Categories
2 MBIRI

2 MBIRI 5

Aika likasa mu Kachisi

1 Momwemo zidatha ntchito zonse Solomoni adazichitira nyumba ya Yehova. Ndipo Solomoni anabwera nazo zopatulika zija za atate wake Davide; naziikasiliva, ndi golide, ndi zipangizo zonse m’chuma cha nyumba ya Mulungu.

Kuperekedwa kwa Kachisi

2 Pamenepo Solomoni anasonkhanitsira akuluakulu a Israele, ndi akulu onse a mafuko, ndi akalonga a nyumba za makolo a ana a Israele, kuYerusalemu, kukatengalikasa la chipanganocha Yehova kumzinda wa Davide ndiwoZiyoni.

3 Ndipo amuna onse a Israele anasonkhana kwa mfumu kumadyerero anachitikawo, m’mwezi wachisanu ndi chiwiri.

4 Nadza akuluakulu onse a Israele, nanyamula likasalo Alevi.

5 Ndipo anakwera nalo likasa, ndichihema chokomanako, ndi zipangizo zonse zopatulika zinali m’chihemamo; izizo ansembe Alevi anakwera nazo.

6 Ndi mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Israele losonkhana kwa iye anali kulikasa, naphera nsembe, nkhosa ndi ng’ombe zosawerengeka kuchuluka kwake.

7 Ndipo ansembe analowa nalo likasa la chipangano la Yehova kumalo kwake m’chipinda chamkati mwa Kachisi, m’malo opatulika kwambiri, pansi pa mapiko aakerubi.

8 Pakuti akerubi anafunyulula mapiko ao pamalo a likasa, ndi akerubi anaphimba likasa ndi mphiko zake pamwamba pake.

9 Ndipo zinatalikitsa mphikozo, kuti nsonga za mphiko zidaoneka kulikasa chakuno cha chipinda chamkati, koma sizinaoneke kubwalo; ndipo zili komweko mpaka lero lino.

10 Munalibe kanthu kena m’likasa, koma magome awiri Mose anawaika m’mwemo ku Horebu, muja Yehova anachita chipangano ndi ana a Israele potuluka iwo mu Ejipito.

11 Ndipo ansembe anatuluka m’malo opatulika, pakuti ansembe onse anali komwe adadzipatula, osasunga magawidwe ao;

12 Alevi omwe akuimba, onsewo ndiwo Asafu, Hemani, Yedutuni, ndi ana ao, ndi abale ao ovala bafuta, ali nazo nsanje, ndi zisakasa, ndi azeze, anaima kum’mawa kwa guwa la nsembe, ndi pamodzi nao ansembe zana limodzi mphambu makumi awiri akuomba malipenga.

13 Ndipo kunali, pakuchita limodzi amalipenga ndi oimba, kumveketsa mau amodzi akulemekeza ndi kuyamika Yehova, ndi pakukweza mau ao pamodzi ndi malipenga, ndi nsanje, ndi zoimbira zina, ndi kulemekeza Yehova, ndi kuti, Pakuti Iye ndiye wabwino, pakuti chifundo chake chikhala chikhalire; pamenepo mtambo unadzaza nyumbayi, ndiyo nyumba ya Yehova;

14 ndipo ansembe sanakhoze kuimirira kutumikira chifukwa cha mtambowo; pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza nyumba ya Mulungu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CH/5-38eb7d8c257d9e000ebb9a24d68f7d32.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *