Categories
2 MBIRI

2 MBIRI 11

Mulungu aletsa nkhondo pakati pa Yuda ndi Israele

1 Ndipo atafika ku Yerusalemu Rehobowamu, anamemeza a nyumba ya Yuda ndi Benjamini amuna osankhika zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu, ndiwo ankhondo, alimbane ndi Aisraele kubwezanso ufumu kwa Rehobowamu.

2 Koma mau a Yehova anadza kwa Semaya munthu wa Mulunguyo, ndi kuti,

3 Lankhula ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Benjamini, ndi kuti,

4 Atero Yehova, Musamuka kukayambana ndi abale anu, bwererani yense kunyumba yake; pakuti chinthu ichi chifuma kwa Ine. Ndipo anamvera mau a Yehova, nabwerera osakayambana ndi Yerobowamu.

5 Ndipo Rehobowamu anakhala mu Yerusalemu, namanga mizinda yolimbikiramo mu Yuda.

6 Anamangadi Betelehemu, ndi Etamu, ndi Tekowa,

7 ndi Betezuri, ndi Soko, ndi Adulamu,

8 ndi Gati, ndi Maresa, ndi Zifi,

9 ndi Adoraimu, ndi Lakisi, ndi Azeka,

10 ndi Zora, ndi Ayaloni, ndi Hebroni; ndiyo mizinda yamalinga ya mu Yuda ndi Benjamini.

11 Ndipo analimbitsa malingawo, naikamo atsogoleri, ndi chakudya chosungikiratu, ndi mafuta, ndi vinyo.

12 Ndi m’mizinda iliyonse anaikamo zikopa ndi mikondo, nailimbitsa chilimbitsire. Ndipo Yuda ndi Benjamini anakhala ake.

Alevi ndi Aisraele ambiri afika ku Yerusalemu

13 Ndipo ansembe ndi Alevi okhala mu Israele yense anadziphatikiza kwa iye, ochokera m’malire ao onse.

14 Pakuti Alevi anasiya podyetsa pao, ndi maiko aoao, nadza ku Yuda ndi ku Yerusalemu; popeza Yerobowamu ndi ana ake anawataya, kuti asachitire Yehova ntchito ya nsembe;

15 nadziikira ansembe a misanje, ndi a ziwanda, ndi a anaang’ombe adawapanga.

16 Ndipo akuwatsata iwo anadza ku Yerusalemu, ochokera m’mafuko onse a Israele, iwo akupereka mitima yao kufuna Yehova Mulungu wa Israele, kudzaphera Yehova Mulungu wa makolo ao nsembe.

17 Momwemo analimbikitsa ufumu wa Yuda, nalimbikitsa Rehobowamu, mwana wa Solomoni zaka zitatu; pakuti anayenda m’njira ya Davide ndi Solomoni zaka zitatu.

18 Ndipo Rehobowamu anadzitengera mkazi Mahalati, mwana wamkazi wa Yerimoti mwana wa Davide, ndi wa Abihaili mwana wamkazi wa Eliyabu mwana wa Yese;

19 ndipo anambalira ana, Yeusi, ndi Semariya, ndi Zahamu.

20 Ndi pambuyo pake anatenga Maaka mwana wamkazi wa Abisalomu; ndipo anambalira Abiya, ndi Atai, ndi Ziza, ndi Selomiti.

21 Ndipo Rehobowamu anakonda Maaka mwana wamkazi wa Abisalomu koposa akazi ake onse, ndi akazi ake aang’ono (pakuti adatenga akazi khumi mphambu asanu ndi atatu, ndi akazi aang’ono makumi asanu ndi limodzi, nabala ana aamuna makumi awiri mphambu asanu ndi atatu, ndi ana aakazi makumi asanu ndi limodzi).

22 Ndipo Rehobowamu anaika Abiya mwana wa Maaka akhale wamkulu, kalonga mwa abale ake; ndiko kuti adzamlonga ufumu.

23 Ndipo anachita mwanzeru, nabalalitsa ana ake aamuna onse m’maiko onse a Yuda ndi Benjamini, kumizinda yonse yamalinga; nawapatsa chakudya chochuluka, nawafunira akazi ochuluka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CH/11-0d2091f6ae9a6736539be83cc44f2d27.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *