Categories
YOBU

YOBU 17

1 Mzimu wanga watha, masiku anga afafanizika,

kumanda kwandikonzekeratu.

2 Zoonadi, ali nane ondiseka;

ndi diso langa lili chipenyere m’kundiwindula kwao.

3 Mupatse chigwiriro tsono,

mundikhalire chikole Inu nokha kwanu;

ndani adzapangana nane kundilipirira?

4 Pakuti mwabisira mtima wao nzeru;

chifukwa chake simudzawakuza.

5 Iye wakupereka mabwenzi ake ku ukapolo,

m’maso mwa ana ake mudzada.

6 Anandiyesanso chitonzo cha anthu;

ndipo ndakhala ngati munthu womthira malovu pankhope pake.

7 M’diso mwanga muchita chizirezire chifukwa cha chisoni,

ndi ziwalo zanga zonse zilibe chithunzi.

8 Anthu oongoka mtima adzadabwa nacho,

ndi munthu wosalakwa adzadziutsa kumtsutsa wonyoza Mulunguyo.

9 Koma wolungama asungitsa njira yake,

ndi iye wa manja oyera adzakulabe mumphamvu.

10 Koma bwerani inu nonse, idzani tsono;

pakuti sindipeza mwa inu wanzeru.

11 Masiku anga apitirira, zolingirira zanga zaduka,

zakezake zomwe za mtima wanga.

12 Zisanduliza usiku ukhale usana;

kuunika kuyandikana ndi mdima.

13 Ndikayembekezera kumanda kukhale nyumba yanga;

ndikayala pogona panga mumdima.

14 Ndikati kwa dzenje, Ndiwe atate wanga;

kwa mphutsi, Ndiwe mai wanga ndi mlongo wanga;

15 chilikuti chiyembekezo changa?

Inde, chiyembekezo changa adzachiona ndani?

16 Chidzatsikira kumipingiridzo ya kumanda,

pamene tipumulira pamodzi kufumbi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/17-b338533e7f587ecaf82cea33fff5c062.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *