Categories
YOBU

YOBU 21

Yobu ayankha kuti oipa ambiri amalemerera. Zooneka m’maso sizitiuza za mtima wa Mulungu

1 Pamenepo Yobu anayankha, nati,

2 Mvetsetsani mau anga;

ndi ichi chikhale chitonthozo chanu.

3 Mundilole, ndinene nanenso;

ndipo nditanena ine, sekani.

4 Kodi ine, kudandaula kwanga, ndidandaulira munthu?

Ndipo ndilekerenji kupsa mtima?

5 Ndiyang’anireni, nimusumwe,

gwirani pakamwa panu.

6 Ndikangokumbukira ndivutika mtima,

ndi thupi langa lichita nyaunyau.

7 Oipa akhaliranji ndi moyo,

nakalamba, nalemera kwakukulu?

8 Mbeu zao zikhazikika pamodzi nao pankhope pao,

ndi ana ao pamaso pao.

9 Nyumba zao sizitekeseka ndi mantha,

ngakhale ndodo ya Mulungu siiwakhalira.

10 Ng’ombe yao yamphongo imakwera, yosakanika;

ng’ombe yao yaikazi imaswa, yosapoloza.

11 Atulutsa makanda ao ngati gulu,

ndi ana ao amavinavina.

12 Aimbira lingaka ndi zeze,

nakondwera pomveka chitoliro.

13 Atsekereza masiku ao ndi zokoma,

natsikira m’kamphindi kumanda.

14 Koma adati kwa Mulungu, Tichokereni;

pakuti sitifuna kudziwa njira zanu.

15 Wamphamvuyonse ndiye yani kuti timtumikire?

Ndipo tidzapindulanji pakumpemphera Iye?

16 Taonani, zokoma zao sizili m’dzanja lao;

(koma uphungu wa oipa unditalikira.)

17 Ngati nyali za oipa zizimidwa kawirikawiri?

Ngati tsoka lao liwagwera?

Ngati Mulungu awagawira zowawa mu mkwiyo wake?

18 Ngati akunga ziputu zomka ndi mphepo,

ngati mungu wouluzika ndi nkuntho?

19 Mukuti, Mulungu asungira ana ake a munthu choipa chake,

ambwezere munthuyo kuti achidziwe.

20 Aone yekha chionongeko chake m’maso mwake,

namwe mkwiyo wa Wamphamvuyonse.

21 Pakuti chomsamalitsa nyumba yake nchiyani, atapita iye,

chiwerengo cha miyezi yake chitadulidwa pakati?

22 Ngati pali munthu wakumphunzitsa Mulungu nzeru?

Popeza Iye aweruza mlandu iwo okwezeka.

23 Wina akufa, wabiriwiri,

ali chikhalire ndi chipumulire.

24 Mbale zake zidzala ndi mkaka;

ndi wongo wa m’mafupa ake uli momwe.

25 Koma mnzake akufa ali nao mtima wakuwawa,

osalawa chokoma konse.

26 Iwo agona chimodzimodzi kufumbi,

ndi mphutsi ziwakuta.

27 Taonani, ndidziwa maganizo anu,

ndi chiwembu mundilingirira moipa.

28 Pakuti munena, Ili kuti nyumba ya kalonga?

Ndi hema wokhalamo woipa ali kuti?

29 Simunawafunsa kodi opita m’njira?

Ndipo simusamalira zotsimikiza zao?

30 Zakuti munthu woipa asungika tsiku la tsoka?

Natulutsidwa tsiku la mkwiyo?

31 Adzamfotokozera ndani njira yake pamaso pake?

Nadzamlipitsa ndani pa ichi anachichita?

32 Potsiriza pake adzapita naye kumanda,

nadzadikira pamanda pake.

33 Zibuma za kuchigwa zidzamkomera.

Adzakoka anthu onse amtsate,

monga anamtsogolera osawerengeka.

34 Potero munditonthozeranji nazo zopanda pake,

popeza m’mayankho mwanu mutsala mabodza okha?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/21-111450dd7ce8b948d17130bcf97f6156.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *