele, pakuti anadwala.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2KI/8-6d5a9374d21f5302a629b0cc8d1b9f73.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *