Categories
YOBU

YOBU 4

Elifazi adzudzula Yobu

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,

2 Munthu akayesa kunena nawe mau,

kodi udzamva nao chisoni?

Koma akhoza ndani kudziletsa kunena?

3 Taona iwe walangiza aunyinji,

walimbitsa manja a ofooka.

4 Mau ako anachirikiza iye amene akadagwa,

walimbitsanso maondo otewa.

5 Koma tsopano chakufikira iwe, ndipo ukomoka;

chikukhudza, ndipo uvutika.

6 Kodi kulimbika mtima kwako si ndiko kuti uopa Mulungu,

ndi chiyembekezo chako si ndiwo ungwiro wa njira zako?

7 Takumbukira tsopano, watayika ndani wosapalamula konse?

Kapena oongoka mtima alikhidwa kuti?

8 Monga umo, ndaonera, olimira mphulupulu,

nabzala vuto, akololapo zomwezo.

9 Atayika ndi mpweya wa Mulungu,

nathedwa ndi mpumo wa mkwiyo wake.

10 Kubangula kwa mkango,

ndi kulira kwa mkango waukali kwaletsedwa,

ndi mano a misona ya mkango athyoledwa.

11 Mkango wokalamba udzifera posowa mkoka,

ndi misona ya mkango waukazi imwazika.

12 Anditengera mau m’tseri,

m’khutu mwanga ndinalandira kunong’oneza kwake.

13 M’malingaliro a masomphenya a usiku,

powagwira anthu tulo tatikulu

14 Anandidzera mantha ndi kunjenjemera,

nanthunthumira nako mafupa anga onse.

15 Pamenepo panapita mzimu pamaso panga;

tsitsi la thupi langa lidati nyaunyau.

16 Unaima chilili, koma sindinathe kuzindikira maonekedwe ake;

panali mzukwa pamaso panga;

kunali chete, ndipo ndidamva mau akuti,

17 Kodi munthu adzakhala wolungama ndi kuposa Mulungu?

Kodi munthu adzakhala woyera woposa Mlengi wake?

18 Taona, sakhulupirira atumiki ake;

nawanenera amithenga ake zopusa;

19 kopambana kotani nanga iwo akukhala m’nyumba zadothi,

amene kuzika kwao kuli m’fumbi,

angothudzulidwa ngati njenjete.

20 Kuyambira m’mawa kufikira madzulo athudzuka;

aonongeka kosatha, osasamalirako munthu.

21 Kukometsetsa kwao sikumachotsedwa nao?

Amafa koma opanda nzeru.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/4-c4008d5cfe7524034f6cf5fb55f3f00e.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *