Categories
YOBU

YOBU 1

Yobu wosautsidwabe alimbika kutama Mulungu

1 Panali munthu m’dziko la Uzi, dzina lake ndiye Yobu; ndipo munthuyu anali wangwiro ndi woongoka, wakuopa Mulungu ndi kupewa zoipa.

2 Ndipo anabala ana aamuna asanu ndi awiri, ndi ana aakazi atatu.

3 Zoweta zakenso zinali nkhosa zikwi zisanu ndi ziwiri, ndingamirazikwi zitatu, ndi ng’ombe zamagoli mazana asanu, ndi abulu aakazi mazana asanu, antchito ake omwe ndi ambiri; chotero munthuyu anaposa anthu onse a kum’mawa.

4 Ndipo ana ake aamuna anamuka kukachita madyerero m’nyumba ya yense pa tsiku lake; natumiza mthenga kuitana alongo ao atatu adzadye nadzamwe nao.

5 Ndipo kunatero, atatha masiku a madyererowa Yobu anatumiza mau, nawapatula, nauka mamawa, nafukiza nsembe zopsereza, monga mwa kuwerenga kwa iwo onse; pakuti Yobu anati, Kapena anachimwa ana anga, nachitira Mulungu mwano m’mtima mwao, Anatero Yobu masiku onse.

6 Ndipo panali tsiku lakuti ana a Mulungu anadza kudzionetsa kwa Yehova, nadzansoSatanapakati pao.

7 Nati Yehova kwa Satana, Ufuma kuti? Nayankha Satana kwa Yehova, nati, Kupitapita m’dziko ndi kuyendayenda m’mwemo.

8 Ndipo Yehova anati kwa Satana, Kodi waonerera mtumiki wanga Yobu? Pakuti palibe wina wonga iye m’dzikomo, munthu wangwiro ndi woongoka, wakuopa Mulungu ndi kupewa zoipa.

9 Nayankha Satana, nati kwa Yehova, Kodi Yobu aopa Mulungu pachabe?

10 Kodi simunamtchinge iye ndi nyumba yake, ndi zake zonse, pomzinga ponse? Ntchito ya manja ake mwaidalitsa, ndi zoweta zake zachuluka m’dziko.

11 Koma mutambasule dzanja lanu ndi kumkhudzira zake zonse, ndipo adzakuchitirani mwano pamaso panu.

12 Nati Yehova kwa Satana, Taona, zonse ali nazo zikhale m’dzanja mwako; pa iye pokha usatambasula dzanja lako. Natuluka Satana pamaso pa Yehova.

13 Tsono panali tsiku loti ana ake aamuna ndi aakazi analinkudya ndi kumwa vinyo m’nyumba ya mkulu wao;

14 nafika mthenga kwa Yobu, nati, Ng’ombe zinalikulima, ndi abulu aakazi analikudya pambali pao;

15 koma anazigwera Aseba, nazitenga, nawapha anyamata ndi lupanga lakuthwa, ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

16 Akali chilankhulire uyu, anadza winanso, nati, Wagwa moto wa Mulungu wochokera kumwamba, wapsereza nkhosa ndi anyamata, nuzinyeketsa; ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

17 Akali chilankhulire uyu, anadza winanso, nati, Ababiloni anadzigawa magulu atatu, nazigwera ngamira, nazitenga, nawapha anyamata ndi lupanga lakuthwa, ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

18 Akali chilankhulire, anadza winanso, nati, Ana anu aamuna ndi aakazi analinkudya ndi kumwa vinyo m’nyumba ya mkulu wao;

19 ndipo taonani, inadza mphepo yaikulu yochokera kuchipululu, niomba pangodya zonse zinai za nyumbayo, nigwa pa anyamatawo, nafa; ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

20 Pamenepo Yobu ananyamuka, nang’amba malaya ake, nameta mutu wake, nagwa pansi, nalambira,

21 nati, Ndinatuluka m’mimba ya mai wanga wamaliseche, wamaliseche ndidzamukanso; Yehova anapatsa, Yehova watenga, lidalitsike dzina la Yehova.

22 Mwa ichi chonse Yobu sanachimwe, kapena kunenera Mulungu cholakwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/1-39622e1b07c595d70d8d6edbd856ff10.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *