Categories
ESTERE

ESTERE 9

Ayuda awapha adani ao

1 Mwezi wakhumi ndi chiwiri tsono, ndiwo mwezi wa Adara, tsiku lake lakhumi ndi chitatu, mau a mfumu ndi lamulo lake ali pafupi kuchitika, tsikuli adani a Ayuda anayesa kuwachitira ufumu, koma chinasinthika; popeza Ayuda anachitira ufumu iwo odana nao;

2 pakuti Ayuda anasonkhana pamodzi m’mizinda mwao, m’maiko onse a mfumu Ahasuwero, kuwathira manja ofuna kuwachitira choipa, ndipo palibe munthu analimbika pamaso pao; popeza kuopsa kwao kudawagwera mitundu yonse ya anthu.

3 Ndipo akalonga onse a maikowo, ndi akazembe, ndi ziwanga, ndi iwo ochita ntchito ya mfumu, anathandiza Ayuda; popeza kuopsa kwa Mordekai kudawagwera.

4 Pakuti Mordekai anali wamkulu m’nyumba ya mfumu, ndi mbiri yake idabuka m’maiko onse; pakuti munthuyu Mordekai anakulakulabe.

5 Ndipo Ayuda anakantha adani ao onse, kuwakantha ndi lupanga, ndi kuwapulula, nachitira odana nao monga anafuna.

6 Ndipo m’chinyumba cha ku Susa Ayuda anakantha, naononga amuna mazana asanu.

7 Napha Parasadata, ndi Dalifoni, ndi Asipata,

8 ndi Porata, ndi Adaliya, ndi Aridata,

9 ndi Parimasta, ndi Arisai, ndi Aridai, ndi Vaizata,

10 ana aamuna khumi a Hamani mwana wa Hamedata, mdani wa Ayuda. Koma sanalande zofunkha.

11 Tsiku lomwelo anabwera nacho kwa mfumu chiwerengo cha iwo ophedwa m’chinyumba cha ku Susa.

12 Ndipo mfumu inati kwa mkazi wamkulu Estere, Ayuda adapha, naononga amuna mazana asanu m’chinyumba cha ku Susa, ndi ana aamuna khumi a Hamani; nanga m’maiko ena a mfumu munachitikanji? Pempho lanu ndi chiyani tsono? Lidzachitikira inu; kapena mufunanjinso? Kudzachitika.

13 Nati Estere, Chikakomera mfumu, alole Ayuda okhala mu Susa achite ndi mawa lomwe monga mwa lamulo la lero; ndi ana aamuna khumi a Hamani apachikidwe pamtengo.

14 Ndipo mfumu inati azichita motero, nalamulira mu Susa, napachikidwa ana aamuna khumi a Hamani.

15 Ndipo Ayuda okhala mu Susa anasonkhana pamodzi, tsiku lakhumi ndi chinai la mwezi wa Adara, napha amuna mazana atatu mu Susa; koma sanalande zofunkha.

16 Nasonkhana pamodzi Ayuda ena okhala m’maiko a mfumu, nalimbikira moyo wao, napumula pa adani ao, nawapha a iwo odana nao zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu zisanu; koma sanalande zofunkha.

17 Chinachitika ichi tsiku lakhumi ndi chitatu la mwezi wa Adara, ndi tsiku lake lakhumi ndi chinai anapumula, naliyesa tsiku lamadyerero ndi lakukondwera.

18 Koma Ayuda okhala mu Susa anasonkhana tsiku lakhumi ndi chitatu ndi lakhumi ndi chinai, ndi pa tsiku lakhumi ndi chisanu anapumula, naliyesa tsiku lamadyerero ndi lakukondwera.

19 Chifukwa chake Ayuda a kumidzi, okhala m’mizinda yopanda malinga, amaliyesa tsiku lakhumi ndi chinai la mwezi wa Adara tsiku la kukondwera ndi madyerero, ndi tsiku lokoma, ndi lakutumizirana magawo.

Masungidwe a tsiku la Purimu

20 Ndipo Mordekai analembera izi, natumiza makalata kwa Ayuda onse okhala m’maiko onse a mfumu Ahasuwero, a kufupi ndi a kutali,

21 kuwalimbikitsira, asunge tsiku lakhumi ndi chinai, mwezi wa Adara, ndi tsiku lake lakhumi ndi chisanu lomwe, chaka ndi chaka,

22 ndiwo masiku amene Ayuda anapumula pa adani ao; ndi mwezi wachisoni unawasandulikira wakukondwera, ndi wamaliro ukhale tsiku lokoma, awayese masiku amadyerero ndi akukondwera, akutumizirana magawo, ndi akupatsa zaufulu kwa osauka.

23 Ndipo Ayuda anavomereza kuchita monga umo adayambira, ndi umo Mordekai adawalembera;

24 popeza Hamani mwana wa Hamedata wa ku Agagi, mdani wa Ayuda onse, adapangira Ayuda chiwembu kuwaononga, naombeza Puri, ndiwo ula, kuwatha ndi kuwaononga;

25 koma pofika mlanduwo kwa mfumu, iye adalamula polemba kalata kuti chiwembu choipa cha Hamani adachipangira Ayuda chimbwerere mwini; ndi kuti iye ndi ana ake aamuna apachikidwe pamtengo.

26 Chifukwa chake anatcha masikuwaPurimu, ndilo dzina la ulawo. Momwemo, chifukwa cha mau onse a kalatayo, ndi izi adaziona za mlanduwo, ndi ichi chidawadzera,

27 Ayuda anakhazikitsa ichi, nadzilonjezetsa okha, ndi mbeu yao, ndi onse akuphatikana nao, chingalekeke, kuti adzasunga masiku awa awiri monga mwalembedwa, ndi monga mwa nyengo yao yoikika, chaka ndi chaka;

28 ndi kuti masikuwa adzakumbukika ndi kusungika mwa mibadwo yonse, banja lililonse, dziko lililonse, ndi mzinda uliwonse; ndi kuti masiku awa sadzalekeka mwa Ayuda, kapena kusiyidwa chikumbukiro chao mwa mbeu yao.

29 Pamenepo Estere mkazi wamkulu mwana wa Abihaili, ndi Mordekai Myuda, analembera molamulira, kukhazikitsa kalata iyi yachiwiri ya Purimu.

30 Natumiza iye makalata kwa Ayuda onse, kumaiko zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi awiri a ufumu wa Ahasuwero, ndiwo mau a mtendere ndi choonadi;

31 kukhazikitsa masiku awa a Purimu m’nyengo zao, m’mene Mordekai Myuda ndi mkazi wamkulu Estere adawakhazikitsira; ndi umo anadzikhazikitsira okha, ndi mbeu yao, kunena za kusala kwao, ndi kufuula kwao.

32 Ndipo kunena kwake kwa Estere kunakhazikitsa mau awa a Purimu; ndipo kunalembedwa m’buku.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EST/9-0405c021758e9aec8ee5ce6d062431b6.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *