Mamangidwe a Kachisi
1 Pamenepo Solomoni anayamba kumanga nyumba ya Yehova kuYerusalemu, m’phiri la Moriya, kumene Mulungu anaonekera kwa Davide atate wake pamalo pamene Davide anakonzeratu pa dwale la Orinani Myebusi.
2 Nayamba kumanga tsiku lachiwiri la mwezi wachiwiri, chaka chachinai cha ufumu wake.
3 Ndipo maziko adawaika Solomoni akumangapo nyumba ya Mulungu ndi awa: utali wake, kuyesa mikono monga mwa muyeso wakale, ndiwo mikono makumi asanu ndi limodzi, ndi kupingasa kwake mikono makumi awiri.
4 Ndi chipinda cholowera chinali kukhomo kwa nyumba, m’litali mwake monga mwa kupingasa kwa nyumba munali mikono makumi awiri, ndi msinkhu wake zana limodzi mphambu makumi awiri; ndipo analikuta m’katimo ndi golide woona.
5 M’nyumba yaikulu tsono anatchinga ndi mitengo yamlombwa, imene anaikuta ndi golide wabwino, nalembapo ngati migwalangwa ndi maunyolo.
6 Ndipo anakuta nyumba ndi miyala ya mtengo wake; ndi golide wake ndiye golide wa Paravaimu.
7 Anamamatizanso Kachisi, mitanda, ziundo, ndi makoma ake, ndi zitseko zake, ndi golide; nalembaakerubipamakoma.
8 Ndipo anamanga malo opatulika kwambiri, m’litali mwake monga mwa kupingasa kwa nyumba mikono makumi awiri, ndi kupingasa kwake mikono makumi awiri; naikuta ndi golide wabwino wakufikira matalente mazana asanu ndi limodzi.
9 Ndi kulemera kwake kwa misomali ndiko masekeli makumi asanu a golide. Ndipo anazikuta ndi golide zipinda zosanjikizana.
10 Ndipo m’malo opatulika kwambiri anapanga akerubi awiri, anachita osema, nawakuta ndi golide.
11 Ndi mapiko a akerubi m’litali mwake ndimo mikono makumi awiri; phiko la kerubi mmodzi mikono isanu, lojima khoma la nyumba; ndi phiko linzake mikono isanu, lokhudzana nalo phiko la kerubi wina.
12 Ndi phiko la kerubi wina mikono isanu lojima khoma la nyumba, ndi phiko linzake mikono isanu lolumikizana ndi phiko la kerubi wina.
13 Mapiko a akerubi awa anafunyululika mikono makumi awiri; ndipo anaima ndi mapazi ao, ndi nkhope zao zinaloza kukhomo.
14 Ndipo anaomba nsalu yotchinga ya thonje lamadzi, ndi lofiira, ndi lofiirira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, naomberamo akerubi.
15 Ndipo anapanga ku khomo la nyumba nsanamira ziwiri za mikono makumi atatu mphambu ziwiri; ndi mutu unakhala pamwamba pa iliyonse ndiwo mikono isanu.
16 Napanga maunyolo a m’chipinda chamkati, nawamanga pa mitu ya nsanamirazi, napanga makangaza zana limodzi, nawamanga pamaunyolo.
17 Ndipo anaimiritsa nsanamirazo pakhomo pa Kachisi; imodzi ku dzanja lamanja, ndi inzake ku dzanja lamanzere; nalitcha dzina la iyi ya ku dzanja lamanja Yakini, ndi dzina la iyi ya ku dzanja lamanzere Bowazi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CH/3-0d1ae3980a50b2e8282ecb090333d1c7.mp3?version_id=1068—