Categories
EZARA

EZARA 8

Maina a opita ndi Ezara. Ulendo wao mpaka Yerusalemu

1 Ndipo akulu a nyumba za makolo ndi awa, ndi chibadwidwe cha iwo okwera nane limodzi kuchokera ku Babiloni, pokhala mfumu Arita-kisereksesi, ndi ichi:

2 wa ana a Finehasi, Geresomo; wa ana a Itamara, Daniele; wa ana a Davide, Hatusi.

3 Wa ana a Sekaniya, wa ana a Parosi, Zekariya; ndi pamodzi naye, powawerenga monga mwa chibadwidwe chao, amuna zana limodzi mphambu makumi asanu.

4 Wa ana a Pahatimowabu, Eliehoenai mwana wa Zerahiya; ndi pamodzi naye amuna mazana awiri.

5 Wa ana a Sekaniya, mwana wa Yahaziele; ndi pamodzi naye amuna mazana atatu.

6 Ndi wa ana a Adini, Ebedi mwana wa Yonatani; ndi pamodzi naye amuna makumi asanu.

7 Ndi wa ana a Elamu, Yesaya mwana wa Ataliya; ndi pamodzi naye amuna makumi asanu ndi awiri.

8 Ndi wa ana a Sefatiya, Zebadiya mwana wa Mikaele; ndi pamodzi naye amuna makumi asanu ndi atatu.

9 Wa ana a Yowabu, Obadiya mwana wa Yehiyele; ndi pamodzi naye amuna mazana awiri mphambu khumi kudza asanu ndi atatu.

10 Ndi wa ana a Selomiti, mwana wa Yosofiya; ndi pamodzi naye amuna zana limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi.

11 Ndi wa ana a Bebai, Zekariya mwana wa Bebai; ndi pamodzi naye amuna makumi awiri mphambu asanu ndi atatu.

12 Ndi wa ana a Azigadi, Yohanani mwana wa Hakatani; ndi pamodzi naye amuna zana limodzi mphambu khumi limodzi.

13 Ndi a ana otsiriza a Adonikamu, maina ao ndiwo Elifeleti, Yeiyele, ndi Semaya; ndi pamodzi nao amuna makumi asanu ndi limodzi.

14 Ndi wa ana a Bigivai, Utai ndi Zakuri, ndi pamodzi nao amuna makumi asanu ndi awiri.

15 Ndipo ndinawasonkhanitsa ku mtsinje wopita ku Ahava, ndi komweko tinakhala m’misasa masiku atatu; ndipo ndinapenyerera anthu ndi ansembe, koma sindinapezapo wa ana a Levi.

16 Pamenepo ndinatumiza munthu kuitana Eliyezere, Ariyele, Semaya, ndi Elinatani, ndi Yaribu, ndi Elinatani, ndi Natani, ndi Zekariya, ndi Mesulamu, ndiwo akulu; ndi Yoyaribu ndi Elinatani, ndiwo aphunzitsi.

17 Ndipo ndinawatumiza kwa Ido mkulu, kumalo dzina lake Kasifiya; ndinalonganso m’kamwa mwao mau akunena kwa Ido, ndi kwa abale ake antchito a m’kachisi, pamalo paja Kasifiya, kuti azibwera nao kwa ife otumikira za nyumba ya Mulungu wathu.

18 Ndipo monga munatikhalira dzanja lokoma la Mulungu wathu, anatitengera munthu wanzeru wa ana a Mali, mwana wa Levi, mwana wa Israele; ndi Serebiya, pamodzi ndi ana ake ndi abale ake khumi mphambu asanu ndi atatu;

19 ndi Hasabiya, ndi pamodzi naye Yesaya wa ana a Merari, abale ake ndi ana ao makumi awiri;

20 ndi antchito a m’kachisi, amene Davide ndi akalonga adapereka atumikire Alevi, antchito a m’kachisi mazana awiri mphambu makumi awiri, onsewo otchulidwa maina.

21 Pamenepo ndinalalikira chosala komweko kumtsinje wa Ahava, kuti tidzichepetse pamaso pa Mulungu wathu, kumfunsa ationetsere njira yolunjika ya kwa ife, ndi ang’ono athu, ndi chuma chathu chonse.

22 Pakuti ndinachita manyazi kupempha kwa mfumu gulu la asilikali, ndi apakavalo, kutithandiza pa adani panjira; popeza tidalankhula ndi mfumu kuti, Dzanja la Mulungu wathu likhalira mokoma onse akumfuna; koma mphamvu yake ndi mkwiyo wake zitsutsana nao onse akumsiya.

23 Momwemo tinasala ndi kupempha ichi kwa Mulungu wathu; nativomereza Iye.

24 Pamenepo ndinapatula akulu a ansembe khumi ndi awiri, ndiwo Serebiya, Hasabiya, ndi abale ao khumi pamodzi nao,

25 ndi kuwayeserasiliva, ndi golide, ndi zipangizo, ndizo chopereka cha kwa nyumba ya Mulungu wathu, chimene mfumu, ndi aphungu ake, ndi akalonga ake, ndi Aisraele onse anali apawa, adapereka.

26 Ndipo ndinawayesera m’dzanja mwao matalente a siliva mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu, ndi zipangizo zasiliva matalente zana limodzi,

27 ndi zikho zagolide makumi awiri za madariki chikwi chimodzi, ndi zipangizo ziwiri za mkuwa wabwino wonyezimira wokhumbika ngati golide.

28 Ndipo ndinanena nao, Inu ndinu opatulikira Yehova, ndi zipangizozo nzopatulikira, ndi siliva ndi golide, ndizo chopereka chaufulu cha kwa Yehova Mulungu wa makolo anu.

29 Mukhale maso ndi kuzisunga mpaka muziyesera pamaso pa ansembe aakulu ndi Alevi, ndi akulu a nyumba za makolo a Israele kuYerusalemu, m’zipinda za nyumba ya Yehova.

30 Potero ansembe ndi Alevi analandira kulemera kwake kwa siliva ndi golide ndi zipangizo, abwere nazo ku Yerusalemu kunyumba ya Mulungu wathu.

31 Pamenepo tinachoka ku mtsinje wa Ahava tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, kunka ku Yerusalemu; ndipo dzanja la Mulungu wathu linakhala pa ife, ndi kutilanditsa m’dzanja la mdani ndi wolalira m’njira.

32 Ndipo tinafika ku Yerusalemu ndi kukhalako masiku atatu.

33 Ndipo pa tsiku lachinai siliva ndi golide ndi zipangizo zinayesedwa m’nyumba ya Mulungu wathu, m’dzanja la Meremoti mwana wa Uriya wansembe, ndi pamodzi naye Eleazara mwana wa Finehasi, ndi pamodzi nao Yozabadi mwana wa Yesuwa, ndi Nowadiya mwana wa Binuyi, Alevi;

34 zonsezi anaziwerenga ndi kuziyesa; ndi kulemera kwake konse kunalembedwa nthawi yomweyo.

35 Otengedwa ndende, atatuluka m’ndende, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israele, ng’ombe khumi ndi ziwiri za Aisraele onse, nkhosa zamphongo makumi asanu ndi anai mphambu zisanu ndi imodzi, anaankhosa makumi asanu ndi awiri mphambu asanu ndi awiri, atonde khumi ndi awiri, akhale nsembe yazolakwa; zonsezi ndizo nsembe yopsereza ya kwa Yehova.

36 Ndipo napereka malamulo a mfumu kwa akazembe a mfumu, ndi kwa ziwanga, tsidya lino la mtsinjewo; ndipo iwo anathandiza anthu ndi nyumba ya Mulungu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZR/8-21896ee61cfeea48a89c0f6bcf80a020.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *