Categories
YOBU

YOBU 16

Yobu atonza mabwenziwo kuti mau ao samthandiza, akana kuti sanachimwe, nadziponya kwa Mulungu. Chiyembekezo chake ndi imfa

1 Pamenepo Yobu anayankha, nati,

2 Ndamva zambiri zotere;

inu nonse ndinu otonthoza mtima mondilemetsa.

3 Kodi adzatha mau ouluzika?

Kapena chikuwindula nchiyani kuti uyankha zotere?

4 Inenso ndikadanena monga inu,

moyo wanu ukadakhala m’malo mwa moyo wanga,

ndikadalumikizanitsa mau akutsutsana nanu,

ndi kukupukusirani mutu wanga.

5 Koma ndikadakulimbikitsani ndi m’kamwa mwanga,

ndi chitonthozo cha milomo yanga chikadatsitsa chisoni chanu.

6 Chinkana ndinena chisoni changa sichitsika;

ndipo ndikaleka, chindichokera nchiyani?

7 Koma tsopano wandilemetsa Iye;

mwapasula msonkhano wanga wonse.

8 Kundigwira kwanu, ndiko umboni wonditsutsa,

kuonda kwanga kundiukira, kuchita umboni pamaso panga.

9 Iye ananding’amba m’kundida kwake, nakwiya nane,

anandikukutira mano;

mdani wanga ananditong’olera maso ake.

10 Iwo anandiyasamira pakamwa pao;

anandiomba pama ndi kunditonza;

asonkhana pamodzi kunditsutsa.

11 Mulungu andipereka kwa osulangama,

nandiponya m’manja a oipa.

12 Ndinali mkupuma, koma anandithyola;

inde anandigwira pakhosi, nandiphwanya;

nandiimika ndikhale chandamali.

13 Eni mauta ake andizinga,

ang’amba impso zanga, osazileka;

natsanulira pansi ndulu yanga.

14 Andipasulapasula;

andithamangira ngati wamphamvu.

15 Ndadzisokerera chiguduli kukhungu langa.

Ndipo ndaipsa mphamvu yanga m’fumbi.

16 Nkhope yanga njodetsedwa ndi kulira misozi,

ndi pa zikope zanga pali mthunzi wa imfa;

17 pangakhale palibe chiwawa m’manja mwanga,

ndi pemphero langa ndi loyera.

18 Dziko iwe, usakwirire mwazi wanga,

ndi kulira kwanga kusowe popumira.

19 Tsopanonso, taona, mboni yanga ili kumwamba,

ndi nkhoswe yanga ikhala m’mwamba.

20 Mabwenzi anga andinyoza;

koma diso langa lilirira misozi kwa Mulungu.

21 Ha? Munthu akadapembedzera mnzake kwa Mulungu,

monga munthu apembedzera mnansi wake!

22 Pakuti zitafika zaka zowerengeka,

ndidzamuka kunjira imene sindibwererako.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/16-f78bde1bc7b47e1c85e13075d13dd839.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *