Categories
YOBU

YOBU 3

Madandaulo a Yobu

1 Atatero, Yobu anatsegula pakamwa pake, natemberera tsiku lake.

2 Nalankhula Yobu nati,

3 Litayike tsiku lobadwa ine,

ndi usikuwo udati, Waima naye mwana wamwamuna.

4 Tsiku lija likhale mdima;

Mulungu asalifunse kumwamba,

ndi kuunika kusaliwalire.

5 Mdima ndi mthunzi wa imfa ziliyese laolao;

mtambo ulikhalire;

zonse zodetsa usana bii ziliopse.

6 Usiku uja, mdima weniweni uugwere;

usakondwerere mwa masiku a m’chaka;

usalowe m’chiwerengedwe cha miyezi.

7 Ha! Usiku uja ukhale chumba;

kuimbira kokondwera kusalowe m’mwemo.

8 Autemberere iwo akutemberera usana,

Odziwa kuutsaLeviyatani.

9 Nyenyezi za chizirezire zide;

uyembekezere kuunika, koma kuusowe;

usaone kephenyuka kwa mbandakucha;

10 popeza sunatseke pa makomo ake mimba ya mai wanga.

Kapena kundibisira mavuto pamaso panga.

11 Ndinalekeranji kufera m’mimba?

Ndi kupereka mzimu wanga pobadwa ine.

12 Anandilandiriranji maondo?

Kapena mawere kuti ndiyamwe?

13 Pakuti ndikadagona pansi pomwepo ndi kukhala chete;

ndikanagona tulo; pamenepo ndikadaona popumula;

14 pamodzi ndi mafumu ndi maphungu a padziko,

akudzimangira m’mabwinja;

15 kapena pamodzi ndi akalonga eni ake a golide,

odzaza nyumba zao ndisiliva;

16 Kapena ngati nsenye yobisika ndikadakhala kuli zii;

ngati makanda osaona kuunika.

17 Apo oipa aleka kumavuta;

ndi apo ofooka mphamvu akhala m’kupumula.

18 Apo a m’kaidi apumula pamodzi,

osamva mau a wofulumiza wao.

19 Ang’ono ndi akulu ali komwe;

ndi kapolo amasuka kwa mbuyake.

20 Amninkhiranji kuunika wovutika,

ndi moyo kwa iye wakuwawa mtima,

21 wakuyembekezera imfa, koma kuli zii,

ndi kuikumba koposa chuma chobisika,

22 wakusekerera ndi chimwemwe

ndi kukondwera pakupeza manda?

23 Amuonetseranji kuunika munthu wa njira yobisika,

amene wamtsekera Mulungu?

24 Pakuti ndikati ndidye, kumadza kuusa moyo kwanga;

ndi kudzuma kwanga kumathiridwa ngati madzi.

25 Pakuti chimene ndinachiopa chandigwera,

ndi chimene ndachita nacho mantha chandidzera.

26 Wosakhazikika, ndi wosakhala chete, ndi wosapumula ine,

koma mavuto anandidzera.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/3-6202c66f3a581cf16dd9267fbbf35907.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *