Categories
YOBU

YOBU 2

1 Panalinso tsiku lakuti anadza ana a Mulungu kudzionetsa kwa Yehova, nadzaSatanayemwe pakati pao kudzionetsa kwa Yehova.

2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, Ufuma kuti? Nayankha Satana, nati kwa Yehova, Kupitapita m’dziko, ndi kuyendayenda m’mwemo.

3 Ndipo Yehova anati kwa Satana, Kodi waonerera mtumiki wanga Yobu? Pakuti palibe wina wonga iye m’dzikomo, munthu wangwiro ndi woongoka, wakuopa Mulungu, ndi kupewa zoipa; naumirirabe kukhala wangwiro, chinkana undisonkhezera ndimuononge kopanda chifukwa.

4 Nayankha Satana, nati kwa Yehova, Khungu kulipa khungu, inde munthu adzapereka zonse ali nazo kuombola moyo wake.

5 Koma tambasulani dzanja lanu, ndi kukhudza fupa lake ndi mnofu wake, ndipo adzakuchitirani mwano pamaso panu.

6 Ndipo Yehova anati kwa Satana, Taona, akhale m’dzanja lako; moyo wake wokha uuleke.

7 Natuluka Satana pamaso pa Yehova, nazunza Yobu ndi zilonda zowawa, kuyambira kuphazi lake kufikira pakati pamutu pake.

8 Ndipo anadzitengera phale, kudzikanda nalo; nakhala pansi m’maphulusa.

9 Pamenepo mkazi wake ananena naye, Kodi uumiriranso kukhala wangwiro? Chitira Mulungu mwano, ufe.

10 Koma ananena naye, Ulankhula monga amalankhula akazi opusa. Ha! Tidzalandira zokoma kwa Mulungu kodi, osalandiranso zoipa? Pa ichi chonse Yobu sanachimwe ndi milomo yake.

Mabwenzi ake atatu adzacheza naye

11 Atamva tsono mabwenzi atatu a Yobu za choipa ichi chonse chidamgwera, anadza, yense kuchokera kwao, Elifazi wa ku Temani, ndi Bilidadi Msuki, ndi Zofari wa ku Naama, napangana kudzafika kumlirira ndi kumsangalatsa.

12 Ndipo pokweza maso ao ali kutali, sanamdziwe, nakweza mau ao, nalira; nang’amba yense malaya ake, nawaza fumbi kumwamba ligwe pamitu pao.

13 Nakhala pansi pamodzi naye panthaka masiku asanu ndi awiri usana ndi usiku, palibe mmodzi ananena naye kanthu, popeza anaona kuti kuwawaku nkwakukulu ndithu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/2-7862c23242b46a078b9b4cba4e23b540.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *