1 Ndipo ndinamva mau aakulu ochokera ku Kachisi, akunena kwaangeloasanu ndi awiri, Mukani, ndipo tsanulirani kudziko mbale zisanu ndi ziwiri za mkwiyo wa Mulungu.
2 Ndipo anachoka woyamba, natsanulira mbale yake kudziko; ndipo kunakhala chilonda choipa ndi chosautsa pa anthu akukhala nalo lemba la chilombo nalambira fano lake.
3 Ndipo wachiwiri anatsanulira mbale yake m’nyanja; ndipo kunakhala mwazi ngati wa munthu wakufa; ndipo zamoyo zonse za m’nyanja zidafa.
4 Ndipo wachitatu anatsanulira mbale yake kumitsinje ndi akasupe a madzi; ndipo kunasanduka mwazi.
5 Ndipo ndinamva mngelo wa madziwo nanena, Muli wolungama, amene muli, nimunali, Woyera Inu, chifukwa mudaweruza kotero;
6 popeza anatsanulira mwazi wa oyera mtima, ndi wa aneneri, ndipo mudawapatsa mwazi amwe; ayenera iwo.
7 Ndipo ndinamva wa paguwa la nsembe, alinkunena, Inde, Ambuye Mulungu, Wamphamvuyonse, maweruziro anu ali oona ndi olungama.
8 Ndipo wachinai anatsanulira mbale yake padzuwa; ndipo analipatsa ilo litenthe anthu ndi moto.
9 Ndipo anatenthedwa anthu ndi kutentha kwakukulu; ndipo anachitira mwano dzina la Mulungu wokhala nao ulamuliro pa miliri iyi; ndipo sanalape kuti amchitire ulemu.
10 Ndipo wachisanu anatsanulira mbale yake pa mpando wachifumu wa chilombo; ndipo ufumu wake unadetsedwa; ndipo anatafuna malilime ao ndi kuwawa kwake,
11 nachitira mwano Mulungu wa mu Mwamba chifukwa cha zowawa zao ndi zilonda zao; ndipo sanalape ntchito zao.
12 Ndipo wachisanu ndi chimodzi anatsanulira mbale yake pamtsinje waukulu Yufurate; ndi madzi ake anaphwa, kuti ikonzeke njira ya mafumu ochokera potuluka dzuwa.
13 Ndipo ndinaona motuluka m’kamwa mwa chinjoka, ndi m’kamwa mwa chilombo, ndi m’kamwa mwa mneneri wonyenga mizimu itatu yonyansa, ngati achule;
14 pakuti ali mizimu ya ziwanda zakuchita zizindikiro; zimene zituluka kunka kwa mafumu a dziko lonse, kuwasonkhanitsira kunkhondo ya tsiku lalikulu la Mulungu, Wamphamvuyonse.
15 (Taonani, ndidza ngati mbala. Wodala iye amene adikira, nasunga zovala zake, kuti angayende wausiwa, nangapenye anthu usiwa wake.)
16 Ndipo anawasonkhanitsira kumalo otchedwa mu Chihebri Armagedoni.
17 Ndipo wachisanu ndi chiwiri anatsanulira mbale yake mumlengalenga; ndipo mu Kachisimo mudatuluka mau aakulu, ochokera kumpando wachifumu ndi kunena, Chachitika;
18 ndipo panakhala mphezi, ndi mau, ndi mabingu; ndipo panali chivomezi chachikulu chotero sichinaoneke chiyambire anthu padziko, chivomezi cholimba chotero, chachikulu chotero.
19 Ndipo chimzinda chachikulucho chidagawika patatu, ndi mizinda yaamitunduinagwa; ndipo Babiloni waukulu unakumbukika pamaso pa Mulungu, kuti aupatse chikho cha vinyo waukali wa mkwiyo wake.
20 Ndipo zisumbu zonse zidathawa, ndi mapiri sanapezeke.
21 Ndipo anatsika kumwamba matalala aakulu, lonse lolemera ngati talente, nagwa pa anthu; ndipo anthu anachitira Mulungu mwano chifukwa cha mliri wa matalala, pakuti mliri wake ndi waukulu ndithu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/REV/16-4a7c5fa8f0384b99d887d442e00a631e.mp3?version_id=1068—