Chigawo cha oimbira nyimbo
1 Ndipo Davide ndi akazembe a gulu la nkhondo anapatulira utumikiwo ena a ana a Asafu, ndi a Hemani, ndi a Yedutuni, anenere ndi azeze, ndi zisakasa, ndi nsanje; ndi chiwerengo cha antchito monga mwa kutumikira kwao ndicho:
2 a ana a Asafu: Zakuri, ndi Yosefe, ndi Netaniya, ndi Asarela, ana a Asafu; mwa chilangizo cha Asafu, wakunenera mwa chilangizo cha mfumu.
3 A Yedutuni, ana a Yedutuni: Gedaliya, ndi Zeri, ndi Yesaya, Hasabiya, ndi Matitiya, asanu ndi mmodzi; mwa chilangizo cha atate wao Yedutuni, ndiye wakunenera ndi kuyamika ndi kulemekeza Yehova ndi zeze.
4 A Hemani, ana a Hemani: Bukiya, Mataniya, Uziyele, Sebuele, ndi Yerimoti, Hananiya, Hanani, Eliyata, Gidaliti, ndi Romamiti-Ezere, Yosibekasa, Maloti, Hotiri, Mahaziyoti;
5 awa onse ndiwo ana a Hemani mlauli wa mfumu m’mau a Mulungu, kuti akweze mphamvu yake. Ndipo Mulungu anapatsa Hemani ana aamuna khumi ndi anai, ndi ana aakazi atatu.
6 Onsewa anawalangiza ndi atate wao aimbe m’nyumba ya Yehova ndi nsanje, zisakasa ndi azeze; atumikire nazo m’nyumba ya Mulungu; ndipo Asafu, Yedutuni, ndi Hemani, anawalangiza ndi mfumu.
7 Ndipo chiwerengo chao, pamodzi ndi abale ao ophunzitsidwa aimbire Yehova, onse anthetemya, ndiwo mazana awiri mphambu makumi asanu ndi atatu.
8 Ndipo anachita maere pa udikiro wao, analingana onse, ang’ono ndi akulu, mphunzitsi ndi wophunzira.
9 Maere oyamba tsono anagwera a banja la Asafu ndiye Yosefe; wachiwiri Gedaliya, iye ndi abale ake, ndi ana ake khumi ndi awiri;
10 wachitatu Zakuri, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
11 wachinai Iziri, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
12 wachisanu Netaniya, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
13 wachisanu ndi chimodzi Bukiya, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
14 wachisanu ndi chiwiri Yesarela, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
15 wachisanu ndi chitatu Yesaya, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
16 wachisanu ndi chinai Mataniya, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
17 wakhumi Simei, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
18 wakhumi ndi chimodzi Azarele, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
19 wakhumi ndi chiwiri Hasabiya, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
20 wakhumi ndi chitatu Subaele, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
21 wakhumi ndi chinai Matitiya, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
22 wakhumi ndi chisanu Yeremoti, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
23 wakhumi ndi chisanu ndi chimodzi Hananiya, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
24 wakhumi ndi chisanu ndi chiwiri Yosibekasa, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
25 wakhumi ndi chisanu ndi chitatu Hanani, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
26 wakhumi ndi chisanu ndi chinai Maloti, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
27 wamakumi awiri Eliyata, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
28 wa makumi awiri ndi chimodzi Hotiri, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
29 wa makumi awiri ndi chiwiri Gidaliti, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
30 wa makumi awiri ndi chitatu Mahaziyoti, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri;
31 wa makumi awiri ndi chinai Romamiti-Ezere, ana ake ndi abale ake khumi ndi awiri.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/25-10cfaaf8799697c1e2b944529adc67bf.mp3?version_id=1068—